Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Mafumu 16:2 - Buku Lopatulika

2 Popeza ndinakukuza iwe kuchokera kufumbi, ndi kukuika iwe mfumu ya anthu anga Israele, koma iwe unayenda m'njira ya Yerobowamu, ndi kuchimwitsa anthu anga Israele, kuputa mkwiyo wanga ndi machimo ao;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Popeza ndinakukuza iwe kuchokera kufumbi, ndi kukuika iwe mfumu ya anthu anga Israele, koma iwe unayenda m'njira ya Yerobowamu, ndi kuchimwitsa anthu anga Israele, kuputa mkwiyo wanga ndi machimo ao;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 “Iwe sudaali kanthu konse, ndidachita kukukweza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga a ku Israele. Komabe tsopano wachimwa ngati Yerobowamu, ndipo waŵachimwitsa anthu a ku Israelewo, mwakuti iwo aputa mkwiyo wanga chifukwa cha kuchimwa kwaoko.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.

Onani mutuwo Koperani




1 Mafumu 16:2
16 Mawu Ofanana  

Ndipo adzapereka Aisraele chifukwa cha machimo a Yerobowamu anachimwawo, nachimwitsa nao Aisraele.


Kauze Yerobowamu, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Ndingakhale ndinakukulitsa pakati pa anthu, ndi kukukhalitsa pakati pa anthu ndi kukukhalitsa mfumu ya anthu anga Aisraele,


Nachita zoipa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya atate wake, ndi m'tchimo lomwelo iye akachimwitsa nalo Aisraele.


Ndipo anachimwa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya Yerobowamu, ndi m'tchimo lake iye anachimwitsa nalo Israele.


Ndipo Mose anati kwa Aroni, Anthu awa anakuchitiranji, kuti iwe watengera iwo kulakwa kwakukulu kotere?


Ana atola nkhuni, atate akoleza moto, akazi akanyanga ufa, kuti aumbe mikate ya mfumu yaikazi ya kumwamba, athirire milungu ina nsembe yothira, kuti autse mkwiyo wanga.


Chifukwa chake yense wakumasula limodzi la malamulo amenewa ang'onong'ono, nadzaphunzitsa anthu chomwecho, adzatchulidwa wamng'onong'ono mu Ufumu wa Kumwamba; koma yense wakuchita ndi kuphunzitsa awa, iyeyu adzatchulidwa wamkulu mu Ufumu wa Kumwamba.


Iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yachifumu, ndipo anakweza aumphawi.


Iai, ana anga, popeza mbiri imene ndilikuimva sili yabwino iai; mulikulakwitsa anthu a Yehova.


Amuutsa waumphawi m'fumbi, nanyamula wosowa padzala, kukamkhalitsa kwa akalonga; ndi kuti akhale nacho cholowa cha chimpando cha ulemerero. Chifukwa nsanamira za dziko lapansi nza Yehova, ndipo Iye anakhazika dziko pa izo.


Chifukwa chake mbuye wanga mfumu amvere mau a kapolo wake. Ngati ndi Yehova anakuutsirani inu kutsutsana ndi ine, alandire chopereka; koma ngati ndi ana a anthu, atembereredwe pamaso pa Yehova, pakuti anandipirikitsa lero kuti ndisalandireko cholowa cha Yehova, ndi kuti, Muka, utumikire milungu ina.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa