1 Samueli 25:28 - Buku Lopatulika28 Mukhululukire kulakwa kwa mdzakazi wanu; pakuti Yehova adzapatsadi mbuye wanga banja lokhazikika, pakuti mbuyanga amaponya nkhondo za Yehova; ndipo mwa inu simudzapezeka choipa masiku anu onse. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201428 Mukhululukire kulakwa kwa mdzakazi wanu; pakuti Yehova adzapatsadi mbuye wanga banja lokhazikika, pakuti mbuyanga amaponya nkhondo za Yehova; ndipo mwa inu simudzapezeka choipa masiku anu onse. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa28 Chonde, mukhululukire cholakwa cha ine mdzakazi wanu. Zoonadi, Chauta adzakhazikitsa banja lanu mu ufumu, poti mukummenyera nkhondo. Motero choipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero28 Chonde khululukani zolakwa za ine mdzakazi wanu. Ndithu Yehova adzakhazikitsa banja la mbuye wanga mu ufumu, popeza mukumenya nkhondo ya Yehova. Choncho choyipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu. Onani mutuwo |