Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Samueli 14:33 - Buku Lopatulika

33 Pamenepo anauza Saulo, kuti, Onani anthu alikuchimwira Yehova, umo akudya zamwazi. Ndipo iye anati, Munachita konyenga; kunkhunizani mwala waukulu kwa ine lero.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

33 Pamenepo anauza Saulo, kuti, Onani anthu alikuchimwira Yehova, umo akudya zamwazi. Ndipo iye anati, Munachita konyenga; kunkhunizani mwala waukulu kwa ine lero.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

33 Koma ena adauza Saulo kuti, “Onani, anthu akuchimwira Chauta podyera kumodzi ndi magazi.” Saulo adati, “Mwaukira Chauta lero! Pezani mwala waukulu muukunkhunizire kuno.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

33 Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 14:33
12 Mawu Ofanana  

Koma nyama, m'mene muli moyo wake, ndiwo mwazi wake, musadye.


Ndipo munthu aliyense wa mbumba ya Israele, kapena mlendo wogonera pakati panu, wakudya mwazi uliwonse; nkhope yanga idzatsutsana naye munthu wakudya mwaziyo, ndi kumsadza kumchotsa kwa anthu a mtundu wake.


Musamadya kanthu ndi mwazi wake; musamachita nyanga, kapena kuombeza ula.


Ndipo musamadya mwazi uliwonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse.


Aliyense akadya mwazi uliwonse, munthuyo achotsedwe kwa anthu a mtundu wake.


Wonyenga iwe! Tayamba kuchotsa m'diso lako mtandawo, ndipo pomwepo udzapenyetsa kuchotsa kachitsotso m'diso la mbale wako.


koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.


Chifukwa chake uli wopanda mau owiringula, munthu iwe, amene uli yense wakuweruza; pakuti m'mene uweruza wina, momwemo udzitsutsa iwe wekha, pakuti iwe wakuweruza, umachita zomwezo.


Mwazi wao wokha musamadya; muziuthira panthaka ngati madzi.


Koma mulimbikepo ndi kusadya mwaziwo; popeza mwazi ndiwo moyo, nimusamadya moyo pamodzi ndi nyama yake.


Mwazi wake wokha musamadya; muuthire pansi ngati madzi.


Ndipo Saulo anati, Balalikani pakati pa anthu, nimuwauze kuti abwere kwa ine kuno munthu yense ndi ng'ombe yake, ndi munthu yense ndi nkhosa yake, aziphe pano, ndi kuzidya, osachimwira Yehova ndi kudya zamwazi. Nabwera anthu onse, yense ndi ng'ombe yake, usiku uja naziphera pomwepo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa