Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mbiri 17:6 - Buku Lopatulika

6 Ndi mtima wake unakwezeka m'njira za Yehova; anachotsanso misanje ndi zifanizo mu Yuda.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndi mtima wake unakwezeka m'njira za Yehova; anachotsanso misanje ndi zifanizo m'Yuda.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Iyeyo adalimba mtima pa zinthu za Chauta. Kuwonjezera pamenepo, adathetsa akachisi ndiponso mafano a Aserimu ku Yuda.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.

Onani mutuwo Koperani




2 Mbiri 17:6
16 Mawu Ofanana  

Ndipo anayenda m'njira yonse ya atate wake Asa, osapatukamo; nachita choyenera pamaso pa Yehova, koma misanje sanaichotse; anthu anapherabe nsembe, nafukiza zonunkhira pamsanje.


Ndipo Asa anachita chokoma ndi choyenera m'maso mwa Yehova Mulungu wake,


nachotsa maguwa a nsembe achilendo, ndi misanje; naphwanya zoimiritsa zao, nalikha zifanizo zao,


Chinkana misanje siinachotsedwe mu Israele, mtima wa Asa unali wangwiro masiku ake onse.


Koma zapezeka zokoma mwa inu, popeza mwazichotsa zifanizo m'dzikomo, mwalunjikitsanso mtima wanu kufuna Mulungu.


Komatu misanje siinachotsedwe; popeza pamenepo anthu sadakonzere mitima yao kwa Mulungu wa makolo ao.


Chitatha ichi chonse tsono, Aisraele onse opezekako anatuluka kunka kumizinda ya Yuda, naphwanya zoimiritsa, nalikha zifanizo, nagamula misanje ndi maguwa a nsembe mu Yuda monse, ndi mu Benjamini, mu Efuremunso, ndi mu Manase, mpaka adaziononga zonse. Pamenepo ana onse a Israele anabwerera, yense kudziko lake ndi kumizinda yao.


Pakuti pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuyonse, ndi kuweramutsa nkhope yako kwa Mulungu.


Odala angwiro m'mayendedwe ao, akuyenda m'chilamulo cha Yehova.


Ndipo adzaimbira njira za Yehova; pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.


koma mupasule maguwa a nsembe ao, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kulikha zifanizo zao;


Wanzeru ndani, kuti azindikire izi? Waluntha, kuti adziwe izi? Pakuti njira za Yehova zili zoongoka; ndipo olungama adzayendamo, koma olakwa adzagwamo.


nati, Wodzala ndi chinyengo chonse ndi chenjerero lonse, iwe, mwana wa mdierekezi, mdani wa chilungamo chonse, kodi sudzaleka kuipsa njira zolunjika za Ambuye?


Popeza simunatumikire Yehova Mulungu wanu ndi chimwemwe ndi mokondwera mtima, chifukwa cha kuchuluka zinthu zonse;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa