Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


131 Mau a Mulungu Okhudza Kutambalika

131 Mau a Mulungu Okhudza Kutambalika

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, kutamanda Mulungu kumatanthauza kuvomereza zabwino zonse zimene Mulungu watichitira. Timamuyamika chifukwa cha mphamvu zake zopambana zonse ndipo nthawi zonse timakweza dzina lake.

Ngati tili mu utumiki wotamanda Mulungu, tiyenera kukhala pa ubwenzi ndi Mzimu Woyera nthawi zonse. Chifukwa kudzera mu ubwenzi ndi Iye, timadziwa bwino Mulungu m'miyoyo yathu. Timam'tamanda chifukwa cha zimene tazidziwa tokha, osati zimene tamva kwa ena. Umu ndi momwe timatamanditsira Mulungu Wamuyaya ndikutsogolera anthu kuti amulemekeze ndi kumukweza.

Mwayi wotamanda Mulungu si wa aliyense. Choncho, ndikofunikira kusunga mitima yathu yoyera ndi kupita pamaso pa Mulungu opanda chilema. Tisachite chilichonse chomwe chingatichititse manyazi. Tiyenera kuyamikira mwayi wotumikira Mulungu ndi kumupatsa ulemerero nthawi zonse. Tiyenera kulola kuti nyimbo zatsopano zotamanda Yesu zizituluka m'kamwa mwathu.

Komanso, tiyenera kukumbukira kuti monga atumiki, tiyenera kutetezerana ndikudikirirana kuti mdani asatiipitse. Tiyenera kuyang'ana pa zinthu zoyera, zabwino, ndi zolungama. Monga thupi limodzi, cholinga chathu chikhale choti dzina la Mulungu litamandike pakati pa anthu amoyo.




Yesaya 42:8

Ine ndine Yehova; dzina langa ndi lomweli; ndipo ulemerero wanga Ine sindidzapereka kwa wina, ngakhale kunditamanda kwa mafano osemedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:12

Zowindira Inu Mulungu, zili pa ine, ndidzakuchitirani zoyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:15

Ambuye, tsegulani pa milomo yanga; ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:25

Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukulu, zowinda zanga ndidzazichita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:8

M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu, ndi ulemu wanu tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 149:1

Aleluya, Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano, ndi chilemekezo chake mu msonkhano wa okondedwa ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:1

Aleluya; Ulemekeze Yehova, moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 113:1

Aleluya; Lemekezani, inu atumiki a Yehova; lemekezani dzina la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:1

Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse; ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:21

Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha, ndipo munakhala chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:2

Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:12

kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:4

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:6

Inu munandigwiriziza kuyambira ndisanabadwe, kuyambira pa thupi la mai wanga wondichitira zokoma ndinu; ndidzakulemekezani kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:1-2

Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzawerengera zodabwitsa zanu zonse. ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu; pakuti, Inu Yehova, simunawasiya iwo akufuna Inu. Imbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni; lalikirani mwa anthu ntchito zake. Pakuti Iye wofuna chamwazi awakumbukira; saiwala kulira kwa ozunzika. Ndichitireni chifundo, Yehova; penyani kuzunzika kwanga kumene andichitira ondidawo, inu wondinyamula kundichotsa kuzipata za imfa. Kuti ndibukitse lemekezo lanu lonse; pa bwalo la mwana wamkazi wa Ziyoni, ndidzakondwera nacho chipulumutso chanu. Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba, lakodwa phazi lao muukonde anautcha. Anadziwika Yehova, anachita kuweruza, woipayo anakodwa ndi ntchito ya manja ake. Oipawo adzabwerera kumanda, inde amitundu onse akuiwala Mulungu. Pakuti sadzaiwalika nthawi zonse waumphawi, kapena chiyembekezo cha ozunzika sichidzaonongeka kosatha. Ukani, Yehova, asalimbike munthu; amitundu aweruzidwe pankhope panu. Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu; ndidzaimbira dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 7:17

Ndidzayamika Yehova monga mwa chilungamo chake; ndipo ndidzaimbira Yehova Wam'mwambamwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:1

Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzawerengera zodabwitsa zanu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:7

muja nyenyezi za m'mawa zinaimba limodzi mokondwera, ndi ana onse a Mulungu anafuula ndi chimwemwe?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:30

Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliimbira, ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:3

Ndidzaitanira Yehova, woyenera kutamandika, ndipo adzandipulumutsa ine kwa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:13

Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 57:9

Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye, ndidzakuimbirani mwa mitundu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 8:18

Ndipo tatuma pamodzi naye mbaleyo, amene kusimba kwake m'Uthenga Wabwino kuli m'Mipingo yonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:3

Koma Inu ndinu woyera, wakukhala m'malemekezo a Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 11:17

ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu, ndiye mkulu wakuyamba mayamiko, popemphera; ndi Bakibukiya wotsatana naye mwa abale ake, ndi Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 9:5

Nati Alevi, Yesuwa, ndi Kadimiyele, Bani, Hasabineya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya, ndi Petahiya, Imirirani, lemekezani Yehova Mulungu wanu kunthawi za nthawi; ndipo lilemekezeke dzina lanu la ulemerero, lokuzika loposa chilemekezo ndi chiyamiko chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 33:16

Namanga guwa la nsembe la Yehova, napherapo nsembe zamtendere ndi zoyamika, nalamulira Yuda atumikire Yehova Mulungu wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:4

Imbirani Yehova, inu okondedwa ake, ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 25:6

Onsewa anawalangiza ndi atate wao aimbe m'nyumba ya Yehova ndi nsanje, zisakasa ndi azeze; atumikire nazo m'nyumba ya Mulungu; ndipo Asafu, Yedutuni, ndi Hemani, anawalangiza ndi mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 6:32

Ndipo anatumikira ndi kuimba pakhomo pa Kachisi wa chihema chokomanako mpaka Solomoni adamanga nyumba ya Yehova m'Yerusalemu, naimirira m'utumiki wao monga mwa malongosoledwe ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 12:27

Ndipo popereka linga la Yerusalemu anafunafuna Alevi m'malo mwao monse, kubwera nao ku Yerusalemu, kuti achite kuperekaku mokondwera, ndi mayamiko, ndi kuimbira, ndi nsanje, zisakasa, ndi azeze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 12:8

Ndi Alevi ndiwo Yesuwa, Binuyi, Kadimiyele, Serebiya, Yuda, ndi Mataniya; iye ndi abale ake amatsogolera mayamiko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 12:46

Pakuti m'masiku a Davide ndi Asafu kalelo kunali mkulu wa oimbira, ndi wa nyimbo zolemekeza ndi zoyamikira Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:1

Fuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima, oongoka mtima ayenera kulemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 23:5

ndi zikwi zinai odikira; ndi zikwi zinai analemekeza Yehova ndi zoimbira zimene ndinazipanga, anati Davide, kuti alemekeze nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 20:22

Ndipo poyamba iwo kuimba, ndi kulemekeza Yehova, anaika olalira alalire Aamoni, Amowabu, ndi a m'phiri la Seiri, akudzera Ayuda; ndipo anawakantha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 29:31

Pamenepo Hezekiya anayankha, nati, Tsopano mwadzipatulira kwa Yehova, senderani, bwerani nazo nsembe zophera ndi nsembe zoyamika kunyumba ya Yehova. Ndi msonkhano unabwera nazo nsembe zophera ndi nsembe zoyamika, ndi onse a mtima wofuna mwini anabwera nazo nsembe zopsereza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 23:13

napenya, ndi kuona mfumu inaima pa nsanamira yake polowera; ndi atsogoleri, ndi malipenga, anali kwa mfumu; ndi anthu onse a m'dziko anakondwera, naomba amalipenga; oimbira omwe analiko ndi zoimbirazo, nalangiza poimbira cholemekeza. Pamenepo Ataliya anang'amba zovala zake, nati, Chiwembu, chiwembu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 23:30

ndi kuimirira m'mawa ndi m'mawa kuyamika ndi kulemekeza Yehova, momwemonso madzulo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:1-3

Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse; kumlemekeza kwake kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza. Misona ya mkango isowa nimva njala, koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino. Idzani ananu ndimvereni ine, ndidzakulangizani zakumuopa Yehova. Munthu wokhumba moyo ndani, wokonda masiku, kuti aone zabwino? Uletse lilime lako lisatchule zoipa, ndipo milomo yako isalankhule chinyengo. Futuka pazoipa, nuchite zabwino, funa mtendere ndi kuulondola. Maso a Yehova ali pa olungama mtima, ndipo makutu ake atchereza kulira kwao. Nkhope ya Yehova itsutsana nao akuchita zoipa, kudula chikumbukiro chao pa dziko lapansi. Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva, nawalanditsa kumasautso ao onse. Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, apulumutsa iwo a mzimu wolapadi. Masautso a wolungama mtima achuluka, koma Yehova amlanditsa mwa onsewa. Moyo wanga udzatamanda Yehova; ofatsa adzakumva nadzakondwera. Iye asunga mafupa ake onse; silinathyoka limodzi lonse. Mphulupulu idzamupha woipa; ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama. Yehova aombola moyo wa anyamata ake, ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye. Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 47:1-2

Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa. Pakuti Yehova Wam'mwambamwamba ndiye woopsa; ndiye mfumu yaikulu pa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 7:6

Naimirira ansembe m'udikiro wao; ndi Alevi omwe ndi zoimbira za Yehova, adazipanga Davide mfumu kuyamika nazo Yehova, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire, polemekeza Davide mwa utumiki wao; ndi ansembe anaomba malipenga pamaso pao, nakhala chilili Israele yense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 48:1

Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi, m'mudzi wa Mulungu wathu, m'phiri lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:23

Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine; ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:3-4

Pakuti chifundo chanu chiposa moyo makomedwe ake; milomo yanga idzakulemekezani. Potero ndidzakuyamikani m'moyo mwanga; ndidzakweza manja anga m'dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 65:1-2

M'Ziyoni akulemekezani Inu mwachete, Mulungu, adzakuchitirani Inu chowindachi. Mukhutitsa nthaka yake yolima; mufafaniza nthumbira zake; muiolowetsa ndi mvumbi; mudalitsa mmera wake. Muveka chakachi ndi ukoma wanu; ndipo mabande anu akukha zakucha. Akukha pa mabusa a m'chipululu; ndipo mapiri azingika nacho chimwemwe. Podyetsa mpodzaza ndi zoweta; ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu; zifuula mokondwera, inde ziimbira. Wakumva pemphero Inu, zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:4

Imbirani Yehova, liimbireni nyimbo dzina lake; undirani mseu Iye woberekekayo kuchidikha; dzina lake ndiye Yehova; ndipo tumphani ndi chimwemwe pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:28

Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu. Ndimuyesa Ambuye Yehova pothawirapo ine, kuti ndifotokozere ntchito zanu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:1

Tikuyamikani Inu, Mulungu; tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi; afotokozera zodabwitsa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 79:13

Potero ife anthu anu ndi nkhosa zapabusa panu tidzakuyamikani kosatha; tidzafotokozera chilemekezo chanu ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:4

Odala iwo akugonera m'nyumba mwanu; akulemekezani chilemekezere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 86:12

Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:1-2

Tiyeni tiimbire Yehova mokondwera; tifuule kwa thanthwe la chipulumutso chathu. Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa chisoni, ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, ndipo sadziwa njira zanga. Chifukwa chake ndinalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga. Tidze nacho chiyamiko pamaso pake, timfuulire Iye mokondwera ndi nyimbo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:1-2

Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi. Nenani mwa amitundu, Yehova achita ufumu; dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke; adzaweruza mitundu ya anthu molunjika. Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi; nyanja ibume mwa kudzala kwake. Munda ukondwerere ndi zonse zili m'mwemo; pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera. Pamaso pa Yehova, pakuti akudza; pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo, ndi mitundu ya anthu ndi choonadi. Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:12

Kondwerani mwa Yehova, olungama inu; ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 98:1-3

Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; popeza anachita zodabwitsa: Dzanja lake lamanja, mkono wake woyera, zinamchitira chipulumutso. Yehova anawadziwitsira chipulumutso chake; anaonetsera chilungamo chake pamaso pa amitundu. Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake kunyumba ya Israele; malekezero onse a dziko lapansi anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:1-5

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi. Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera. Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu; Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake. Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake. Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:1-2

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera. Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu, kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu. Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi, motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye. Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu. Monga atate achitira ana ake chifundo, Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye. Popeza adziwa mapangidwe athu; akumbukira kuti ife ndife fumbi. Koma munthu, masiku ake akunga udzu; aphuka monga duwa la kuthengo. Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe: Ndi malo ake salidziwanso. Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana; kwa iwo akusunga chipangano chake, ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita. Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo. Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:33

Ndidzaimbira Yehova m'moyo mwanga: ndidzaimbira Mulungu wanga zomlemekeza pokhala ndilipo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 105:1-3

Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lake; bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye. ndipo anachiimikira Yakobo, chikhale malemba, chikhale chipangano chosatha kwa Israele. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani, gawo la cholandira chako; pokhala iwo anthu owerengeka, inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo; nayendayenda kuchokera mtundu wina kufikira mtundu wina, kuchokera ufumu wina kufikira anthu ena. Sanalola munthu awasautse; ndipo anadzudzula mafumu chifukwa cha iwowa. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga, musamachitira choipa aneneri anga. Ndipo anaitana njala igwere dziko; anathyola mchirikizo wonse wa mkate. Anawatsogozeratu munthu; anamgulitsa Yosefe akhale kapolo: Anapweteka miyendo yake ndi matangadza; anamgoneka m'unyolo; kufikira nyengo yakuchitika maneno ake; mau a Yehova anamuyesa. Muimbireni, muimbireni zomlemekeza; fotokozerani zodabwitsa zake zonse. Mfumuyo anatuma munthu nammasula; woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira. Anamuika akhale woyang'anira nyumba yake, ndi woweruza wa pa zake zonse: Amange nduna zake iye mwini, alangize akulu ake adziwe nzeru. Pamenepo Israele analowa m'Ejipito; ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu. Ndipo anachulukitsatu mtundu wa anthu ake, nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa. Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ake, kuti achite monyenga ndi atumiki ake. Anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aroni amene adamsankha. Anaika pakati pao zizindikiro zake, ndi zodabwitsa m'dziko la Hamu. Anatumiza mdima ndipo kunada; ndipo sanapikisane nao mau ake. Anasanduliza madzi ao akhale mwazi, naphanso nsomba zao. Mudzitamandire ndi dzina lake loyera: mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:1

Aleluya. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino: Pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:8-9

Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake, ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu! Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka, nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:1

Aleluya. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse, mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 113:1-3

Aleluya; Lemekezani, inu atumiki a Yehova; lemekezani dzina la Yehova. Lodala dzina la Yehova Kuyambira tsopano kufikira kosatha. Chitulukire dzuwa kufikira kulowa kwake lilemekezedwe dzina la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:17-18

Akufa salemekeza Yehova, kapena aliyense wakutsikira kuli chete: Koma ife tidzalemekeza Yehova kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:1-2

Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha. Amitundu onse adandizinga, zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula. Adandizinga, inde, adandizinga: Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula. Adandizinga ngati njuchi; anazima ngati moto waminga; indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula. Kundikankha anandikankha ndikadagwa; koma Yehova anandithandiza. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndipo anakhala chipulumutso changa. M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso: Dzanja lamanja la Yehova likwezeka, Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu. Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo, ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova. Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai. Nditsegulireni zipata za chilungamo; ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova. Anene tsono Israele, kuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:171

Milomo yanga itulutse chilemekezo; popeza mundiphunzitsa malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 135:1-3

Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova! Lemekezani inu atumiki a Yehova. Ndiye amene anapanda amitundu ambiri, napha mafumu amphamvu; Sihoni mfumu ya Aamori, ndi Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a Kanani: Ndipo anapereka dziko lao likhale chosiyira, chosiyira cha kwa Israele anthu ake. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha; chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake, koma adzaleka atumiki ake. Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golide, ntchito ya manja a anthu. Pakamwa ali napo koma osalankhula; maso ali nao, koma osapenya; makutu ali nao, koma osamva; inde, pakamwa pao palibe mpweya. Akuwapanga adzafanana nao; inde, onse akuwakhulupirira. A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova: A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova: Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu. A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova: Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova. Alemekezedwe Yehova kuchokera m'Ziyoni, amene akhala m'Yerusalemu. Aleluya. Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino; muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:1-2

Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse; ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu. Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:13

Indedi, olungama adzayamika dzina lanu; oongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:1-3

Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi. Ntchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova; ndi okondedwa anu adzakulemekezani. Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu, adzalankhulira mphamvu yanu. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake, ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya, ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonseyonse. Yehova agwiriziza onse akugwa, naongoletsa onse owerama. Maso a onse ayembekeza Inu; ndipo muwapatsa chakudya chao m'nyengo zao. Muolowetsa dzanja lanu, nimukwaniritsira zamoyo zonse chokhumba chao. Yehova ali wolungama m'njira zake zonse, ndi wachifundo m'ntchito zake zonse. Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, onse akuitanira kwa Iye m'choonadi. Adzachita chokhumba iwo akumuopa; nadzamva kufuula kwao, nadzawapulumutsa. Masiku onse ndidzakuyamikani; ndi kulemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi. Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga. Pakamwa panga padzanena chilemekezo cha Yehova; ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lake loyera kunthawi za nthawi. Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ndi ukulu wake ngwosasanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:1-2

Aleluya; Ulemekeze Yehova, moyo wanga. Yehova adzachita ufumu kosatha, Mulungu wako, Ziyoni, ku mibadwomibadwo. Aleluya. Ndidzalemekeza Yehova m'moyo mwanga; ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:1

Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma; pakuti chikondwetsa ichi, chilemekezo chiyenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:1-5

Aleluya. Lemekezani Yehova kochokera kumwamba; mlemekezeni m'misanje. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse; zokwawa, ndi mbalame zakuuluka. Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu; zinduna ndi oweruza onse a padziko. Anyamata ndiponso anamwali; okalamba pamodzi ndi ana. Alemekeze dzina la Yehova; pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka; ulemerero wake uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo. Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake, chilemekezo cha okondedwa ake onse; ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye. Aleluya. Mlemekezeni, angelo ake onse; mlemekezeni, makamu ake onse. Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi; mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira. Mlemekezeni, m'mwambamwamba, ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo. Alemekeze dzina la Yehova; popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 149:1-3

Aleluya, Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano, ndi chilemekezo chake mu msonkhano wa okondedwa ake. Akondwere Israele mwa Iye amene anamlenga; ana a Ziyoni asekere mwa mfumu yao. Alemekeze dzina lake ndi kuthira mang'ombe; amuimbire zomlemekeza ndi lingaka ndi zeze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 150:1-6

Aleluya. Lemekezani Mulungu m'malo ake oyera; mlemekezeni m'thambo la mphamvu yake. Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba; mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji. Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga; mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze. Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang'ombe: Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro. Mlemekezeni ndi nsanje zomveka: Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa. Zonse zakupuma zilemekeze Yehova. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:1-2

Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga. Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:1

Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, chifukwa mwachita zinthu zodabwitsa, ngakhale zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m'zoonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:3

ndikakonzere iwo amene alira maliro m'Ziyoni, ndi kuwapatsa chovala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, chovala cha matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo atchedwe mitengo ya chilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:16

nanena kwa Iye, Mulinkumva kodi chimene alikunena awa? Ndipo Yesu ananena kwa iwo, Inde: simunawerenga kodi, M'kamwa mwa makanda ndi oyamwa munafotokozera zolemekeza?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:46-47

Ndipo Maria anati, Moyo wanga ulemekeza Ambuye, ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 19:37-40

Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake pa phiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau akulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona; nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m'dzina la Ambuye; mtendere m'Mwamba, ndi ulemerero m'Mwambamwamba. Ndipo Afarisi ena a m'khamu la anthu anati kwa Iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu. Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona Iye; pakuti anati apite njira yomweyi. Ndipo anayankha nati, Ndinena ndi inu, ngati awa khala chete miyala idzafuula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 4:24

Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira Iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:47

nalemekeza Mulungu, ndi kukhala nacho chisomo ndi anthu onse. Ndipo Ambuye anawaonjezera tsiku ndi tsiku amene akuti apulumutsidwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:25

Koma ngati pakati pa usiku, Paulo ndi Silasi analinkupemphera, naimbira Mulungu nyimbo, ndipo a m'ndendemo analinkuwamva;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:11

Ndiponso, Tamandani Ambuye, inu a mitundu yonse; ndipo anthu onse amtamande.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:31

Chifukwa chake mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale muchita kanthu kena, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:15

Ayamikike Mulungu chifukwa cha mphatso yakeyake yosatheka kuneneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:19-20

ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuimbira ndi kuimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu; ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino. ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, chifukwa cha zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:4

Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:16-18

Kondwerani nthawi zonse; Pempherani kosaleka; M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:15-16

Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake. Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mwini wake, kotero kuti mukalalikire zoposazo za Iye amene anakuitanani mutuluke mumdima, mulowe kuunika kwake kodabwitsa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 4:11

Muyenera inu, Ambuye wathu, ndi Mulungu wathu, kulandira ulemerero ndi ulemu ndi mphamvu; chifukwa mudalenga zonse, ndipo mwa chifuniro chanu zinakhala, nizinalengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:15

Ndipo mngelo wachisanu ndi chiwiri anaomba lipenga, ndipo panakhala mau akulu m'Mwamba, ndi kunena, Ufumu wa dziko lapansi wayamba kukhala wa Ambuye wathu, ndi wa Khristu wake: ndipo adzachita ufumu kufikira nthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 15:3-4

Ndipo aimba nyimbo ya Mose kapolo wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwanawankhosa, nanena, Ntchito zanu nzazikulu ndi zozizwitsa, Ambuye Mulungu, Wamphamvuyonse; njira zanu nzolungama ndi zoona, Mfumu Inu ya nthawi zosatha. Ndani adzakhala wosaopa ndi wosalemekeza dzina lanu Ambuye? Chifukwa Inu nokha muli woyera; chifukwa mitundu yonse idzadza nidzalambira pamaso panu, popeza zolungama zanu zidaonetsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:1-3

Zitatha izi ndinamva ngati mau akulu a khamu lalikulu m'Mwamba, lili kunena, Aleluya; chipulumutso, ndi ulemerero, ndi mphamvu, nza Mulungu wathu; Ndipo ndinagwa pa mapazi ake kumlambira iye. Ndipo ananena ndi ine, Tapenya, usatero; ine ndine kapolo mnzako, ndi mnzao wa abale ako akukhala nao umboni wa Yesu; lambira Mulungu: pakuti umboni wa Yesu ndiwo Mzimu wa chinenero. Ndipo ndinaona mutatseguka m'Mwamba; ndipo taonani, kavalo woyera, ndi Iye wakumkwera wotchedwa Wokhulupirika ndi Woona; ndipo aweruza, nachita nkhondo molungama. Ndipo maso ake ali lawi la moto, ndi pamutu pake pali nduwira zachifumu zambiri; ndipo ali nalo dzina lolembedwa, wosalidziwa wina yense koma Iye yekha. Ndipo avala chovala chowazidwa mwazi; ndipo atchedwa dzina lake, Mau a Mulungu. Ndipo magulu a nkhondo okhala m'Mwamba anamtsata Iye, okwera pa akavalo oyera, ovala bafuta woyera woti mbu. Ndipo m'kamwa mwake mutuluka lupanga lakuthwa, kuti akanthe nalo mitundu ya anthu; ndipo Iye adzawalamulira ndi ndodo yachitsulo: ndipo aponda Iye moponderamo mphesa mwa vinyo waukali wa mkwiyo wa Mulungu Wamphamvuyonse. Ndipo ali nalo pa chovala chake ndi pa ntchafu yake dzina lolembedwa, MFUMU YA MAFUMU, NDI MBUYE WA AMBUYE. Ndipo ndinaona mngelo alikuima m'dzuwa; ndipo anafuula ndi mau akulu akunena ndi mbalame zonse zakuuluka pakati pa mlengalenga: Idzani kuno, sonkhanani kuphwando la Mulungu wamkulu, kuti mudzadye nyama ya mafumu, ndi nyama ya akapitao, ndi nyama ya anthu amphamvu, ndi nyama ya akavalo, ndi ya iwo akukwerapo, ndi nyama ya anthu onse, mfulu ndi akapolo, ndi ang'ono ndi akulu. Ndipo ndinaona chilombocho, ndi mafumu a dziko, ndi magulu a nkhondo ao, osonkhanidwa kuchita nkhondo pa Iye wakukwera pa kavalo, ndi gulu la nkhondo lake. pakuti maweruzo ake ali oona ndi olungama; ndipo anaweruza mkazi wachigololo wamkulu, amene anaipsa dziko ndi chigololo chake, ndipo anabwezera chilango mwazi wa akapolo ake pa dzanja lake la mkaziyo. Ndipo chinagwidwa chilombocho, ndi pamodzi nacho mneneri wonyenga amene adachita zizindikiro pamaso pake, zimene anasokeretsa nazo iwo amene adalandira lemba la chilombo, ndi iwo akulambira fano lake; iwo awiri anaponyedwa ali moyo m'nyanja yamoto yakutentha ndi sulufure: ndipo otsalawa anaphedwa ndi lupanga la Iye wakukwera pa kavalo, ndilo lotuluka m'kamwa mwake; ndipo mbalame zonse zinakhuta ndi nyama zao. Ndipo anatinso, Aleluya. Ndipo utsi wake ukwera kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 28:7

Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 35:18

Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; m'chikhamu cha anthu ndidzakulemekezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:3

Ndipo anapatsa nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, chilemekezo cha kwa Mulungu wanga; ambiri adzachiona, nadzaopa, ndipo adzakhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:12-13

Zowindira Inu Mulungu, zili pa ine, ndidzakuchitirani zoyamika. Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa, simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe? Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu m'kuunika kwa amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:1-2

Fuulirani kwa Mulungu, dziko lonse lapansi. Pakuti munatiyesera, Mulungu, munatiyenga monga ayenga siliva. Munapita nafe kuukonde; munatisenza chothodwetsa pamsana pathu. Munapititsa anthu oberekeka pamwamba pamitu pathu; tinapyola moto ndi madzi; koma munatifikitsa potitsitsimutsa. Ndidzalowa m'nyumba yanu ndi nsembe zopsereza, ndidzakuchitirani zowinda zanga, zimene inazitchula milomo yanga, ndinazinena pakamwa panga posautsika ine. Ndidzakufukizirani nsembe zopsereza zonona, pamodzi ndi chofukiza cha mphongo za nkhosa; ndidzakonza ng'ombe pamodzi ndi mbuzi. Idzani, imvani, inu nonse akuopa Mulungu, ndipo ndidzafotokozera zonse anazichitira moyo wanga. Ndinamfuulira Iye pakamwa panga, ndipo ndinamkuza ndi lilime langa. Ndikadasekera zopanda pake m'mtima mwanga, Ambuye sakadamvera. Koma Mulungu anamvadi; anamvera mau a pemphero langa. Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:6-8

Inu munandigwiriziza kuyambira ndisanabadwe, kuyambira pa thupi la mai wanga wondichitira zokoma ndinu; ndidzakulemekezani kosalekeza. Ndikhala chodabwitsa kwa ambiri; koma Inu ndinu pothawira panga polimba. M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu, ndi ulemu wanu tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:6

Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:22

Ndipo apereke nsembe zachiyamiko, nafotokozere ntchito zake ndi kufuula mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:10-12

Ntchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova; ndi okondedwa anu adzakulemekezani. Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu, adzalankhulira mphamvu yanu. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake, ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:2

Ndidzalemekeza Yehova m'moyo mwanga; ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:12-13

Yerusalemu, lemekezani Yehova; Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu. Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu: Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 38:20

Yehova ndiye wondipulumutsa ine; Chifukwa chake tidzaimba nyimbo zanga, ndi zoimba zazingwe Masiku onse a moyo wathu m'nyumba ya Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:21

anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:16

Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:13-14

Ndipo dzidzidzi panali pamodzi ndi mngeloyo ambirimbiri a gulu la Kumwamba, natamanda Mulungu, nanena, Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba, ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:8

Mwa ichi alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale chipatso chambiri; ndipo mudzakhala ophunzira anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:33-36

Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka! Pakuti anadziwitsa ndani mtima wake wa Ambuye? Kapena anakhala mphungu wake ndani? Ndipo anayamba ndani kumpatsa Iye, ndipo adzambwezeranso? Chifukwa zinthu zonse zichokera kwa Iye, zichitika mwa Iye, ndi kufikira kwa Iye. Kwa Iyeyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:57

koma ayamikike Mulungu, amene atipatsa ife chigonjetso mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:24

ndipo analemekeza Mulungu mwa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:12

kuti ife amene tinakhulupirira Khristu kale tikayamikitse ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:12

ndi kuyamika Atate, amene anatiyeneretsa ife kulandirana nao cholowa cha oyera mtima m'kuunika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:12

Ndi kuti, Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga, pakati pa Mpingo ndidzakuimbirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:11

akalankhula wina, alankhule ngati manenedwe a Mulungu; wina akatumikira, achite ngati mu mphamvu imene Mulungu ampatsa, kuti m'zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu, amene ali nao ulemerero ndi mphamvu kunthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:171-172

Milomo yanga itulutse chilemekezo; popeza mundiphunzitsa malemba anu. Lilime langa liimbire mau anu; pakuti malamulo anu onse ndiwo olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:4-5

Mafumu onse a pa dziko lapansi adzakuyamikani, Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu. Ndipo adzaimbira njira za Yehova; pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:21

Pakamwa panga padzanena chilemekezo cha Yehova; ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lake loyera kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 150:6

Zonse zakupuma zilemekeze Yehova. Aleluya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:30

Ndipo pamene anaimba nyimbo, anatuluka kunka kuphiri la Azitona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:68-69

Wolemekezeka Ambuye, Mulungu wa Israele; chifukwa Iye anayang'ana, nachitira anthu ake chiombolo. Ndipo Iye anatikwezera ife nyanga ya chipulumutso, mwa fuko la Davide mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 19:37

Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake pa phiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau akulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamuyaya, Wamkulu ndi Wamphamvu, Inu nokha ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu wonse! Atate Woyera, ndikubwera kwa Inu ndi chiyamiko choti mwandilola kukutamandani ndi kukulambirani tsiku lililonse la moyo wanga. Ndikukupemphani kuti mulimbikitse utumiki uliwonse wotamanda ndi kulambira, kubweretsa mphamvu yatsopano m'miyoyo ya oimba ndi olambira a Ufumu wanu, kuti tsiku lililonse akhale ndi moyo wodzipereka kwa Inu. Awathandizeni kumvetsetsa kuti kulambira kwabwino kwambiri kumachokera mu mtima wodzichepetsa womwe umadziwa ukulu wanu, sikuti kungoimba kapena kusewera chida, koma kukhala ndi moyo wogwirizana ndi zimene akuimba. Ngakhale pakati pa zolakwa, zofooka ndi mayesero, awathandizeni kuzindikira kuti tsiku ndi tsiku akufunikira mphamvu zanu ndi kukhalapo kwanu kuti akupatseni kulambira koona mzimu ndi m'choonadi. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa