Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Samueli 25:25 - Buku Lopatulika

25 Mbuye wanga, musasamalire munthu uyu woipa, ndiye Nabala; chifukwa monga dzina lake momwemo iye; dzina lake ndiye Nabala, ndipo ali nako kupusa; koma ine mdzakazi wanu sindinaone anyamata a mbuye wanga, amene munawatumiza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

25 Mbuye wanga, musasamalire munthu uyu woipa, ndiye Nabala; chifukwa monga dzina lake momwemo iye; dzina lake ndiye Nabala, ndipo ali nako kupusa; koma ine mdzakazi wanu sindinaona anyamata a mbuye wanga, amene munawatumiza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

25 Mbuyanga asasamale za amuna anga, munthu wa mkhalidwe wovuta uja. Monga momwe dzina lake liliri, iyenso ali choncho. Monga dzina lake limatanthauzira kuti chitsiru, zake zonse nzauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindidaŵaone anyamata anu amene mudaaŵatumawo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

25 Mbuye wanga musasamale za mwamuna wanga Nabala, munthu wa khalidwe loyipa. Iyeyu ali monga dzina lake liliri. Monga dzina lake litanthauza kuti chitsiru, ndiye kuti zake zonse ndi zauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindinawaone anthu amene mbuye wanga munawatuma.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 25:25
9 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake tsono mfumu mbuye wanga asasauke mtima ndi chinthuchi, ndi kuganiza kuti ana aamuna onse a mfumu afa; pakuti Aminoni yekha wafa.


Wolungama asamalira mlandu wa osauka; koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.


Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.


Chifukwa chake anatsanulira pa iye mkwiyo wake waukali, ndi mphamvu za nkhondo; ndipo unamyatsira moto kuzungulira kwake, koma iye sanadziwe; ndipo unamtentha, koma iye sanachisunge m'mtima.


Mukapanda kumvera, mukapanda kuliika mumtima mwanu, kupatsa dzina langa ulemerero, ati Yehova wa makamu, ndidzakutumizirani temberero, ndi kutemberera madalitso anu; inde, ndawatemberera kale chifukwa simuliika mumtima.


Chifukwa chake tsono mudziwe ndi kulingalira chimene mudzachita; popeza anatsimikiza mtima kuchitira choipa mbuye wathu, ndi nyumba yake yonse; popeza iye ali woipa, ndipo munthu sakhoza kulankhula naye.


Ndipo atagwadira pa mapazi ake anati, Pa ine, mbuye wanga, pa ine pakhale uchimowo; ndipo mulole mdzakazi wanu alankhule m'makutu anu, nimumvere mau a mdzakazi wanu.


Chifukwa chake tsono, mbuye wanga, pali Yehova, ndipo pali moyo wanu, popeza Yehova anakuletsani kuti mungakhetse mwazi, ndi kudzibwezera chilango ndi dzanja la inu nokha, chifukwa chake adani anu, ndi iwo akufuna kuchitira mbuye wanga choipa, akhale ngati Nabala.


Tsono dzina la munthuyo ndiye Nabala, ndi dzina la mkazi wake ndiye Abigaile; ndiye mkazi wa nzeru yabwino, ndi wa nkhope yokongola; koma mwamunayo anali waphunzo ndi woipa machitidwe ake; ndipo iye anali wa banja la Kalebe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa