Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 25:33 - Buku Lopatulika

33 Ku mphanda ina kukhale zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa; ndi ku mphanda inzake zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa; zitere mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m'choikaponyalicho.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

33 Ku mphanda ina kukhale zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; ndi ku mphanda inzake zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; zitere mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m'choikapo nyalicho.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

33 Mphanda yoyamba ikhale ndi zikho zitatu zopangidwa ngati maluŵa amtowo, nkhunje ndi duŵa. Ku mphanda ina kukhalenso zikho zitatu zonga maluŵa amtowo, nkhunje ndi duŵa. Zikhale momwemo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zotuluka m'choikaponyalecho.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

33 Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zikhale pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri pakhalenso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zikhale chimodzimodzi ndipo zituluke mʼchoyikapo nyalecho.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 25:33
7 Mawu Ofanana  

pakhale mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m'mwemo; itere ku mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m'choikaponyalicho.


ndipo panali mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zotuluka m'mwemo, inatero pa mphanda zisanu ndi imodzi zochokera m'mwemo.


ndi mitengo iwiri ya azitona pomwepo, wina kudzanja lamanja la mbaleyo, ndi wina kudzanja lake lamanzere.


Kapena sayatsa nyali, ndi kuivundikira m'mbiya, koma aiika iyo pa choikapo chake; ndipo iunikira onse ali m'nyumbamo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa