Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 9:12 - Buku Lopatulika

12 Ndipo mfumu Solomoni anampatsa mfumu yaikazi ya ku Sheba chifuniro chake chonse, chilichonse anachipempha, osawerengera zija adabwera nazo kwa mfumu. Momwemo anabwerera, namuka ku dziko lake, iyeyu ndi anyamata ake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Ndipo mfumu Solomoni anampatsa mfumu yaikazi ya ku Sheba chifuniro chake chonse, chilichonse anachipempha, osawerengera zija adabwera nazo kwa mfumu. Momwemo anabwerera, namuka ku dziko lake, iyeyu ndi anyamata ake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Tsono Solomoni adapatsa mfumukazi ya ku Sheba ija zonse zimene inkafuna ndiponso chilichonse chimene idaapempha, osaŵerengera zimene anali ataipatsa kale posinthana nayo mphatso. Tsono mfumukaziyo idabwerera ku dziko lakwao pamodzi ndi atumiki ake aja.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Mfumu Solomoni inapereka kwa mfumu yayikazi ya ku Seba zonse zimene inazifuna ndi kuzipempha ndipo Solomoni anayipatsa mfumuyo zoposa zimene iyo inabweretsa kwa Solomoni. Ndipo mfumuyo inabwerera ku dziko lake pamodzi ndi atumiki ake.

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 9:12
5 Mawu Ofanana  

Ndipo mfumu Solomoni ananinkha mfumu yaikazi ya ku Sheba chifuniro chake chonse anachipempha iye, osawerenga chimene Solomoni anamninkha mwa ufulu wake. Momwemo iye anabwerera namukanso ku dziko lake, iyeyo ndi anyamata ake.


Ndipo mfumu inasema mitengo yambawa ikhale mizati ya nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi azeze, ndi zisakasa za oimbira; sizinaoneke zotere ndi kale lonse m'dziko la Yuda.


Kulemera kwake tsono kwa golide anafika kwa Solomoni chaka chimodzi ndiko matalente mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi limodzi a golide;


likupatse cha mtima wako, ndipo likwaniritse upo wako wonse.


Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa