Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Ahebri 11:29 - Buku Lopatulika

29 Ndi chikhulupiriro anaoloka Nyanja Yofiira kupita ngati pamtunda: ndiko Aejipito poyesanso anamizidwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

29 Ndi chikhulupiriro anaoloka Nyanja Yofiira kupita ngati pamtunda: ndiko Aejipito poyesanso anamizidwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

29 Pokhala ndi chikhulupiriro, Aisraele adaoloka Nyanja Yofiira ngati pamtunda pouma. Koma Aejipito, kuti nawonso ayesere kuwoloka, adamizidwa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

29 Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.

Onani mutuwo Koperani




Ahebri 11:29
14 Mawu Ofanana  

Ndipo munagawanitsa nyanja pamaso pao, napita iwo pakati pa nyanja pouma, ndipo munaponya mozama owalondola, ngati mwala m'madzi olimba.


Anasanduliza nyanja ikhale mtunda. Anaoloka mtsinje choponda pansi, apo tinakondwera mwa Iye.


Anagawa nyanja nawapititsapo; naimitsa madziwo ngati khoma.


Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, chilimikani, ndipo penyani chipulumutso cha Yehova, chimene adzakuchitirani lero; pakuti Aejipito mwawaona lerowa, simudzawaonanso konse.


Ndipo ana a Israele analowa pakati pa nyanja pouma; ndi madziwo anakhala kwa iwo ngati khoma palamanja, ndi palamanzere.


Ndipo Mose anatambasulira dzanja lake kunyanja, ndi nyanja inabwerera m'mayendedwe ake mbandakucha; ndipo Aejipito pothawa anakomana nayo; ndipo Yehova anakutumula Aejipito m'kati mwa nyanja.


Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a mu Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudatuluka mu Ejipito; ndi chija munachitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordani, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa