Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Mbiri 4:41 - Buku Lopatulika

41 Iwo tsono olembedwa maina anadza masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda, nakantha mahema ao ndi zokhalamo zao, naziononga konse mpaka lero, nakhala m'malo mwao; popeza panali podyetsa zoweta zao pamenepo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

41 Iwo tsono olembedwa maina anadza masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda, nakantha mahema ao ndi zokhalamo zao, naziononga konse mpaka lero, nakhala m'malo mwao; popeza panali podyetsa zoweta zao pamenepo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

41 Anthu a fuko a Simeoniwo, ochita kulembedwa maina, adadza pa nthaŵi ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda, ndipo adaononga mahema a Ahamuwo ndi kupha Ameuni amene adaŵapeza kumeneko. Adaonongeratu anthu onsewo kotero kuti dzina lao silidamvekenso mpaka lero lino. Kenaka iwowo adakhala ku malo amenewo, popeza kuti kunali msipu womadyetsako ziweto zao.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

41 Anthu amene mayina awowa alembedwa, anabwera pa nthawi ya Hezekiya mfumu ya Yuda. Iwo anathira nkhondo fuko la Hamu mʼmalo awo amene amakhala komanso Ameuni amene anali kumeneko ndipo anawononga onsewo kotero kuti mbiri yawo simvekanso mpaka lero lino. Kotero iwo anakhala mʼmalo awo chifukwa kunali msipu wa ziweto zawo.

Onani mutuwo Koperani




1 Mbiri 4:41
13 Mawu Ofanana  

Ahazi mwana wake, Hezekiya mwana wake, Manase mwana wake,


ndi midzi yao yonse pozungulira pake pa mizinda yomweyi, mpaka Baala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.


Pakuti adagwa, nafa ambiri, popeza nkhondoyi nja Mulungu. Ndipo anakhala m'malo mwao mpaka anatengedwa ndende.


Anakanthanso a m'mahema a ng'ombe, nalanda nkhosa zochuluka, ndi ngamira; nabwerera kunka ku Yerusalemu.


Ndipo zitatha izi, kunachitika kuti ana a Mowabu, ndi ana a Amoni, ndi ena pamodzi ndi Aamoni, anadza kuyambana nkhondo ndi Yehosafati.


Ndipo Mulungu anamthandiza poyambana ndi Afilisti, ndi Aarabu okhala mu Guribaala, ndi Ameuni.


Chifukwa chake tamvani uphungu wa Yehova, umene waupangira pa Edomu; ndi zimene walingalirira okhala mu Temani, ndithu adzawakoka, ana aang'ono a zoweta; ndithu adzayesa busa lao bwinja pamodzi nao.


ndipo ndi mmodzi analenga mitundu yonse ya anthu, kuti akhale ponse pa nkhope ya dziko lapansi, atapangiratu nyengo zao, ndi malekezero a pokhala pao;


Asidoni omwe, ndi Aamaleke, ndi Amaoni anakupsinjani. Pamenepo munafuula kwa Ine, ndipo ndinakupulumutsani m'dzanja lao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa