Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 32:9 - Buku Lopatulika

9 Pambuyo pake Senakeribu mfumu ya Asiriya, akali ku Lakisi ndi mphamvu yake yonse pamodzi naye, anatuma anyamata kwa Hezekiya mfumu ya Yuda, ndi kwa Ayuda onse okhala ku Yerusalemu, ndi kuti,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Pambuyo pake Senakeribu mfumu ya Asiriya, akali ku Lakisi ndi mphamvu yake yonse pamodzi naye, anatuma anyamata kwa Hezekiya mfumu ya Yuda, ndi kwa Ayuda onse okhala ku Yerusalemu, ndi kuti,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Pambuyo pa zimenezi Senakeribu, mfumu ya ku Asiriya, amene anali atazinga mzinda wa Lakisi pamodzi ndi ankhondo ake onse, adatuma akazembe ake ku Yerusalemu kwa Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi kwa anthu onse a ku Yuda amene anali mu Yerusalemu. Adaŵatuma ndi mau akuti,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 32:9
9 Mawu Ofanana  

Ndipo mfumu ya Asiriya anatuma nduna ndi mkulu wa adindo ndi kazembe ochokera ku Lakisi ndi khamu lalikulu la nkhondo kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Nakwera iwo, nafika ku Yerusalemu. Ndipo atakwera, anafika, naima kumcherenje wa thamanda la kumtunda, ndilo la ku mseu wa ku Malo a Wotsuka Thonje.


ndi Adoraimu, ndi Lakisi, ndi Azeka,


Atero Senakeribu mfumu ya Asiriya, Mutama chiyani kuti mukhala m'linga mu Yerusalemu?


Ndipo mfumu ya Asiriya inatumiza kazembe kuchokera pa Lakisi, kunka ku Yerusalemu, kwa mfumu Hezekiya, ndi nkhondo yambiri. Ndipo iye anaima chifupi ndi mcherenje wa thamanda la kumtunda, m'khwalala la pa mwaniko wa wotsuka nsalu.


Ndipo kazembeyo anabwerera, napeza mfumu ya Asiriya ilikuponyana nkhondo ndi Libina; pakuti anamva kuti inachoka ku Lakisi.


Manga galeta kukavalo waliwiro, wokhala mu Lakisi iwe, woyamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni ndi iye; pakuti zolakwa za Israele zinapezedwa mwa iwe.


Ndipo Yoswa, ndi Aisraele onse naye, anapitirira kuchokera ku Libina kunka ku Lakisi; namanga misasa, nathira nkhondo pa uwo;


mfumu ya ku Yaramuti, imodzi; mfumu ya ku Lakisi, imodzi;


Lakisi ndi Bozikati ndi Egiloni;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa