Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Akorinto 14:13 - Buku Lopatulika

13 Chifukwa chake wolankhula lilime, apemphere kuti amasule.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Chifukwa chake wolankhula lilime, apemphere kuti amasule.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Nchifukwa chake munthu wolankhula chilankhulo chosadziŵika, apemphere kuti alandirenso mphatso ya kuchitanthauzira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 14:13
11 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake ndinena ndi inu, Zinthu zilizonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.


Iwo onse analikukangalika m'kupemphera, pamodzi ndi akazi, ndi Maria, amake wa Yesu, ndi abale ake omwe.


amenewo, m'mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:


ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.


Ali nazo mphatso za machiritso onse kodi? Kodi onse alankhula ndi malilime? Kodi onse amasulira mau?


Momwemo inunso, popeza muli ofunitsitsa mphatso za Mzimu, funani kuti mukachuluke kukumangirira kwa Mpingo.


Pakuti ngati ndipemphera m'lilime, mzimu wanga upemphera, koma chidziwitso changa chikhala chosabala kanthu.


Nanga chiyani tsono, abale? Pamene musonkhana, yense ali nalo salimo, ali nacho chiphunzitso, ali nalo vumbulutso, ali nalo lilime, ali nacho chimasuliro. Muchite zonse kukumangirira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa