Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Akorinto 16:22 - Buku Lopatulika

22 Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

22 Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

22 Ngati munthu sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Maranatha! Ambuye athu, bwerani!

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

22 Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 16:22
32 Mawu Ofanana  

Ndiuze, iwe amene moyo wanga ukukonda, umaweta kuti gulu lako? Umaligonetsa kuti pakati pa usana? Pakuti ndikhalirenji ngati wosochera pambali pa magulu a anzako?


M'kamwa mwake muli mokoma; inde, ndiye wokondweretsa ndithu. Ameneyu ndi wokondedwa wanga, ameneyu ndi bwenzi langa, ana aakazi inu a ku Yerusalemu.


Ndiimbire wokondedwa wanga nyimbo ya wokondedwa wanga ya munda wake wampesa. Wokondedwa wanga anali ndi munda wampesa m'chitunda cha zipatso zambiri;


Iye wakukonda atate wake, kapena amake koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wake wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.


Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.


Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo Ine ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsa ndekha kwa iye.


Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.


Sindikadachita mwa iwo ntchito zosachita wina, sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano anaona, nada Ine ndi Atate wanganso.


Iyeyo adzalemekeza Ine; chifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.


Yesu anati kwa iwo, Mulungu akadakhala Atate wanu, mukadakonda Ine; pakuti Ine ndinatuluka, ndi kuchokera kwa Mulungu; pakuti sindinadze kwa Ine ndekha, koma Iyeyu anandituma Ine.


Amenewo anadza kwa ansembe aakulu ndi akulu, nati, Tadzitemberera nalo temberero kuti sitidzalawa kanthu kufikira titamupha Paulo.


Pakuti ndikadafuna kuti ine ndekha nditembereredwe kundichotsa kwa Khristu chifukwa cha abale anga, ndiwo a mtundu wanga monga mwa thupi;


Chifukwa chake ndikuuzani inu, kuti palibe munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; ndipo palibe wina akhoza kunena, Yesu ali Ambuye, koma mwa Mzimu Woyera.


Pakuti mwa Khristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.


Akhale nacho chisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Khristu m'chosaonongeka.


Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.


pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.


amene mungakhale simunamuone mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero:


Kwa inu tsono akukhulupirira, ali wa mtengo wake; koma kwa iwo osakhulupirira, Mwala umene omangawo anaukana, womwewo unayesedwa mutu wa pangodya.


Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.


Yense wokhulupirira kuti Yesu ndiye Khristu wabadwa kuchokera kwa Mulungu; ndipo yense wakukonda Iye amene anabala akondanso iye amene anabadwa wochokera mwa Iye.


Iye wakuchitira umboni izi, anena, Indetu; ndidza msanga. Amen; idzani, Ambuye Yesu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa