Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Ezara 4:10 - Buku Lopatulika

10 ndi amitundu otsala amene, Osinapara wamkulu ndi womveka adawatenga mikoli, nawakhalitsa m'mizinda ya Samariya, ndi m'dziko lotsala tsidya lino la mtsinje wa Yufurate.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 ndi amitundu otsala amene, Osinapara wamkulu ndi womveka adawatenga mikoli, nawakhalitsa m'mudzi wa Samariya, ndi m'dziko lotsala tsidya lino la mtsinje wa Yufurate.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Enanso ndi mitundu ina imene Osinapara, wamkulu ndi womveka uja, adaisamutsa ndi kuikhazika m'mizinda ya Samariya ndi kwinanso m'madera a m'chigawo chimene chili Patsidya pa Yufurate.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.

Onani mutuwo Koperani




Ezara 4:10
8 Mawu Ofanana  

Atamva tsono adani a Yuda ndi Benjamini kuti ana aja a ndende analikumangira Yehova Mulungu wa Israele Kachisi,


Zolembedwa m'kalatayo anazitumiza kwa Arita-kisereksesi mfumu: ife akapolo anu, anthu a tsidya lino la mtsinjewo, tikupatsani moni.


Mfumu nibweza mau kwa Rehumu chiwinda cha malamulo, ndi kwa Simisai mlembi, ndi kwa anzao otsala okhala mu Samariya, ndi otsala tsidya lino la mtsinjewo, Moni, ndi nthawi yakuti.


Arita-kisereksesi mfumu ya mafumu kwa Ezara wansembe, mlembi wa lamulo la Mulungu wa Kumwamba, mtendere weniweni, ndi pa nthawi yakuti.


Nanena iye pamaso pa abale ake ndi ankhondo a ku Samariya, nati, Alikuchitanji Ayuda ofookawa? Adzimangire linga kodi? Adzapereka nsembe kodi? Adzatsiriza tsiku limodzi kodi? Adzakometsanso miyala ya ku miunda yotenthedwa?


Ndipo tsono, Mulungu wathu, ndinu Mulungu wamkulu, ndi wamphamvu, ndi woopsa, wakusunga pangano ndi chifundo, asachepe pamaso panu mavuto athu onse amene anatigwera ife, ndi mafumu athu, akulu athu, ndi ansembe athu, ndi aneneri athu, ndi makolo athu, ndi anthu anu onse, kuyambira masiku a mafumu a Asiriya, mpaka lero lino.


Perekani kwa anthu onse mangawa ao; msonkho kwa eni ake a msonkho; kulipira kwa eni ake a kulipidwa; kuopa kwa eni ake a kuwaopa; ulemu kwa eni ake a ulemu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa