Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Timoteyo 2:10 - Buku Lopatulika

10 komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Kwenikweni adzikongoletse ndi ntchito zabwino, monga ayenera kuchitira akazi amene amati ndi opembedza Mulungu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.

Onani mutuwo Koperani




1 Timoteyo 2:10
15 Mawu Ofanana  

Avala mphamvu ndi ulemu; nangoseka nthawi ya m'tsogolo.


Mumpatse zipatso za manja ake; ndi ntchito zake zimtame kubwalo.


Koma mu Yopa munali wophunzira dzina lake Tabita, ndilo kunena Dorika; mkazi ameneyo anadzala ndi ntchito zabwino ndi zachifundo zimene anazichita.


Ndipo Petro ananyamuka, napita nao. M'mene anafikako, anapita naye kuchipinda chapamwamba; ndipo amasiye onse anaimirirapo pali iye, nalira, namuonetsa malaya ndi zovala zimene Dorika adasoka, pamene anali nao pamodzi.


Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.


Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse.


Momwemonso, akazi adziveke okha ndi chovala choyenera, ndi manyazi, ndi chidziletso; osati ndi tsitsi lake loluka, ndi golide kapena ngale, kapena malaya a mtengo wake wapatali;


amene anadzipereka yekha m'malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.


Okhulupirika mauwa, ndipo za izi ndifuna kuti ulimbitse mau, kuti iwo akukhulupirira Mulungu asamalire akhalebe atsogoleri a ntchito zabwino. Izi nzokoma ndi zopindulitsa anthu;


ndipo mayendedwe anu mwa amitundu akhale okoma, kuti, m'mene akamba za inu ngati ochita zoipa, akalemekeze Mulungu pakuona ntchito zanu zabwino, m'tsiku la kuyang'anira.


Popeza izi zonse zidzakanganuka kotero, muyenera inu kukhala anthu otani nanga, m'mayendedwe opatulika ndi m'chipembedzo,


Ndidziwa ntchito zako, ndi chikondi, ndi chikhulupiriro, ndi utumiki, ndi chipiriro chako, ndi kuti ntchito zako zotsiriza zichuluka koposa zoyambazo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa