Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Samueli 25:38 - Buku Lopatulika

38 Ndipo kunali, atapita masiku khumi, Yehova anamkantha Nabala, nafa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

38 Ndipo kunali, atapita masiku khumi, Yehova anamkantha Nabala, nafa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

38 Patapita masiku khumi, Chauta adakantha Nabala naafa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

38 Patapita masiku khumi, Yehova anakantha Nabala ndipo anafa.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 25:38
13 Mawu Ofanana  

Pomwepo mkwiyo wa Yehova udayaka pa Uza, ndipo Mulungu anamkantha pomwepo, chifukwa cha kusalingiriraku; nafa iye pomwepo pa likasa la Mulungu.


Ndipo Yehova anadwaza mfumu, nakhala iye wakhate mpaka tsiku la imfa yake, nakhala m'nyumba ya padera. Ndipo Yotamu mwana wa mfumu anayang'anira banja la mfumu, naweruza anthu a m'dziko.


Ndipo kunali, usiku womwewo mthenga wa Yehova anatuluka, nakantha m'misasa ya Aasiriya zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu, ndipo pouka anthu mamawa, taonani, onsewo ndi mitembo.


Momwemo mfumu siinamvere anthuwo; pakuti kusinthaku kudafuma kwa Mulungu, kuti Yehova akhazikitse mau ake, amene ananenetsa Ahiya wa ku Silo kwa Yerobowamu mwana wa Nebati.


Ndi Yerobowamu sanaonenso mphamvu m'masiku a Abiya, namkantha Yehova, nafa iye.


Mukabisa nkhope yanu, ziopsedwa; mukalanda mpweya wao, zikufa, ndipo zibwerera kufumbi kwao.


Ha? M'kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zoopsa.


Ndipo panakhala pakati pa usiku, Yehova anakantha ana oyamba onse a m'dziko la Ejipito, kuyambira mwana woyamba wa Farao wakukhala pa mpando wachifumu wake kufikira mwana woyamba wa wam'nsinga ali m'kaidi; ndi ana oyamba onse a zoweta.


Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, chifukwa sanampatse Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.


ndipo, kudalitsike kuchenjera kwako, nudalitsike iwe, pakuti unandiletsa kusakhetsa mwazi, ndi kusabwezera chilango ndi dzanja la ine ndekha.


Tsono m'mawa vinyo atamchokera Nabala, mkazi wake anamuuza zimenezi; ndipo mtima wake unamyuka m'kati mwake, iye nasanduka ngati mwala.


Nati Davide, Pali Yehova, Yehova adzamkantha iye; kapena tsiku la imfa yake lidzafika; kapena adzatsikira kunkhondo, nadzafako.


Ndipo muyang'anire, ngati likwera panjira ya malire akeake ku Betesemesi, Iye anatichitira choipa ichi chachikulu; koma likapanda kutero, tidzadziwapo kuti dzanja limene linatikantha, silili lake; langotigwera tsokali.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa