1 Mafumu 13:2 - Buku Lopatulika2 Ndipo iye anafuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe, nati, Guwa la nsembe, guwa la nsembe, atero Yehova, Taona mwana adzabadwa m'nyumba ya Davide, dzina lake ndi Yosiya, adzaphera pa iwe ngati nsembe anthu ansembe a misanje, amene alikufukiza zonunkhira pa iwe, nadzatentha pa iwe mafupa a anthu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20142 Ndipo iye anafuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe, nati, Guwa la nsembe, guwa la nsembe, atero Yehova, Taona mwana adzabadwa m'nyumba ya Davide, dzina lake ndi Yosiya, adzaphera pa iwe ngati nsembe anthu ansembe a misanje, amene alikufukiza zonunkhira pa iwe, nadzatentha pa iwe mafupa a anthu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa2 Ndipo mneneriyo adatemberera guwalo potsata mau a Chauta nati, “Guwa iwe, guwa iwe, imva mau a Chauta, akunena kuti, ‘Mwana wamwamuna adzabadwa pa banja la Davide, dzina lake Yosiya. Pa iwe iyeyo adzaperekapo ngati nsembe ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene amafukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’ ” Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero2 Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’ ” Onani mutuwo |