Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mafumu 4:20 - Buku Lopatulika

20 Namnyamula, napita naye kwa amake. Ndipo anakhala pa maondo ake kufikira usana, namwalira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Namnyamula, napita naye kwa amake. Ndipo anakhala pa maondo ake kufikira usana, namwalira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Adamunyamula, nakampereka kwa mai wake. Mwanayo adakhala pamiyendo pa mai wake mpaka masana, basi nkumwalira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.

Onani mutuwo Koperani




2 Mafumu 4:20
14 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Tengatu mwana wako, wamwamuna wayekhayo, Isaki, amene ukondana naye, numuke ku dziko la Moriya; numpereke iye kumeneko nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri lomwe ndidzakuuza iwe.


Koma Israele anamkonda Yosefe koposa ana ake onse, pakuti anali mwana wa ukalamba wake; ndipo anamsokera iye malaya amwinjiro.


Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ake; ndipo anamuda iye koposa.


Ndipo kunali, zitatha izi, mwana wa mkazi mwini nyumbayo anadwala; ndipo pokula nthenda yake, analeka kupuma.


Nati kwa atate wake, Mutu wanga, mutu wanga! Pamenepo anati kwa mnyamata, Umnyamule umuke naye kwa amake.


Ndipo anakwera, namgoneka pa kama wa munthu wa Mulungu, natuluka, namtsekera.


Kodi mkazi angaiwale mwana wake wa pabere, kuti iye sangachitire chifundo mwana wombala iye? Inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.


Monga munthu amene amake amtonthoza mtima, momwemo ndidzatonthoza mtima wanu; ndipo mudzatonthozedwa mtima mu Yerusalemu.


eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m'mitima yambiri akaululidwe.


Ndipo pamene anayandikira kuchipata cha mzindawo, onani, anthu analikunyamula munthu wakufa, mwana wamwamuna mmodzi yekha, amake ndiye mkazi wamasiye; ndipo anthu ambiri amumzinda anali pamodzi naye.


Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.


Pamenepo alongo ake anatumiza kwa Iye, nanena, Ambuye, onani, amene mumkonda adwala.


Koma Yesu anakonda Marita, ndi mbale wake, ndi Lazaro.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa