Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Akorinto 16:14 - Buku Lopatulika

14 Zanu zonse zichitike m'chikondi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Zanu zonse zichitike m'chikondi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Zonse zimene muchita, muzichite mwachikondi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Chitani zonse mwachikondi.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 16:14
22 Mawu Ofanana  

Zinthu izi ndilamula inu, kuti mukondane wina ndi mnzake.


Koma ngati iwe wachititsa mbale wako chisoni ndi chakudya, pamenepo ulibe kuyendayendanso ndi chikondano. Usamuononga ndi chakudya chako, iye amene Khristu adamfera.


Koma funitsitsani mphatso zoposa. Ndipo ndikuonetsani njira yokoma yoposatu.


Tsatani chikondi; koma funitsitsani mphatso zauzimu, koma koposa kuti mukanenere.


Koma ndikupemphani inu, abale, (mudziwa banja la Stefanasi, kuti ali chipatso choyamba cha Akaya, ndi kuti anadziika okha kutumikira oyera mtima),


Koma za zoperekedwa nsembe kwa mafano: Tidziwa kuti tili nacho chidziwitso tonse. Chidziwitso chitukumula, koma chikondi chimangirira.


Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,


koma Ambuye akukulitseni inu, nakuchulukitseni m'chikondano wina kwa mnzake ndi kwa anthu onse, monganso ife titero kwa inu;


Koma tsopano pofika Timoteo kwathu kuchokera kwa inu, ndi kutifotokozera mbiri yokoma ya chikhulupiriro ndi chikondano chanu, ndi kuti mutikumbukira bwino masiku onse, pokhumba kutiona ife, monganso ife kukuonani inu;


Tiziyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu, abale, monga kuyenera; pakuti chikhulupiriro chanu chikula chikulire, ndipo chichulukira chikondano cha inu nonse, yense pa mnzake;


koma chitsirizo cha chilamuliro ndicho chikondi chochokera mu mtima woyera ndi m'chikumbu mtima chokoma ndi chikhulupiriro chosanyenga;


Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu.


koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;


ndi pachipembedzo chikondi cha pa abale; ndi pachikondi cha pa abale chikondi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa