Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Chivumbulutso 12:2 - Buku Lopatulika

2 ndipo anali ndi pakati; ndipo afuula alimkubala, ndi kumva zowawa zakubala.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 ndipo anali ndi pakati; ndipo afuula alimkubala, ndi kumva zowawa zakubala.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Maiyo anali ndi pathupi, ndipo pa nthaŵi yochira adalira nako mokuwa kupweteka kwa kubala.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala.

Onani mutuwo Koperani




Chivumbulutso 12:2
12 Mawu Ofanana  

Monga ngati mkazi wokhala ndi pakati, amene nthawi yake yakubala yayandikira, amva zopweteka, ndi kufuula m'zowawa zake; momwemo takhala ife pamaso panu, Yehova.


Iye adzaona zotsatira mavuto a moyo wake, nadzakhuta nazo; ndi nzeru zake mtumiki wanga wolungama adzalungamitsa ambiri, nadzanyamula mphulupulu zao.


Imba, iwe wouma, amene sunabale; imba zolimba ndi kufuula zolimba, iwe amene sunabale mwana; pakuti ana a mfedwa achuluka koposa ana a mkazi wokwatibwa ndi mwamuna, ati Yehova.


Mau a phokoso achokera m'mzinda, mau ochokera mu Kachisi, mau a Yehova amene abwezera adani ake chilango.


Tsono ufuulitsa chifukwa ninji? Palibe mfumu mwa iwe kodi? Watayika kodi mu uphungu wako, kuti zowawa zakugwira ngati mkazi wobala?


Chifukwa chake Iye adzawapereka kufikira nthawi yoti wobalayo wabala; pamenepo otsala a abale ake adzabwera pamodzi ndi ana a Israele.


Koma ndizo zonsezi zowawa zoyamba.


Mkazi pamene akuti abale ali nacho chisoni, chifukwa yafika nthawi yake; koma pamene wabala mwana, sakumbukiranso kusaukako, chifukwa cha chimwemwe kuti wabadwa munthu kudziko lapansi.


Tiana tanga, amene ndilikumvanso zowawa za kubala inu, kufikira Khristu aumbika mwa inu,


Pakuti kwalembedwa, Kondwera, chumba iwe wosabala; imba nthungululu, nufuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala; pakuti ana ake a iye ali mbeta achuluka koposa ana a iye ali naye mwamuna.


Ndipo mchira wake uguza limodzi la magawo atatu a nyenyezi zam'mwamba, nuziponya padziko. Ndipo chinjoka chinaimirira pamaso pa mkazi akuti abale, kuti, akabala icho chikalikwire mwana wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa