Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Mafumu 18:3 - Buku Lopatulika

3 Nachita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adazichita Davide kholo lake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Nachita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adazichita Davide kholo lake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Hezekiya adachita zolungama pamaso pa Chauta, monga momwe ankachitira Davide kholo lake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.

Onani mutuwo Koperani




2 Mafumu 18:3
19 Mawu Ofanana  

Ndipo kudzakhala kuti ukadzamvera iwe zonse ndikulamulirazo, nukadzayenda m'njira zanga ndi kuchita chilungamo pamaso panga, kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga anatero Davide mtumiki wanga pamenepo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndidzakumangira ndi kukukhazikitsira nyumba, monga ndinammangira Davide, ndipo ndidzakupatsa iwe Israele.


Ndipo kunali, atakalamba Solomoni, akazi ake anapambutsa mtima wake atsate milungu ina; ndipo mtima wake sunakhale wangwiro ndi Yehova Mulungu wake monga mtima wa Davide atate wake.


Ndipo Asa anachita zabwino pamaso pa Yehova monga Davide kholo lake.


chifukwa kuti Davide adachita cholungama pamaso pa Yehova, osapatuka masiku ake onse pa zinthu zonse adamlamulira Iye, koma chokhacho chija cha Uriya Muhiti.


Ndipo ukadzayenda m'njira zanga kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga atate wako Davide anayendamo, Ine ndidzachulukitsa masiku ako.


Koma misanje sanaichotse; anthu anapherabe nsembe, nafukiza kumisanje.


Ndipo anachita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosanga Davide kholo lake; nachita monga mwa zonse anazichita Yowasi atate wake.


Mukumbukire Yehova kuti ndinayendabe pamaso panu m'choonadi, ndi mtima wangwiro, ndi kuchita zokoma m'kuona kwanu. Nalira Hezekiya kulira kwakukulu.


Nachita iye zoongoka pamaso pa Yehova, nayenda m'njira yonse ya Davide kholo lake, osapatukira ku dzanja lamanja kapena kulamanzere.


Nachita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga umo monse adachitira Davide kholo lake.


Apenyerera anthu, ndi kuti, ndinachimwa, ndaipsa choongokacho, ndipo sindinapindule nako.


Chifukwa chake ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse; koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.


ndipo anati, Ngati udzamveratu mau a Yehova, Mulungu wako, ndi kuchita zoona pamaso pake, ndi kutchera khutu pa malamulo ake, ndi kusunga malemba ake onse, za nthenda zonse ndinaziika pa Aejipito sindidzaziika pa iwe nnena imodzi; pakuti Ine Yehova ndine wakuchiritsa iwe.


Kumbukiranitu tsopano, Yehova, kuti ndayenda pamaso panu m'zoonadi ndi mtima wangwiro, ndipo ndachita zabwino pamaso panu. Ndipo Hezekiya analira kolimba.


Chotero chilamulo chili choyera, ndi chilangizo chake nchoyera, ndi cholungama, ndi chabwino.


Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ichi nchabwino.


Ndipo tsopano, Israele, Yehova Mulungu wanu afunanji nanu, koma kuti muziopa Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zake zonse, ndi kukonda, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,


Ndipo muzichita zolunjika ndi zokoma pamaso pa Yehova; kuti chikukomereni, ndi kuti mulowe kukalandira dziko lokomali Yehova analumbirira makolo anu,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa