Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Mafumu 1:3 - Buku Lopatulika

3 Tsono anafunafuna m'malire monse a Israele namwali wokongola, napeza Abisagi wa ku Sunamu, nabwera naye kwa mfumu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Tsono anafunafuna m'malire monse a Israele namwali wokongola, napeza Abisagi wa ku Sunamu, nabwera naye kwa mfumu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Choncho adafunafuna namwali wokongola m'dziko lonse la Israele, ndipo adapeza Abisagi wa ku Sunamu, nabwera naye kwa mfumu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.

Onani mutuwo Koperani




1 Mafumu 1:3
9 Mawu Ofanana  

Pamenepo anyamata ake ananena naye, Amfunire mbuye wanga mfumu namwali, aimirire pamaso pa mfumu namsunge; nagone m'mfukato mwanu, kuti mbuye mfumu yanga afundidwe.


Ndipo namwaliyo anali wokongola ndithu, namasunga mfumu namtumikira; koma mfumu sinamdziwe.


Potero anamuka, nafika kwa munthu wa Mulungu kuphiri la Karimele. Ndipo kunali, pakumuona munthu wa Mulungu alinkudza kutali, anati kwa Gehazi mnyamata wake, Tapenya, suyo Msunamu uja;


Ndipo linafika tsiku lakuti Elisa anapitirira kunka ku Sunemu, kumeneko kunali mkazi womveka; ameneyo anamuumiriza adye mkate. Potero pomapitirako iyeyo, ankawapatukirako kukadya mkate.


Pamenepo anyamata a mfumu omtumikira anati, Amfunire mfumu anamwali okongola;


ndi namwali womkonda mfumu akhale mkazi wamkulu m'malo mwa Vasiti. Ndipo chinthuchi chinamkonda mfumu, nachita chomwecho.


Ndi malire ao anali ku Yezireele, ndi Kesuloti, ndi Sunemu;


Ndipo Afilisti anasonkhana, nadza namanga misasa ku Sunemu; ndipo Saulo anasonkhanitsa Aisraele onse, namanga iwo ku Gilibowa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa