Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Mafumu 7:2 - Buku Lopatulika

2 Anamanganso nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni, m'litali mwake munali mikono zana limodzi, kupingasa kwake mikono makumi asanu, ndi msinkhu wake mikono makumi atatu; naisanja pa mizere inai ya mapanda amkungudza, ndi mitanda yamkungudza, ndi mitanda yamkungudza yotanthalika mapandawo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Anamanganso nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni, m'litali mwake munali mikono zana limodzi, kupingasa kwake mikono makumi asanu, ndi msinkhu wake mikono makumi atatu; naisanja pa mizere inai ya mapanda amkungudza, ndi mitanda yamkungudza, ndi mitanda yamkungudza yotanthalika mapandawo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Nyumbayo inali ndi chigawo china chachikulu chotchedwa Nyumba ya Nkhalango ya ku Lebanoni. M'litali mwake inali mamita 44, m'mimba mwake inali mamita 22, msinkhu wake unali mamita 13 ndi theka. Adaimanga pamwamba pa mizere inai ya nsanamira zamkungudza, ndipo panali mitanda yamkungudza pamwamba pa nsanamirazo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Iye anamanga nyumba yaufumu yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni yomwe mulitali mwake inali mamita 44, mulifupi mwake mamita 22, msinkhu wake mamita 13 ndi theka; ndipo inakhazikika pa mizere inayi ya mapanda a mkungudza yokhala ndi mitanda ya mkungudza yotanthalika pa mapandawo.

Onani mutuwo Koperani




1 Mafumu 7:2
8 Mawu Ofanana  

Ndi malihawo mazana atatu a golide wonsansantha, lihawo limodzi linapangidwa ndi miyeso ya mina itatu ya golide; ndipo mfumu inazisungira zonse m'nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni.


Ndipo zikho zomwera zonse za mfumu Solomoni zinali zagolide, ndi zotengera zonse za nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni zinali zagolide yekhayekha, panalibe zasiliva, pakuti siliva anangoyesedwa opanda pake masiku onse a Solomoni.


Ndipo inayalidwa ndi mkungudza pamwamba pa zipinda makumi anai mphambu zisanu zolongosoledwa pa mapanda, mzere umodzi zipinda khumi mphambu asanu.


Ndipo kunali, atatsiriza Solomoni kumanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi chifuniro chonse cha Solomoni anachikhumbacho,


ndi mizinda yonse yosungamo zinthu zake za Solomoni, ndi mizinda yosungamo magaleta ake, ndi mizinda yokhalamo apakavalo ake, ndi zina zilizonse zidakomera Solomoni kuzimanga mu Yerusalemu, ndi ku Lebanoni, ndi m'dziko lonse la ufumu wake.


Napanganso malihawo mazana atatu a golide wonsansantha, chikopa chimodzi chinathera masekeli mazana atatu a golide; ndipo mfumu inazilonga m'nyumba yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni.


Khosi lako likunga nsanja yaminyanga; maso ako akunga matawale a ku Hesiboni, a pa chipata cha Batirabimu; mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebanoni imene iloza ku Damasiko.


Ndipo Iye anachotsa chophimba cha Yuda; ndipo iwe unayang'ana tsiku limenelo pa zida za m'nyumba ya nkhalango.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa