Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 7:22 - Buku Lopatulika

22 Ndipo adzayankha, Popeza anasiya Yehova Mulungu wa makolo ao amene anawatulutsa m'dziko la Ejipito, nagwira milungu ina, nailambira ndi kuitumikira; chifukwa chake anawagwetsera choipa ichi chonse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

22 Ndipo adzayankha, Popeza anasiya Yehova Mulungu wa makolo ao amene anawatulutsa m'dziko la Ejipito, nagwira milungu ina, nailambira ndi kuitumikira; chifukwa chake anawagwetsera choipa ichi chonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

22 Tsono azidzati, ‘Nchifukwa chakuti anthuwo adasiya Chauta, Mulungu wa makolo ao, amene adaŵatulutsa ku dziko la Ejipito, ndipo adadzifunira milungu ina, namaipembedza ndi kumaitumikira. Nkuwona Chautayo waŵachita zoipa zonsezi.’ ”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

22 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 7:22
10 Mawu Ofanana  

Pakuti Iye anawakweretsera mfumu ya Ababiloni, ndiye anawaphera anyamata ao ndi lupanga, m'nyumba ya malo ao opatulika, osachitira chifundo mnyamata kapena namwali, mkulu kapena nkhalamba; Mulungu anawapereka onse m'dzanja lake.


Ndipo ndidzanena nao za maweruzo anga akuweruzira zoipa zao zonse; popeza anandisiya Ine, nafukizira milungu ina, nagwadira ntchito za manja ao.


Pamenepo uziti kwa iwo, Chifukwa makolo anu anandisiya Ine, ati Yehova, natsata milungu ina, naitumikira, naigwadira, nandisiya Ine, osasunga chilamulo changa;


Koma ngati simudzamva mau amenewa, Ine ndilumbira, pali Ine mwini, ati Yehova, nyumba iyi idzakhala yabwinja.


Ndipo adzakusangalatsani pamene muona njira yao, ndi zochita zao; ndipo mudzadziwa kuti sindinazichite kopanda chifukwa zonse ndinazichita momwemo, ati Ambuye Yehova.


Ndipo anakwaniritsa mau ake adanenawo, kutitsutsa ife ndi oweruza athu otiweruza, ndi kutitengera choipa chachikulu; pakuti pansi pa thambo lonse sipanachitike monga umo panachitikira Yerusalemu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa