Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


105 Mauthenga a Mulungu Ponena za Uchiuta wa Khristu

105 Mauthenga a Mulungu Ponena za Uchiuta wa Khristu

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, nthawi zambiri Yesu ankachita ndi kunena zinthu zomwe Mulungu yekha ndiye anali ndi ufulu wozichita ndi kuzinena. Mungaganizire zimenezo!

Ankanena zinthu zosonyeza kuti iye ndi Mulungu. Zimadabwitsa kwambiri!

Ndipo chofunika kwambiri, anapatsidwa ulamuliro, ulemerero, ndi ufumu kuti anthu onse, mitundu yonse, ndi a ziyankhulo zonse azimutumikira. Ulamuliro wake ndi wosatha, sudzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongedwa. Tangoganizirani ulamuliro wosatha!

Bukhu la Danieli 7:13-14 limati: “Ndinaona m’masomphenya anga ausiku, ndipo taonani, munthu wonga mwana wa munthu anabwera ndi mitambo ya kumwamba, ndipo anafika kwa Wakale Masiku, ndipo anam’bweretsa pamaso pake. Ndipo anapatsidwa ulamuliro, ulemerero, ndi ufumu, kuti anthu onse, mitundu yonse, ndi a ziyankhulo zonse azimutumikira. Ulamuliro wake ndiwo ulamuliro wosatha umene sudzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongedwa.” Apa, Yesu, monga Mwana wa Munthu, akuwonetsedwa kuti ndiye wolamulira wosatha.

Zimenezi zimandipatsa chiyembekezo chachikulu, ndipo ndikukhulupirira kuti zimakupatsaninso chiyembekezo!




Yohane 8:58

Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti Abrahamu asanabadwe, Ine ndilipo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 20:28

Tomasi adati, “Ambuye anga! Mulungu wanga!”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:9

Pakuti m'thupi la Khristu umulungu wonse umakhalamo wathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:33

Apo amene anali m'chombo aja adamgwadira Yesu nati, “Ndithudi, ndinu Mwana wa Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:1

Pachiyambi pa zonse Iye amene amatchedwa dzina loti Mau, anali alipo kale. Anali kwa Mulungu, ndipo anali Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:6

Koma pamene ankatuma Mwana wake wachisamba pansi pano, Mulungu adati, “Angelo onse a Mulungu azimpembedza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:14

Wotchedwa Mau uja adasanduka munthu, nadzakhala pakati pathu. Anali wokoma mtima ndi wokhulupirika kwabasi. Ndipotu tidaona ulemerero wake, ndiye kuti ulemerero womwe Iye amalandira kwa Atate pokhala Mwana wao mmodzi yekha uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:38

Koma ngati ndimazichitadi, khulupirirani ntchitozo, ngakhale simukhulupirira Ine. Apo mudzadziŵa mosapeneka konse kuti Atate amakhala mwa Ine, ndipo Ine ndimakhala mwa Atate.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:2

Iwowo ankafunsa kuti, “Ali kuti mwana amene adabadwa kuti adzakhale Mfumu ya Ayuda? Ife tidaona nyenyezi yake ikutuluka kuvumaku, motero tabwera kudzampembedza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:30

Ine ndi Atate ndife amodzi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:9

Mwadzidzidzi Yesu adakumana nawo nati, “Monitu azimai!” Iwo adadza pafupi, nkugwira mapazi ake, nampembedza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:9

Yesu adamuyankha kuti, “Iwe Filipo, ndakhala nanu nthaŵi yonseyi, ndipo sunandidziŵebe? Amene waona Ine, waonanso Atate. Nanga bwanji ukuti, ‘Tiwonetseni Atate?’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:18

Pamenepo ndiye Ayuda adankirankira kufuna kumupha. Ankati Yesu akuphwanya lamulo lokhudza Sabata, ndiponso ponena kuti Mulungu ndi Atate ake, ankadzilinganiza ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:8

Koma za Mwana wake adati, “Inu Mulungu, mpando wanu wachifumu udzakhala mpaka muyaya, chilungamo ndicho chili ngati ndodo yachifumu mu ulamuliro wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:23

“Namwali wina wosadziŵa mwamuna adzatenga pathupi nkubala mwana wamwamuna. Mwanayo adzatchedwa dzina loti Imanuele,” ndiye kuti “Mulungu ali nafe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:18

Yesu adadza pafupi naŵauza kuti, “Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:35

Mngeloyo adayankha kuti, “Mzimu Woyera adzakutsikirani, ndipo mphamvu za Mulungu Wopambanazonse zidzakuphimbani. Nchifukwa chake Mwana wodzabadwayo adzakhala Woyera, ndipo adzatchedwa Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:11

Usiku womwe uno m'mudzi wa Davide wakubadwirani Mpulumutsi, amene ndi Khristu Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:3-4

Umasimba za Mwana wake, Yesu Ambuye athu. Poyang'anira umunthu wake, kholo lake ndi Davide, amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao. Ndi opusa, osakhulupirika, okhakhala moyo, ndi opanda chifundo. Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita. koma poyang'anira kuyera kwake kwaumulungu, kuuka kwake kwa akufa kukutsimikiza kuti Yesuyo ndi Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 9:5

Iwoŵa ndi zidzukulu za makolo athu akale aja, ndipo Mpulumutsi wolonjezedwa uja ndi wa mtundu wao, kunena za umunthu wake. Mulungu amene amalamulira zonse, alemekezeke mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 4:4

Iwoŵa sakhulupirira, popeza kuti Satana, amene ali mulungu wa dziko lino lapansi, adachititsa khungu maganizo ao, kuwopa kuti angaone kuŵala kwa Uthenga Wabwino. Kuŵalako kumaonetsa ulemerero wa Khristu, ndipo mwa Iyeyu Mulungu mwini amaoneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 4:4

Koma nthaŵi itakwana, Mulungu adatuma Mwana wake. Mwanayo adabadwa mwa mkazi, adabadwa woyenera kumvera Malamulo a Mose.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:20-21

imene Mulungu adaigwiritsa ntchito pamene adaukitsa Khristu kwa akufa, namkhazika ku dzanja lake lamanja m'dziko la Kumwamba. Adamkhazika pamwamba pa mafumu onse, aulamuliro onse ndi akuluakulu onse a Kumwamba, ndiponso pamwamba pa maina ena onse amene anthu angaŵatchule nthaŵi ino kapenanso nthaŵi ilikudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:5-7

Motero nonse mukhale ndi mtima womwe uja umene adaali nawonso Khristu Yesu: Iyeyu anali ndi umulungu chikhalire, komabe sadayese kuti kulingana ndi Mulungu ndi chinthu choti achigwiritsitse. Koma adadzitsitsa kotheratu pakudzitengera umphaŵi wa kapolo, ndi kukhala munthu wonga anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15

Khristuyo ndiye chithunzi chenicheni cha Mulungu wosaoneka. Iye ndiye Mwana wake woyamba, wolamulira zolengedwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:19

Kudakomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 3:16

Ndithudi, chinsinsi cha chipembedzo chathu nchachikulu: “Iye uja adaonekera ali ndi thupi la munthu, Mzimu Woyera adamchitira umboni kuti ndi wolungama, angelo adamuwona, adalalikidwa pakati pa anthu a mitundu yonse, anthu a pa dziko lonse lapansi adamkhulupirira, Iyeyo adatengedwa kunka kumwamba mu ulemerero.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:1-3

Kale lija pa nthaŵi zosiyanasiyana, mwa njira zosiyanasiyana, Mulungu adaalankhula ndi makolo athu kudzera mwa aneneri. Adatinso, “Inu Ambuye, ndinu amene mudalenga dziko lapansi pachiyambi pomwe, zakumwambaku ndi ntchito ya manja anu. Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu achikhalire. Zonsezi zidzafwifwa ngati chovala. Mudzazipindapinda ngati mwinjiro, ndipo zidzasinthika ngati chovala, koma Inu ndinu osasinthika, zaka zanu sizidzatha konse.” Nkale lonse Mulungu sadauzepo mngelo aliyense kuti, “Khala ku dzanja langa lamanja mpaka ndisandutse adani ako kuti akhale ngati chopondapo mapazi ako.” Nanga angelo, kodi suja iwo ndi mizimu yotumikira chabe, imene Mulungu amaituma chifukwa cha anthu odzalandira chipulumutso? Koma masiku otsiriza ano walankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Ndi mwa Iyeyu Mulungu adalenga zolengedwa zonse, namuika kuti alandire zinthu zonse ngati choloŵa chake. Iye ndiye kuŵala koonetsa ulemerero wa Mulungu, ndipo ndiye chithunzi chenicheni chosonyeza khalidwe la Mulungu. Iyeyu amachirikiza zonse ndi mau ake amphamvu. Atayeretsa mtundu wa anthu pakuŵachotsa machimo, adakakhala Kumwamba, ku dzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:14

Tiyeni tsono, tigwiritse chikhulupiriro chimene timavomereza. Pakuti tili naye Mkulu wa ansembe wopambana, amene adapita mpaka kukafika kumwamba kwenikweni kwa Mulungu. Iyeyu ndi Yesu, Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:20

Tikudziŵa kuti Mwana wa Mulungu adafika, ndipo adatipatsa nzeru kuti timdziŵe Mulungu woona. Ndipo tili mwa Mulungu woonayo, chifukwa tili mwa Mwana wake Yesu Khristu. Iyeyo ndiye Mulungu woona ndiponso moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:8

“Ine ndine Woyamba ndiponso Wotsiriza,” akutero Ambuye Mulungu, Mphambe, amene alipo, amene analipo kale, amene alikudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:13

Alefa ndi Omega ndine. Ndiye kuti Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimalizo ndine.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:16

Simoni Petro adayankha kuti, “Inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja, Mwana wa Mulungu wamoyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:51

Ine ndine chakudya chamoyo chimene chidatsika kuchokera Kumwamba. Munthu wodya chakudyachi, adzakhala ndi moyo mpaka muyaya. Ndipo chakudyacho chimene Ine ndidzapereka ndi thupi langa, limene ndikulipereka kuti anthu a pa dziko lonse lapansi akhale ndi moyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:25

Yesu adamuuza kuti, “Woukitsa anthu kwa akufa ndiponso woŵapatsa moyo ndine. Munthu wokhulupirira Ine, ngakhale afe adzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:6

Ndipotu ndikunenetsa kuti pali wina pano woposa Nyumba ya Mulunguyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:61-62

Yesu adangokhala chete, osayankha kanthu. Pamenepo mkulu wa ansembe uja adafunsanso kuti, “Kodi ndiwedi Mpulumutsi wolonjezedwa uja, Mwana wa Mulungu Wolemekezeka?” Yesu adayankha kuti, “Inde, ndinedi. Ndipo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvuzonse. Mudzamuwona akubwera pa mitambo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:35

Mumtambomo mudamveka mau akuti, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndidamsankha, muzimumvera.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:22

“Atate adaika zonse m'manja mwanga. Palibe wina wodziŵa Mwana kupatula Atate okha. Palibenso wina wodziŵa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuululira.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Mulungutu adaŵakonda kwambiri anthu a pa dziko lonse lapansi. Anali naye Mwana mmodzi yekha, komabe adampereka kuti aliyense wokhulupirira Iyeyo asatayike, koma akhale ndi moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:22

Atate saweruza munthu aliyense, koma adaika Mwana wake kuti akhale woweruza pa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu adamuyankha kuti, “Ineyo ndine njira, ndine choona ndiponso moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate ngati sadzera mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:9

Ngati uvomereza ndi pakamwa pako kuti Yesu ndi Ambuye, ndipo ukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu adamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:6

Koma kwa ife, Mulungu ndi mmodzi yekha, ndiye Atate, amene adalenga zonse, ndipo moyo wathu umalinga kwa Iye. Tilinso ndi Ambuye amodzi okha, Yesu Khristu. Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, ndipo ife tili ndi moyo chifukwa cha Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 12:3

Nchifukwa chake ndikukuuzani kuti munthu amene Mzimu wa Mulungu amamtsogolera, sanganene kuti, “Yesu atembereredwe.” Ndiponso, munthu amene Mzimu Woyera samtsogolera, sanganene kuti, “Yesu ndi Ambuye.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:19

Ndiye kuti mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi ndi Iye mwini, osaŵaŵerengera machimo ao. Ndipo adatipatsa ifeyo mau onena za chiyanjanitsocho kuti tiŵalalike.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndidapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano m'thupi lino, ndi moyo wokhulupirira Mwana wa Mulungu, amene adandikonda napereka moyo wake chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:20-21

Ulemerero ukhale kwa Mulungu amene, mwa mphamvu yake yogwira ntchito mwa ife, angathe kuchita zochuluka kupitirira kutalitali zimene tingazipemphe kapena kuziganiza. Mulungu alandire ulemuwo mu Mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibadwo yonse mpaka muyaya. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:1

Tsono ngati mudaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mtima pa zinthu za Kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:4

Bwerani kwa Iye amene ali mwala wamoyo womwe anthu adaukana, koma Mulungu adausankha kuti ngwamtengowapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:2

Moyowo udaoneka, ndipo ife tidauwona. Tikuuchitira umboni, ndipo tikukulalikirani za moyo wosatha, umene unali kwa Atate ndipo udatiwonekera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:2

Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: aliyense wovomereza kuti Yesu Khristu adadzakhaladi munthu, ameneyo ndi wochokera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:12

Ndipo palibe wina aliyense amene angathe kupulumutsa anthu, pakuti pa dziko lonse lapansi palibe dzina lina limene Mulungu adapatsa anthu kuti tipulumuke nalo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:31

Iwo adamuyankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka iwe ndi a m'nyumba mwako.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:16

Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino ai, chifukwa Uthengawo ndi mphamvu ya Mulungu yopulumutsa munthu aliyense wokhulupirira, poyamba Ayuda, pambuyo pake anthu a mitundu ina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 7:3

Za bambo wake kapena mai wake, kapena makolo ake, palibe chilichonse chidalembedwa. Chimodzimodzi za kubadwa kwake ndi imfa yakenso. Ali ngati Mwana wa Mulungu, akupitiriza kukhala wansembe mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:12

Koma Khristu adapereka nsembe imodzi yokha yochotsera machimo onse. Ndipo ataipereka, adakakhala ku dzanja lamanja la Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:5

Pajatu Mulungu ndi mmodzi yekha, Mkhalapakati mmodzi yekhanso pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja timati Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:13

Pajatu tikudikira tsiku lodala, pamene zidzachitike zimene tikuyembekeza, pamene Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu adzaonetsa ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 5:12

Ndidamva angelowo akuimba mokweza mau kuti, “Mwanawankhosa amene adaaphedwayu, ngwoyenera kulandira mphamvu, chuma, nzeru, nyonga, ulemu, ulemerero ndi chiyamiko.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:16

Pa mkanjo wake, ndi pantchafu pake padaalembedwa dzina loti, “Mfumu ya mafumu onse, ndi Mbuye wa ambuye onse.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 2:11

Adaloŵa m'nyumba, naona mwanayo ali ndi Maria mai wake, ndipo adagwada nampembedza. Kenaka adamasula chuma chao, nampatsa mitulo ya golide, lubani ndi mafuta onunkhira a mure.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 17:5

Akulankhula choncho, kudadza mtambo woŵala nuŵaphimba. Mumtambomo mudamveka mau akuti, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimamkonda, ndipo ndimakondwera naye kwambiri. Muzimumvera.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:19

Nchifukwa chake inu pitani kwa anthu a mitundu yonse, mukaŵasandutse ophunzira anga. Muzikaŵabatiza m'dzina la Atate, ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:1

Uwu ndi Uthenga Wabwino wonena za Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 9:7

Tsono padafika mtambo, nuŵaphimba, ndipo mumtambomo mudamveka mau akuti, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimamkonda, muzimumvera.”?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:41

Nayonso mizimu yoipa inkatuluka mwa anthu ambiri ikufuula nkumanena kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu.” Koma Iye adaidzudzula, osailola kuti ilankhule, chifukwa idaadziŵa kuti analidi Mpulumutsi wolonjezedwa uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 12:41

Yesaya ponena mau amenewo, ankanena za Yesu, chifukwa adaaona ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:5

Ndipo tsopano Inu Atate mundilemekeze pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu lisanalengedwe dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:24

“Atate, ndifuna kuti amene mudandipatsa, iwonso akhale pamodzi ndi Ine kumene ndili. Ndifuna kuti aone ulemerero wanga umene mudandipatsa, chifukwa mudandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31-32

Nanga tsono tinganenenso chiyani pa zonsezi? Ngati Mulungu ali pa mbali yathu, angatsutsane nafe ndani? Iye sadaumire ngakhale Mwana wakewake, koma adampereka chifukwa cha ife tonse. Atatipatsa Mwana wakeyo, nanga Iye nkulephera kutipatsanso zonse mwaulere?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:14

Madalitso a Ambuye Yesu Khristu ndi chikondi cha Mulungu ndiponso chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:3

Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:18

Tsopano kudzera mwa Khristu ife tonse, Ayuda ndi a mitundu ina, tingathe kufika kwa Atate mwa Mzimu Woyera mmodzi yemweyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:19

Mulungu wanga ali ndi chuma chochuluka, ndipo mwa Khristu Yesu adzakupatsani zonse zimene mukusoŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:27

Cholinga cha Mulungu ndi cha kudziŵitsa anthuwo kukoma kwake kwa chinsinsicho ndi ulemerero wake pakati pa anthu akunja. Chinsinsicho nchakuti Khristu ali mwa inu, ndipo Iye amakupatsani chiyembekezo cha kudzalandira ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:3

Mwa Iyeyu mudzapeza chuma chonse chobisika, ndiye kuti nzeru ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 1:10

Tsopano mukudikira Mwana wake kuti abwerenso kuchokera Kumwamba. Mwana wakeyo ndi Yesu, amene Mulungu adamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ulikudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 1:1

Ndine, Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu, monga adalamulira Mulungu, Mpulumutsi wathu, ndiponso Khristu Yesu, chiyembekezo chathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:4

Ndikulembera iwe Tito, mwana wanga weniweni chifukwa choti ineyo ndi iwe tili m'chikhulupiriro chimodzimodzi. Mulungu Atate ndi Khristu Yesu, Mpulumutsi wathu, akukomere mtima ndi kukupatsa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:1

Abale, ndinu oyera ake a Mulungu, inuyo adakuitanani kuti nanunso mukhale ndi moyo wakumwamba. Nchifukwa chake muzisinkhasinkha za Yesu, mtumwi wa Mulungu, ndiponso Mkulu wa ansembe onse wa chikhulupiriro chimene timavomereza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:6

Ndipotu popanda chikhulupiriro nkosatheka kukondweretsa Mulungu. Paja aliyense wofuna kuyandikira kwa Mulungu, ayenera kukhulupirira kuti Mulunguyo alipodi, ndipo kuti amaŵapatsa mphotho anthu omufunafuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:3

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu. Iye mwa chifundo chake chachikulu adatibadwitsanso pakuukitsa Yesu Khristu kwa akufa. Motero timakhulupirira molimba mtima

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:23

Aliyense wokana Mwana, alibenso Atate. Wovomereza Mwana, alinso ndi Atate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:11-12

Umboniwo tsono ndi wakuti Mulungu adatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowo umapezeka mwa Mwana wake. Amene ali ndi Mwanayo, ali nawo moyo. Amene sali ndi Mwana wa Mulungu, alibe moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 1:8

Koma mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera akadzabwera pa inu, ndipo mudzakhala mboni zanga ku Yerusalemu, ku Yudeya ndi ku Samariya konse, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:36

“Tsono Aisraele onse adziŵe ndithu kuti Yesu uja inu mudampachika pamtandayu, Mulungu adamsankhula kuti akhale Ambuye ndi Mpulumutsi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:42

Ndipo adatilamula kuti tikalalikire anthu onse, ndi kuchita umboni kuti Iyeyo ndiye amene Mulungu adamsankha kukhala Woweruza anthu amoyo ndi akufa omwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:10

Ife tinali adani a Mulungu, koma imfa ya Mwana wake idatiyanjanitsa ndi Iye. Tsono popeza kuti imfa ya Khristu idatiyanjanitsa ndi Mulungu, nanji tsono moyo wake, ndiye udzatipulumutsa kwenikweni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:23

Malipiro amene uchimo umalipira ndi imfa. Koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:9

Koma ndi monga Malembo anenera kuti, “Maso a munthu sanaziwone, makutu a munthu sanazimve, mtima wa munthu sunaganizepo konse zimene Mulungu adaŵakonzera amene amamkonda.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:57

Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:26

Nonsenu ndinu ana a Mulungu chifukwa mumakhulupirira Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:7

Ndi imfa ya Mwana wakeyo Mulungu adatipulumutsa, adatikhululukira machimo athu. Nzazikuludi mphatso zaulere

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:3-4

Pakuti kunena za moyo wakalewo mudafa, ndipo moyo wanu watsopano ndi wobisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. Khristu ndiye moyo wanu weniweni tsopano, choncho pamene Iye adzaonekerenso, inunso mudzaonekera mu ulemerero pamodzi naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:14-15

Ndikukulamula kuti, mopanda cholakwa kapena chokayikitsa, utsate bwino zonse zimene udalamulidwa, mpaka Ambuye athu Yesu Khristu adzabwerenso. Pa nthaŵi yake Mulungu adzamuwonetsa kwa ife. Mulunguyo ngwodala ndipo Iye yekha ndiye Wolamula, ndiye Mfumu ya mafumu onse, ndiponso Mbuye wa ambuye onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:8

Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:10

Koma mutamva zoŵaŵa pa kanthaŵi, Mulungu mwini amene nthaŵi zonse amakukomerani mtima, adzakukonzaninso, nadzakukhazikitsani pa maziko olimba. Ndiye amene adakuitanani, kuti pokhala limodzi ndi Khristu, mukalandire ulemerero wake wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:1

Onani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate adatikonda nacho. Adatikonda kwambiri, kotero kuti timatchedwa ana a Mulungu. Ndipo ndifedi ana ake. Anthu odalira zapansipano satidziŵa ifeyo, chifukwa Iyeyonso sadamdziŵe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:15

Aliyense wovomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye, ndipo iye amakhala mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 7:10

Ankafuula mokweza mau kuti, “Chipulumutso nchochokera kwa Mulungu wathu wokhala pa mpando wachifumu, ndiponso kwa Mwanawankhosa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:15

Pambuyo pake mngelo wachisanu ndi chiŵiri adaliza lipenga lake. Atatero kumwamba kudamveka mau okweza. Mauwo adati, “Tsopano mphamvu zolamulira dziko lapansi zili m'manja mwa Ambuye athu ndi mwa Wodzozedwa wake uja, ndipo adzalamulira mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:20

Amene akufotokoza zimenezi akuti, “Indedi, ndikubwera posachedwa.” Inde, bwerani, Ambuye Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:36

Inetu Atate adandipatula nandituma pansi pano. Tsono inuyo munganene bwanji kuti ndikunyoza Mulungu, chifukwa ndati ndine Mwana wa Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wachilungamo, ndinu wamkulu komanso wodabwitsa, inu amene mukhala pampando wachifumu mutavala ulemerero ndi mphamvu, inu woposa zonse ndiponso wangwiro pa zonse zimene muchita. Yesu wokondedwa ndikubwerera kwa inu, chifukwa inu nokha muli ndi ulemerero, mphamvu ndi ufumu, ndikupemphani mundidzetse ndi kukhalapo kwanu ndipo Mzimu wanu Woyera uwonekere pa moyo wanga. Ndithandizeni kutsatira chikhulupiriro chanu ndi kumvera kulikonse kumene ndikupita ndipo kukhalapo ndi Mphamvu ya Mzimu wanu Woyera zikhale zooneka pa moyo wa omwe akumva mawu anu mkamwa mwanga. Mawu anu amati: “Pamenepo amene anali m’ngalawa anamulambira Iye, nanena, Zoonadi ndinu Mwana wa Mulungu.” Mundiphunzitse Yesu kuyenda monga momwe munayendera, kuchiritsa odwala, kumasula ogwidwa ndi kuthandiza onse otsenderezedwa. Munandipulumutsa ku mphamvu ya mdima, Yesu ndinu Mwana wa Mulungu, mkhalapakati pakati pa Mulungu ndi munthu, zikomo chifukwa munadzipereka chifukwa cha chikondi cha anthu polipira mtengo wapatali chifukwa cha machimo athu. Zikomo chifukwa chosandisiya konse komanso kundifuna nthawi zonse. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa