Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


147 Mau a Mulungu Pa Nzeru ndi Miyambi

147 Mau a Mulungu Pa Nzeru ndi Miyambi


Miyambo 1:7

Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako; umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:16

Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:20

Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:10

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:8

Wolandira nzeru akonda moyo wake; wosunga luntha adzapeza zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:1

Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; koma mau owawitsa aputa msunamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:19

Pochuluka mau zolakwa sizisoweka; koma wokhala chete achita mwanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:27

Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa; ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:11

Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:3

Wochenjera aona zoipa, nabisala; koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13-14

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:11

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:22

Zolingalira zizimidwa popanda upo; koma pochuluka aphungu zikhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:1

Wokonda mwambo akonda kudziwa; koma wakuda chidzudzulo apulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:3-4

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa. Ndinapita pa munda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru. Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona, ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa. Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:12

Pakuti nzeru itchinjiriza monga ndalama zitchinjiriza; koma kudziwa kupambana, chifukwa nzeru isunga moyo wa eni ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:23

Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa; koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:15

Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:11

Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo; ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:23

Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; pakuti magwero a moyo atulukamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:8

Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:16

Wanzeru amaopa nasiya zoipa; koma wopusa amanyada osatekeseka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:14

Nyumba ndi chuma ndizo cholowa cha atate; koma mkazi wanzeru achokera kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:15

Alipo golide ndi ngale zambiri; koma milomo yodziwa ndiyo chokometsera cha mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:5

Zoganizira za wakhama zichulukitsadi katundu; koma yense wansontho angopeza umphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:17

Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru, nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:5

Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; munthu wodziwa ankabe nalimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:7

Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:1-2

Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga; motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake; pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye. Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka. Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere. Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha. pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:9

Ukachenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yake; ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:1

Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru akondweretsa atate; koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:30

Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo; ndipo wokola mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:1

Mkazi yense wanzeru amanga banja lake; koma wopusa alipasula ndi manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:8

Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:12

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:14

Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:31

Khutu lomvera chidzudzulo cha moyo lidzakhalabe mwa anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:20

Wolabadira mau adzapeza bwino; ndipo wokhulupirira Yehova adala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:24

Nzeru ili pamaso pa wozindikira; koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:4

Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya; kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:6-7

Milomo ya wopusa ifikitsa makangano; ndipo m'kamwa mwake muputa kukwapulidwa. M'kamwa mwa wopusa mumuononga, milomo yake ikhala msampha wa moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:2

Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino; ndipo wofulumira ndi mapazi ake amachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:1

Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa; wosochera nazo alibe nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:1

Mbiri yabwino ifunika kopambana chuma chambiri; kukukomera mtima anzako kuposa siliva ndi golide.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:23

Gula ntheradi, osaigulitsa; nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:6

Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo, ndi kupulumuka pochuluka aphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:12

Monga mphete yagolide ndi chipini chagolide woyengeka, momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:12

Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru? Ngakhale chitsiru chidzachenjera koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:16

Zapang'ono, ulikuopa Yehova, zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:5-6

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga; usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:21-22

Mwananga, zisachokere kumaso ako; sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira; ndipo mtima wako udzatengapo moyo, ndi khosi lako chisomo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:3

Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:14

Popanda upo wanzeru anthu amagwa; koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:10

Chidzudzulo chilowa m'kati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:32

Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mudzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:1

Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:18

Uphungu utsimikiza zolingalira, ponya nkhondo utapanga upo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:10

Ukalefuka tsiku la tsoka mphamvu yako ichepa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:4

Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake; koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:12

Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima; koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:9

Wobisa cholakwa afunitsa chikondano; koma wobwerezabwereza mau afetsa ubwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:2

Wopusa sakondwera ndi kuzindikira; koma kungovumbulutsa za m'mtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:21

Lilime lili ndi mphamvu pa imfa ndi moyo; wolikonda adzadya zipatso zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:6

Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwake; koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:28

Wosalamulira mtima wake akunga mudzi wopasuka wopanda linga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:20

Posowa nkhuni moto ungozima; ndi popanda kazitape makangano angoleka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:20

Kodi uona munthu wansontho m'mau ake? Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:26

Pakuti yemwe Mulungu amuyesa wabwino ampatsa nzeru ndi chidziwitso ndi chimwemwe; koma wochimwa amlawitsa vuto la kusonkhanitsa ndi kukundika, kuti aperekere yemwe Mulungu amuyesa wabwino. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:5

Kumva chidzudzulo cha anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:13

Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:1

Usanyadire zamawa, popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:16

Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa; koma wanzeru amabisa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:25

Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu; koma mau abwino aukondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:4

Kuchiza lilime ndiko mtengo wa moyo; koma likakhota liswa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:17

Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:6

Phunzitsa mwana poyamba njira yake; ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:13

Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi; koma wokhulupirika mtima abisa mau.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:20

Chinyengo chili m'mitima ya oganizira zoipa; koma aphungu a mtendere amakondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:21

Wonyoza anzake achimwa; koma wochitira osauka chifundo adala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:24

Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:24

Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:24-25

Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali; kuti ungaphunzire mayendedwe ake, ndi kutengera moyo wako msampha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:15-16

Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru, mtima wanga wa inedi udzakondwa. Imso zanga zidzasangalala, polankhula milomo yako zoongoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:11

Mau oyenera a pa nthawi yake akunga zipatso zagolide m'nsengwa zasiliva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:27

Wokumba dzenje adzagwamo, wogubuduza mwala, udzabweranso pa iye mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:17

Chitsulo chinola chitsulo; chomwecho munthu anola nkhope ya mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:10

Chitsulo chikakhala chosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pochenjeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:13

Wobisa machimo ake sadzaona mwai; koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:23

Kuopa Yehova kupatsa moyo; wokhala nako adzakhala wokhuta; zoipa sizidzamgwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:17

Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo; koma wosiya chidzudzulo asochera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:25

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:23

Wosunga m'kamwa mwake ndi lilime lake asunga moyo wake kumavuto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:12

Wochenjera aona zoipa, nabisala; koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:13

Mtima wokondwa usekeretsa nkhope; koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:35

Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:1

Muyeso wonyenga unyansa Yehova; koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Yehova azida; ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa: Maso akunyada, lilime lonama, ndi manja akupha anthu osachimwa; mtima woganizira ziwembu zoipa, mapazi akuthamangira mphulupulu m'mangum'mangu; mboni yonama yonong'ona mabodza, ndi wopikisanitsa abale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:27

Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova; usanthula m'kati monse mwa mimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:25

Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:3

Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake; koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:24

Wolekerera mwanake osammenya amuda; koma womkonda amyambize kumlanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:12

Lozetsa mtima wako kumwambo, ndi makutu ako ku mau anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:23

M'ntchito zonse muli phindu; koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:7

Wolemera alamulira osauka; ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:10

Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:20

Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri; koma wokangaza kulemera sadzapulumuka chilango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:4

Mphotho ya chifatso ndi kuopa Yehova ndiye chuma, ndi ulemu, ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:11

Zakudya zikwanira wolima minda yake; koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:4

Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:15

Wachibwana akhulupirira mau onse; koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:29

Kodi upenya munthu wofulumiza ntchito zake? Adzaima pamaso pa mafumu, osaima pamaso pa anthu achabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:2

Njira zonse za munthu zilungama pamaso pake; koma Yehova ayesa mitima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:18

Wosunga mkuyu adzadya zipatso zake; wosamalira ambuyake adzalemekezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:25

Mtima wa mataya udzalemera; wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:17

Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:5

Oipa samvetsetsa chiweruzo; koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:22

Madalitso a Yehova alemeretsa, saonjezerapo chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:13

Wotseka makutu ake polira waumphawi, nayenso adzalira koma osamvedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:27

Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo, kupatutsa kumisampha ya imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:9

Mwini diso lamataya adzadala; pakuti apatsa osauka zakudya zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:27-28

Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso, ndipo mawa ndidzakupatsa; pokhala uli nako kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:29

Yehova atalikira oipa; koma pemphero la olungama alimvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:18-19

Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee. Njira ya oipa ikunga mdima; sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:3

Maso a Yehova ali ponseponse, nayang'anira oipa ndi abwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:17

Wokonda zoseketsa adzasauka; wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:17-18

Mtima wako usachitire nsanje akuchimwawo; koma opabe Yehova tsiku lonse. Pakutitu padzakhala mphotho; ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:23

Udziwitsitse zoweta zako zili bwanji, samalira magulu ako;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:11

Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova; ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:19-20

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha. pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake; thambo ligwetsa mame.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:5

Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; wolankhula mabodza sadzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:3-4

Chifundo ndi choonadi zisakusiye; uzimange pakhosi pako; uzilembe pamtima pako; Usakangane ndi munthu chabe, ngati sanakuchitire choipa. Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; koma chinsinsi chake chili ndi oongoka. Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama. Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo. Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi. motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino, pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa