Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Mafumu 3:7 - Buku Lopatulika

7 Nakatumiza mau kwa Yehosafati mfumu ya Yuda, ndi kuti, Mfumu ya Mowabu wapandukana ndi ine; kodi udzamuka nane kukathira nkhondo pa Mowabu? Nati, Ndidzakwera: ine ndikhala ngati iwe, anthu anga ngati anthu ako, akavalo anga ngati akavalo ako.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Nakatumiza mau kwa Yehosafati mfumu ya Yuda, ndi kuti, Mfumu ya Mowabu wapandukana ndi ine; kodi udzamuka nane kukathira nkhondo pa Mowabu? Nati, Ndidzakwera: ine ndikhala ngati iwe, anthu anga ngati anthu ako, akavalo anga ngati akavalo ako.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Kenaka Yoramuyo adatumiza mau kwa Yehosafati, mfumu ya ku Yuda, kuti, “Mfumu ya Amowabu yandigalukira ine. Kodi sungapite nane kunkhondo, kuti tikamenyane ndi Amowabu?” Tsono Yehosafatiyo adayankha kuti, “Ndidzapita. Ine ndi iwe ndife amodzi, anthu anga ndi ako omwe, akavalo anga ndi akonso.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”

Onani mutuwo Koperani




2 Mafumu 3:7
12 Mawu Ofanana  

Tsono anati kwa Yehosafati, Kodi udzapita nane kunkhondo ku Ramoti Giliyadi? Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israele, M'mene ukhalira iwe ndi momwe ndikhalira ndine; anthu anga monga anthu ako, akavalo anga monga akavalo ako.


Pamenepo Elisa anamwalira, ndipo anamuika. Ndipo magulu a Amowabu analowa m'dziko poyambira chaka.


Ndipo mfumu Yehoramu anatuluka mu Samariya nthawi yomweyo, namemeza Aisraele onse.


Ndipo anati, Tikwerere njira yiti? Nati iye, Njira ya ku chipululu cha Edomu.


Namuka mfumu ya Israele, ndi mfumu ya Yuda, ndi mfumu ya Edomu, nazungulira njira ya masiku asanu ndi awiri; ndipo panalibe madzi kuti ankhondo amwe, kapena nyama zakuwatsata.


Nati Ahabu mfumu ya Israele kwa Yehosafati mfumu ya Yuda, Mupita nane kodi ku Ramoti Giliyadi? Nayankha, nati, Monga inu momwemo ine; monga anthu anu momwemo anthu anga; tidzakhala nanu ku nkhondoyi.


Natuluka Yehu mwana wa Hanani mlauli kukomana naye, nati kwa mfumu Yehosafati, Muyenera kodi kuthandiza zoipa, ndi kukonda amene adana ndi Yehova? Chifukwa cha ichi ukugwerani mkwiyo wochokera kwa Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa