Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 31:39 - Buku Lopatulika

39 Chimene chinazomoledwa ndi chilombo sindinachitengere kwa iwe; ndekha ndinalipira; padzanja langa unachifuna, chingakhale chobedwa kapena pausiku kapena pausana.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

39 Chimene chinazomoledwa ndi chilombo sindinachitengere kwa iwe; ndekha ndinalipira; pa dzanja langa unachifuna, chingakhale chobedwa kapena pausiku kapena pausana.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

39 Nkhosa ikajiwa ndi zilombo, ine ndinkalipira nthaŵi zonse, sindinkabwera nayo kwa inu, kuwonetsa kuti sindidalakwe. Munkafuna kuti ndilipire chilichonse chobedwa usiku kapena usana.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

39 Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 31:39
9 Mawu Ofanana  

Zaka makumi awiriwo ndakhala nawe, nkhosa ndi mbuzi zako zazikazi sizinapoloze, ndi abira a zoweta zako sindinadye.


Chotero ndinakhala; usana ludzu linakomola ine, usiku chisanu; tulo tanga tinachoka m'maso mwanga.


Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; chifukwa chake musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agalu.


Mlandu uliwonse wa cholakwa, kunena za ng'ombe, za bulu, za nkhosa, za chovala, za kanthu kalikonse kotayika, munthu anenako kali kake; mlandu wa onse awiri ufike kwa oweruza; iye amene oweruza amtsutsa alipe chowirikiza kwa mnansi wake.


Asamadya zakufa zokha, kapena zojiwa, kudzidetsa nazo; Ine ndine Yehova.


Ndipo panali abusa m'dziko lomwelo, okhala kubusa ndi kuyang'anira zoweta zao usiku.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa