Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Mafumu 17:34 - Buku Lopatulika

34 Mpaka lero lino achita monga mwa miyambo yoyambayi; saopa Yehova, sachita monga mwa malemba ao, kapena maweruzo ao, kapena chilamulo, kapena choikika adachilamulira Yehova ana a Yakobo, amene anamutcha Israele,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

34 Mpaka lero lino achita monga mwa miyambo yoyambayi; saopa Yehova, sachita monga mwa malemba ao, kapena maweruzo ao, kapena chilamulo, kapena choikika adachilamulira Yehova ana a Yakobo, amene anamutcha Israele,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

34 Akuchitabe zimene ankachita kale mpaka lero lino. Iwowo salemekeza Chauta kwenikweni ndipo satsata zogamula kapena zolengeza, ngakhale malangizo kapena malamulo amene Chauta adalamula zidzukulu za Yakobe, amene adamtchula kuti Israele.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

34 Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.

Onani mutuwo Koperani




2 Mafumu 17:34
14 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Dzina lako silidzatchedwanso Yakobo, koma Israele, chifukwa unayesana naye Mulungu ndithu, ndipo unapambana.


Yakobo ndipo anafunsa iye, nati, Undiuze ine dzina lako. Ndipo iye anati, Undifunsa dzina chifukwa ninji? Ndipo anamdalitsa iye pamenepo.


Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, natcha pamenepo El-Elohe-Israele.


Ndipo Mulungu anati kwa iye, Dzina lako ndi Yakobo; dzina lako silidzatchedwanso Yakobo, koma dzina lako lidzakhala Israele: ndipo anamutcha dzina lake Israele.


Nati kwa Yerobowamu, Takwaya magawo khumi; popeza atero Yehova Mulungu wa Israele, Taona ndidzaung'amba ufumu m'dzanja la Solomoni ndi kukupatsa iwe mafuko khumi.


Ndipo tsopano mukuti, Kauze mbuye wako kuti Eliya wabwera.


Ndipo Eliya anatenga miyala khumi ndi iwiri, monga mwa ziwerengo cha mafuko ana a Yakobo, amene mau a Yehova adamfikira, kuti, Dzina lako ndi Israele.


Ndipo kunali, poyamba iwo kukhala komweko, sanaope Yehova; ndipo Yehova anawatumizira mikango, niwapha ena a iwowa.


Amaopa Yehova, namatumikiranso milungu yao, monga mwa miyambo ya amitundu anawachotsako.


Koma sanamvere, nachita monga mwa mwambo wao woyamba.


Anatulutsa manja ake awagwire iwo akuyanjana naye, anaipsa pangano lake.


Woyenda moongoka mtima aopa Yehova; koma wokhota m'njira yake amnyoza.


Imvani inu ichi, banja la Yakobo, amene mutchedwa ndi dzina la Israele, amene munatuluka m'madzi a Yuda amene mulumbira dzina la Yehova ndi kutchula dzina la Mulungu wa Israele, koma si m'zoona, pena m'chilungamo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa