Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Mbiri 20:7 - Buku Lopatulika

7 Ndipo potonza Israele iyeyu Yonatani mwana wa Simea mbale wake wa Davide anamkantha.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Ndipo potonza Israele iyeyu Yonatani mwana wa Simea mbale wake wa Davide anamkantha.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Tsiku lina pamene adanyoza Aisraele, Yonatani, mwana wa Simea, mbale wake wa Davide, adamupha.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.

Onani mutuwo Koperani




1 Mbiri 20:7
9 Mawu Ofanana  

ndi Yese anabala mwana wake wamwamuna woyamba Eliyabu, ndi Abinadabu wachiwiri, ndi Simea wachitatu,


Ndipo panalinso nkhondo ku Gati; kumeneko kunali munthu wa msinkhu waukulu, amene zala zake za kumanja ndi kumapazi ndizo makumi awiri mphambu zinai; zisanu ndi chimodzi ku dzanja lililonse, ndi zisanu ndi chimodzi ku phazi lililonse; nayenso anabadwa mwa chimphonacho.


Awa anabadwa mwa chimphonacho ku Gati, koma anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ake.


Ndipo Yonatani atate wake wina wa Davide anali phungu, munthu wanzeru ndi mlembi; ndi Yehiyele mwana wa Hakimoni anakhala ndi ana a mfumu;


Ndani amene, iwe wamtonza ndi kumlalatira? Ndani amene iwe wakwezera mau ako ndi kutukulira maso ako kumwamba? Ndiye Woyera wa Israele.


Pamenepo Yese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankhe.


Nati Mfilistiyo, Ine ndinyoza makamu a nkhondo a Israele lero; mundipatse munthu, kuti tilimbane ife awiri.


Ndipo Davide analankhula ndi anthu akuima pafupi ndi iye, nati, Adzamchitira chiyani munthu wakupha Mfilisti uyu, ndi kuchotsa tonzo lake pakati pa Israele? Pakuti Mfilisti uyu wosadulidwa ndiye yani, kuti azinyoza makamu a Mulungu wamoyo?


Ine kapolo wanu ndinapha mkango ndi chimbalangondo zonse ziwiri; ndipo Mfilisti uyu wosadulidwa adzakhala ngati mmodzi wa izo, popeza wanyoza makamu a Mulungu wamoyo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa