1 Mafumu 3:3 - Buku Lopatulika3 Ndipo Solomoni anakondana ndi Yehova, nayenda m'malemba a Davide atate wake; koma anaphera nsembe nafukiza zonunkhira pamisanje. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20143 Ndipo Solomoni anakondana ndi Yehova, nayenda m'malemba a Davide atate wake; koma anaphera nsembe nafukiza zonunkhira pamisanje. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa3 Solomoni ankakonda Chauta, namasunga malamulo a Davide bambo wake. Komabe ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku akachisi aja. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero3 Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo. Onani mutuwo |
Ndipo kudzakhala kuti ukadzamvera iwe zonse ndikulamulirazo, nukadzayenda m'njira zanga ndi kuchita chilungamo pamaso panga, kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga anatero Davide mtumiki wanga pamenepo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndidzakumangira ndi kukukhazikitsira nyumba, monga ndinammangira Davide, ndipo ndidzakupatsa iwe Israele.