Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Estere 4:4 - Buku Lopatulika

4 Ndipo anamwali a Estere ndi adindo ake anadza, namuuza; ndi mkazi wamkulu anawawidwa mtima kwambiri, natumiza chovala aveke Mordekai, ndi kumchotsera chiguduli chake; koma sanachilandire.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Ndipo anamwali a Estere ndi adindo ake anadza, namuuza; ndi mkazi wamkulu anawawidwa mtima kwambiri, natumiza chovala aveke Mordekai, ndi kumchotsera chiguduli chake; koma sanachilandira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.

Onani mutuwo Koperani




Estere 4:4
10 Mawu Ofanana  

Ndipo ana aamuna ake onse ndi ana aakazi onse anauka kuti amtonthoze: koma anakana kutonthozedwa; ndipo anati, Pakuti ndidzatsikira kumanda kwa mwana wanga, ndilinkulirabe. Atate wake ndipo anamlirira.


Koma anakweza maso ake kuzenera, nati, Ali ndi ine ndani? Ndani? Nampenyererako adindo awiri kapena atatu.


Koma Vasiti mkazi wamkuluyo anakana kudza pa mau a mfumu adamuuza adindowo; potero mfumu idapsa mtima ndithu, ndi mkwiyo wake unatentha m'kati mwake.


Ndi m'maiko monse, paliponse anafikapo mau a mfumu ndi lamulo lake, panali maliro aakulu mwa Ayuda, ndi kusala, ndi kulira misozi, ndi kubuma; nagona m'chiguduli ndi mapulusa ambiri.


Pamenepo Estere anaitana Hataki mdindo wina wa mfumu, amene idamuika amtumikire, namuuza amuke kwa Mordekai, kuti adziwe ichi nchiyani ndi chifukwa chake ninji.


Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye. Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka; mtima wanga unakana kutonthozedwa.


Mlendo amene wadziphatika yekha kwa Yehova asanene, kuti, Yehova adzandilekanitsa ndithu ndi anthu ake; pena mfule asanene, Taonani ine ndili mtengo wouma.


Atero Yehova: Mau a amveka mu Rama, maliro ndi kulira kwakuwawa, Rakele alinkulirira ana ake; akana kutonthozedwa mtima pa ana ake, chifukwa palibe iwo.


Ndipo ananyamuka napita; ndipo taona munthu wa ku Etiopiya, mdindo wamphamvu wa Kandake, mfumu yaikazi ya Aetiopiya, ndiye wakusunga chuma chake chonse, amene anadza ku Yerusalemu kudzapemphera;


Ndipo idzatenga limodzi la magawo khumi la mbeu zanu, ndi la minda yanu yampesa, nidzalipatsa akapitao ake, ndi anyamata ake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa