Ezara 9:2 - Buku Lopatulika2 Pakuti anadzitengera okha ndi ana aamuna ao ana aakazi ao; nisokonezeka mbeu yopatulika ndi mitundu ya maikowa; inde dzanja la akalonga ndi olamulira linayamba kulakwa kumene. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20142 Pakuti anadzitengera okha ndi ana amuna ao ana akazi ao; nisokonezeka mbeu yopatulika ndi mitundu ya maikowa; inde dzanja la akalonga ndi olamulira linayamba kulakwa kumene. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa2 Aisraele ena ndi ana ao aamuna adayamba kukwatira ana aakazi a anthuwo. Motero mtundu wathu wopatulika wadzisokoneza ndi mitundu ya anthu a m'maikowo. Ndipo atsogoleri ndi akuluakulu ndiwo amene akupambana pa kusakhulupirika kumeneku.” Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero2 Zomwe zikuchitika ndi izi. Aisraeli ena ndi ana awo aamuna anayamba kukwatira ana aakazi a anthuwa. Choncho mtundu wopatulika wadzisokoneza ndi mitundu ya anthu a mʼderali. Ndipo atsogoleri ndi akuluakulu ndiwo akupambana pa makhalidwe osakhulupirikawa.” Onani mutuwo |