Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 8:6 - Buku Lopatulika

6 ndi Baalati, ndi mizinda yonse yosungiramo chuma anali nayo Solomoni, ndi mizinda yonse ya magaleta ake, ndi mizinda ya apakavalo ake, ndi zonse anazifuna Solomoni kuzimanga zomkondweretsa mu Yerusalemu, ndi mu Lebanoni, ndi m'dziko lonse la ufumu wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 ndi Baalati, ndi midzi yonse yosungiramo chuma anali nayo Solomoni, ndi midzi yonse ya magaleta ake, ndi midzi ya apakavalo ake, ndi zonse anazifuna Solomoni kuzimanga zomkondweretsa m'Yerusalemu, ndi m'Lebanoni, ndi m'dziko lonse la ufumu wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Adamanganso Baalati ndiponso mizinda yonse yosungiramo zinthu zimene anali nazo, mizinda yonse yosungiramo magaleta ake, ndi ina yomakhalamo anthu ake okwera pa akavalo, ndi zonse zimene Solomoni adafuna kuti amange ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene Solomoni ankaŵalamulira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 pamodzinso ndi Baalati ndi mizinda yake yonse yosungira chuma, ndiponso mizinda yonse yosungiramo magaleta ake ndi akavalo ndi chilichonse anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 8:6
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi apakavalo; anali nao magaleta chikwi chimodzi mphambu mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri, nawasungira m'mizinda yosungamo magaleta, ndi kwa mfumu mu Yerusalemu.


Anamanganso nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni, m'litali mwake munali mikono zana limodzi, kupingasa kwake mikono makumi asanu, ndi msinkhu wake mikono makumi atatu; naisanja pa mizere inai ya mapanda amkungudza, ndi mitanda yamkungudza, ndi mitanda yamkungudza yotanthalika mapandawo.


Ndipo kunali, atatsiriza Solomoni kumanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi chifuniro chonse cha Solomoni anachikhumbacho,


Ndipo Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi apakavalo, nakhala nao magaleta chikwi chimodzi mphambu mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'mizinda ya magaleta ndi kwa mfumu ku Yerusalemu.


Ndipo Yehosafati anakula chikulire, namanga mu Yuda nyumba zansanja, ndi mizinda ya chuma.


Ndipo anamanga Tadimori m'chipululu, ndi mizinda yonse yosungiramo chuma, imene anaimanga mu Hamati.


Anamanganso Betehoroni wa kumtunda, ndi Betehoroni wa kunsi, mizinda ya malinga yokhala nao malinga, zitseko, ndi mipiringidzo;


Ndipo anthu onse otsala mwa Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, osati Aisraele,


Ndinadzipangira zazikulu; ndinadzimangira nyumba; ndi kuoka mipesa;


Idza nane kuchokera ku Lebanoni, mkwatibwi, kuchokera nane ku Lebanoni: Unguza pamwamba pa Amana, pansonga ya Seniri ndi Heremoni, pa ngaka za mikango, pa mapiri a anyalugwe.


ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa