Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 8:12 - Buku Lopatulika

12 Pamenepo Solomoni anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova paguwa la nsembe la Yehova, limene adalimanga pakhomo pachipinda cholowera,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Pamenepo Solomoni anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa la nsembe la Yehova, limene adalimanga pakhomo pachipinda cholowera,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Kenaka Solomoni adapereka nsembe zopsereza kwa Chauta pa guwa la Chauta limene adalimanga patsogolo pa khonde lapoloŵera,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Solomoni anapereka nsembe zopsereza pa guwa lansembe la Yehova limene anamanga patsogolo pa khonde la polowera,

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 8:12
8 Mawu Ofanana  

ndi mitengo, ndi mbale zowazira, ndi zikho za golide woona, ndi cha mitsuko yake yagolide, woyesedwa kulemera kwake mtsuko uliwonse; ndi cha mitsuko yasiliva woyesedwa kulemera kwake mtsuko uliwonse;


Nakwerako Solomoni ku guwa la nsembe pamaso pa Yehova linali ku chihema chokomanako, napereka pamenepo nsembe zopsereza chikwi chimodzi.


Ndipo pakumva Asa mau awa, ndi chinenero cha Odedi mneneriyo, analimbika mtima, nachotsa zonyansazo m'dziko lonse la Yuda ndi Benjamini, ndi m'mizinda adailanda ku mapiri a Efuremu; nakonza guwa la nsembe la Yehova lokhala pakhomo pachipinda cholowera cha nyumba ya Yehova.


Anapanganso guwa la nsembe lamkuwa, m'litali mwake mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwake mikono makumi awiri, ndi msinkhu wake mikono khumi.


Ndipo udindo wa kalonga ndiwo kupereka nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi nsembe zothira, pachikondwerero, ndi pokhala mwezi, ndi pa masabata; pa zikondwerero zonse zoikika a nyumba ya Israele; ndipo apereke nsembe yauchimo, ndi nsembe yaufa, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zamtendere, kuchitira chotetezera nyumba ya Israele.


Ndipo anadza nane ku bwalo lam'kati la nyumba ya Yehova, ndipo taonani, pa khomo la Kachisi wa Yehova, pakati pa khonde lake ndi guwa la nsembe, panali amuna ngati makumi awiri mphambu asanu akufulatira, ku Kachisi wa Yehova, ndi kuyang'ana kum'mawa, napembedza dzuwa kum'mawa.


Ansembe, atumiki a Yehova, alire pakati pa khonde la pakhomo ndi guwa la nsembe, nanene, Alekeni anthu anu, Yehova, musapereka cholowa chanu achitonze, kuti amitundu awalamulire; adzaneneranji mwa anthu, Ali kuti Mulungu wao?


Ndipo Yesu analikuyendayenda mu Kachisi m'khonde la Solomoni.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa