Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Mafumu 22:1 - Buku Lopatulika

1 Yosiya ndiye wa zaka zisanu ndi zitatu polowa ufumu wake, nakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu chimodzi mu Yerusalemu; ndi dzina la make ndi Yedida mwana wa Adaya wa ku Bozikati.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Yosiya ndiye wa zaka zisanu ndi zitatu polowa ufumu wake, nakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu chimodzi m'Yerusalemu; ndi dzina la make ndi Yedida mwana wa Adaya wa ku Bozikati.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Yosiya anali wa zaka zisanu ndi zitatu pamene adadaloŵa ufumu, ndipo adalamulira zaka 31 ku Yerusalemu. Mai wake anali Yedida mwana wa Adaya wa ku Bozikati.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.

Onani mutuwo Koperani




2 Mafumu 22:1
14 Mawu Ofanana  

Ndipo iye anafuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe, nati, Guwa la nsembe, guwa la nsembe, atero Yehova, Taona mwana adzabadwa m'nyumba ya Davide, dzina lake ndi Yosiya, adzaphera pa iwe ngati nsembe anthu ansembe a misanje, amene alikufukiza zonunkhira pa iwe, nadzatentha pa iwe mafupa a anthu.


Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri polowa iye ufumu.


Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri polowa iye ufumu wake, nakhala mfumu zaka makumi asanu ndi zisanu mu Yerusalemu; ndi dzina la make ndiye Hepeziba.


Koma anthu a m'dzikomo anapha onse akumchitira chiwembu mfumu Amoni; ndipo anthu a m'dzikomo anamlonga ufumu Yosiya mwana wake m'malo mwake.


Naikidwa iye m'manda mwake m'munda wa Uza; nakhala mfumu m'malo mwake Yosiya mwana wake.


M'kamwa mwa makanda ndi oyamwa munakhazikitsa mphamvu, chifukwa cha otsutsana ndi Inu, kuti muwaletse mdani ndi wobwezera chilango.


Tsoka kwa dzikowe, pamene mfumu yako ndiye mwana, ndipo akalonga ako adyera mamawa!


Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akulu ao, mwachibwana adzawalamulira.


amene anamdzera mau a Yehova masiku a Yosiya mwana wake wa Amoni, mfumu ya Ayuda chaka chakhumi ndi chitatu cha ufumu wake.


Taona tsono, yemweyo akabala mwana uyu, naona zochimwa zonse adazichita atate wake, naopa wosachita zoterezo,


Mau a Yehova amene anadza kwa Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya, masiku a Yosiya, mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.


ndi Hezekiya anabala Manase; ndi Manase anabala Amoni; ndi Amoni anabala Yosiya;


Lakisi ndi Bozikati ndi Egiloni;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa