Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


68 Mau a m'Baibulo Okhudza Udani

68 Mau a m'Baibulo Okhudza Udani

Kodi munayamba mwaganizirapo kufunika kwa anzathu pa moyo wathu? Nthawi zambiri sitimawayamikira mokwanira kapena kuzindikira kufunika kwawo. M’Mawu a Mulungu muli mavesi ambiri okhudza ubwenzi, monga Yohane 15:13, “Palibe aliyense wokonda kwambiri kuposa uyu, amene anapereka moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.” N’kosavuta kudzitcha mnzanu, koma kukhala mnzanu ndi mayeso amene tiyenera kupambana tsiku lililonse.

Monga abwenzi, tingamve chisoni ndi kulimbikitsana, makamaka pamene akuvutika omwe timawakondadi. Abwenzi enieni amakhoza kumvetsa ndi kugawana mavuto, malingaliro, ndi zosangalatsa, popanda kuweruza.

Muli ndi mphamvu yosankha omwe mukufuna kukhala nawo papafupi, choncho dzizungulirani ndi anthu abwino, omwe amakulandirani momwe mulili, popanda kufuna kusintha umunthu wanu. Ayenera kukhala anthu amene amakuyandikitsani kwa Mulungu, amene amakuthandizani kukwaniritsa cholinga chanu, ndi kukulimbikitsani popanda nsanje.

Muyenera kukhala otsimikiza kuti mudzakhala nawo nthawi yabwino, komanso pamene zinthu sizikuyenda bwino, chifukwa pamenepo ndi pamene chikondi chenicheni chimaonekera. Khalani okhulupirika ku zimene Malemba amaphunzitsa ndipo mudzasangalala ndi nthawi zabwino. Kondani mnzanu nthawi zonse, ndipo adzakhala ngati mbale wanu nthawi ya mavuto (Miyambo 17:17).




Ezekieli 25:15

“Mau a Ine Ambuye Chauta ndi aŵa: Afilisti adalanga anthu anga mwankhanza ndi kuŵalipsira ndi mtima wonyoza ndi wofuna kuŵaononga malinga ndi chidani chao chachikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-20

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa, Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai. kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:33

Musadzinyenge. “Paja kuyanjana ndi anthu ochimwa kumaononga khalidwe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:28

Munthu woipa mtima amafalitsa mkangano, kazitape amadanitsa anthu okhala pa chibwenzibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:9

Wokhululukira cholakwa amafunafuna chikondi, koma wosunga nkhani kukhosi amapha chibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:43-44

“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Ukonde mnzako, ndi kudana ndi mdani wako.’ Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti muzikonda adani anu ndipo muziŵapempherera amene amakuzunzani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:15

Iye adathetsa Malamulo a Mose pamodzi ndi malangizo ake ndi miyambo yake. Adachita zimenezi kuti kuchokera ku mitundu iŵiri ija, alenge mtundu umodzi watsopano, wokhala mwa Iye, kuti choncho adzetse mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:17

Kunyumba kwa mnzako uzipitako kamodzikamodzi, kuwopa kuti angatope nawe, nkuyamba kudana nawe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:10

Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la atate ako. Usachite kupita ku nyumba ya mbale wake, ukakhala pa mavuto. Mnzako wokhala naye pafupi amaposa mbale wako wokhala kutali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 133:1

Ati kukoma ndi kukondweretsa ati, anthu akakhala amodzi mwaubale!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 26:21

Antchito a Isaki aja adakumba chitsime china, ndipo padaukanso mkangano wina pa za chitsime chimenecho. Motero adachitcha Chidani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:18

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:31-32

Muchotseretu pakati panu kuzondana, kukalipa, ndiponso kupsa mtima. Musachitenso chiwawa, kapena kulankhula mau achipongwe, tayani kuipa konse. Muzikomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, ndipo muzikhululukirana monga momwe Mulungu mwa Khristu adakukhululukirani inunso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:9

Kukhala aŵiri nkwabwino koposa kukhala wekha, chifukwa ntchito ya anthu aŵiri ili ndi phindu lopambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:26

Munthu wochita zabwino amatsogolera anzake pa njira yokhoza, koma njira ya munthu woipa imaŵasokeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:12

Nkotheka kuti munthu apambane mnzake amene ali yekha, koma pakakhala aŵiri, iwoŵa adzalimbana naye. Chingwe cha nkhosi zitatu sichidukirapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Chidani chimautsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:11

Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kulankhula zabwino, adzakhala bwenzi la mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:17

Usamakondwerera kugwa kwa mdani wako, mtima wako usamasangalala iyeyo akaphunthwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:9

Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzaŵatcha ana ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:7

Inu okondedwa, tizikondana, pakuti chikondi nchochokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi, ndi mwana wa Mulungu, ndipo amadziŵa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:8

Mau otsiriza ndi aŵa: nonse mukhale a mtima umodzi, ndi omverana chisoni. Muzikondana nawo abale. Mukhale a mtima wachifundo ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:27-28

“Koma inu amene mukumva mau anga, ndikukuuzani kuti, Muzikonda adani anu, muziŵachitira zabwino amene amadana nanu. Muziŵafunira madalitso amene amakutembererani, muziŵapempherera amene amakuvutitsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:10

Ife tinali adani a Mulungu, koma imfa ya Mwana wake idatiyanjanitsa ndi Iye. Tsono popeza kuti imfa ya Khristu idatiyanjanitsa ndi Mulungu, nanji tsono moyo wake, ndiye udzatipulumutsa kwenikweni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:21-22

Kale inu munali kutali ndi Mulungu, ndipo munkadana naye m'maganizo anu ndi m'ntchito zanu zoipa. Koma tsopano, kudzera mwa imfa ya Mwana wake m'thupi lake, Mulungu wakuyanjanitsaninso ndi Iye mwini. Adachita zimenezi kuti pamaso pake muthe kuwoneka muli oyera mtima, opanda banga kapena cholakwa chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:20

Wina akamanena kuti, “Ndimakonda Mulungu”, komabe nkumadana ndi mbale wake, ndi wonama ameneyo. Pakuti munthu wosakonda mbale wake amene wamuwona, sangathe kukonda Mulungu amene sadamuwone.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:7

Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Chauta, ngakhale adani ake omwe amakhala naye mwamtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:14-16

Khristu mwini wake ndiye mtendere wathu. Iye adasandutsa Ayuda ndi anthu a mitundu ina kuti akhale amodzi. Pakupereka thupi lake, adagamula khoma la chidani limene linkatilekanitsa. Iye adathetsa Malamulo a Mose pamodzi ndi malangizo ake ndi miyambo yake. Adachita zimenezi kuti kuchokera ku mitundu iŵiri ija, alenge mtundu umodzi watsopano, wokhala mwa Iye, kuti choncho adzetse mtendere. Khristu adafa pa mtanda kuti athetse chidani, ndipo kuti mwa mtandawo aphatikize pamodzi m'thupi limodzi mitundu iŵiriyo, ndi kuiyanjanitsa ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:7

Anthu oika mtima pa khalidwe lokonda zoipa, amadana ndi Mulungu. Anthu otere sagonjera Malamulo a Mulungu, ndipo kunena zoona, sangathedi kuŵagonjera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:21-22

Mdani wako akakhala ndi njala, umpatse chakudya, akamva ludzu, umpatse madzi akumwa. Potero udzamchititsa manyazi aakulu, ndipo Chauta adzakupatsa mphotho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa, Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai. kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko, dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:9

Anthu okuchitani choipa, osaŵabwezera choipa, okuchitani chipongwe osaŵabwezera chipongwe. Koma inu muziŵadalitsa, pakuti inuyo Mulungu adakuitanirani mkhalidwe wotere, kuti mulandire madalitso ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19-20

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.” Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa. Koma makamaka, monga mau a Mulungu akunenera, “Ngati mdani wako wamva njala, iwe umpatse chakudya. Ngati wamva ludzu, iwe umpatse madzi akumwa. Ukatero udzamchititsa manyazi kwambiri.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza. Chikondi chilibe matama kapena chipongwe, sichidzikonda, sichikwiya, sichisunga mangaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:20-21

Mnzanga adatambasula dzanja lake kuti amenye abwenzi ake, adaphwanya chipangano chake. Mau ake anali osalala kupambana batala, komabe mumtima mwake munali zankhondo. Mau ake anali ofeŵa kupambana mafuta, komabe anali ndi malupanga osololasolola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:18

Munthu wopsa mtima msanga amautsa mkangano, koma munthu woleza mtima amabweretsa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:15

Aliyense wodana ndi mnzake, ndi wopha anthu. Ndipo mukudziŵa kuti aliyense wopha anthu, alibe moyo wosatha mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:10

Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:34

Yesu adati, “Atate, muŵakhululukire anthuŵa, chifukwa sakudziŵa zimene akuchita.” Iwo aja adagaŵana zovala zake pakuchita maere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:12

Paja sitikulimbana ndi anthu chabetu ai. Tikulimbana ndi maufumu, aulamuliro ndi mphamvu za dziko lino lapansi lamdima, ndiponso ndi mizimu yoipa yamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:14-15

Yesetsani kukhala ndi mtendere ndi anthu onse, ndi kukhala oyera mtima, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe amene adzaona Ambuye popanda kuyera mtimako. Chenjerani kuti wina aliyense asabwerere m'mbuyo nkutaya madalitso a Mulungu. Chenjerani kuti wina aliyense asakhale ngati muzu woŵaŵa, umene umaphuka nkuvuta ena ambiri ndi ululu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:4-5

M'malo mwa chikondi changa, iwo amandibwezera zondineneza, ngakhale pamene ndikuŵapempherera. Motero amandibwezera zoipa m'malo mwa zabwino, amandiwonetsa chidani m'malo mwa chikondi changa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:11

Tsono abale, kondwani. Mverani zimene ndikukulangizani, ndipo mukonze zimene zidalakwika. Muzimvana ndi kukhala mu mtendere. Pamenepo Mulungu wachikondi ndi wamtendere adzakhala nanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:1

Abale, wina akagwa m'tchimo lililonse, inu amene Mzimu Woyera amakutsogolerani, mumthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe ndi zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:23-24

Uzikana matsutsano opusa ndi opanda nzeru, paja ukudziŵa kuti zotere zimautsa mikangano. Ndipo mtumiki wa Ambuye asamakhala wokanganakangana ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa onse, mphunzitsi wokhoza, munthu wodziŵa kupirira mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:1

Nchifukwa chake tayani choipa chonse, kunyenga konse, chiphamaso, kaduka ndi masinjiriro onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 3:3-5

Pajatu kale ifenso tinali opusa, osamvera, ndi osokezedwa. Tinali akapolo a zilakolako zoipa ndi zisangalatso zamitundumitundu. Masiku onse tinkakhalira kuchita zoipa ndi kaduka, anthu kudana nafe, ndipo ife tomwe kumadana. Koma pamenepo Mulungu Mpulumutsi wathu adaonetsa kukoma kwake ndiponso chifundo chokonda anthu. Choncho adatipulumutsa osati chifukwa cha ntchito zolungama zimene ife tidaachita, koma mwa chifundo chake pakutisambitsa. Adatisambitsa mwa Mzimu Woyera pakutibadwitsa kwatsopano ndi kutipatsa moyo watsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:3-4

Musamachita kanthu ndi mtima wodzikonda, kapena wodzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa, ndipo aliyense aziwona anzake kuti ngomuposa iyeyo. Chifukwa cha kugwira ntchito ya Khristu, iyeyu adaali pafupifupi kufa. Adaadzipereka osaopa ngakhale kutaya moyo wake kuti azindithandiza pa zimene inu simudathe kukwaniritsa pondithandiza. Musamangofuna zokomera inu nokha, koma zokomeranso anzanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 18:29

adamuwopabe kwambiri ndi kudana naye moyo wake wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:22

Usamanena kuti, “Ndidzabwezera choipa ndine.” Udikire Chauta, ndipo adzakuthandiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 18:21-22

Pamenepo Petro adadzafunsa Yesu kuti, “Ambuye, kodi mbale wanga atamandichimwira, ndidzamkhululukire kangati? Kodi ndidzachite kufikitsa kasanunkaŵiri?” Yesu adamuyankha kuti, “Kodi ndikuti kasanunkaŵiri kokha ngati, iyai, koma mpaka kasanunkaŵiri kuchulukitsa ndi makumi asanu ndi aŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:4-5

“Ukaona ng'ombe ya mdani wako ikusokera, kapena bulu wake, utenge ukampatse. Bulu wa mdani wako akagwa ndi katundu, usabzole ndi kumsiya, koma umthandize kuti adzuke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:5-6

Mulungu amene amapatsa anthu mphamvu zoti athe kupirira naŵalimbitsa mtima, akuthandizeni kumvana bwino, motsata chitsanzo cha Khristu Yesu, akuthandizeni kuti ndi mtima umodzi, nonse pamodzi mulemekeze Mulungu ndi Atate a Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma wofulumira kupsa mtima amaonetsa uchitsiru wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 7:4-5

kubwezera choipa bwenzi langa, kapena kumulanda zinthu mdani wanga popanda chifukwa, mdaniyo andithamangitse ndi kundigwira, andipondereze pansi ndi kundipha, andisiye ndili thasa m'fumbi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:9

Munthu akamati ali m'kuŵala, komabe nkumadana ndi mnzake, akali mu mdima ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:24-25

Munthu wachidani pakamwa pake pamalankhula zabwino, pamene mumtima mwake muli zonyenga. Woteroyo akamalankhula mokometsa mau, usamkhulupirire, pakuti mumtima mwake mwadzaza zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:17-18

Ndikukupemphani abale, chenjera nawoni anthu amene amapatutsa anzao naŵachimwitsa. Iwo amaphunzitsa zosiyana ndi zimene inu mudaphunzira. Muziŵalewa, pakuti anthu otere satumikira Khristu Ambuye athu, koma amangotumikira zilakolako zao basi. Ndi mau okoma ndi oshashalika amanyenga anthu a mitima yoona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:18

“Ngati anthu odalira zapansipano adana nanu, kumbukirani kuti adadana ndi Ine asanadane nanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:18-19

Wochita zonsezi ndi Mulungu, amene mwa Khristu adatiyanjanitsa ndi Iye mwini, ndipo adatipatsa ntchito yolalikira anthu chiyanjanitsocho. Ndiye kuti mwa Khristu Mulungu ankayanjanitsa anthu a pa dziko lonse lapansi ndi Iye mwini, osaŵaŵerengera machimo ao. Ndipo adatipatsa ifeyo mau onena za chiyanjanitsocho kuti tiŵalalike.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:8

Chachikulu nchakuti muzikondana mosafookera, popeza kuti chikondi chimaphimba machimo ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:10

Abale, ndikukupemphani m'dzina la Ambuye athu Yesu Khristu, kuti muzivomerezana pa zimene munena. Pasakhale kupatulana pakati panu, koma muzimvana kwenikweni pokhala a mtima umodzi ndi a maganizo amodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:2-3

Muzikhala odzichepetsa, ofatsa ndi opirira nthaŵi zonse. Muzilezerana mtima mwachikondi, Koma umu si m'mene inu mudaphunzirira za Khristu ai, ngatitu mudamva za Iyeyo, ngatinso mudaphunzitsidwa za Iye, motsata choona chimene chili mwa Yesu. Mudaphunzira kuti muleke mayendedwe anu akale, muvule moyo wanu wakale uja umene unkadziwononga ndi zilakolako zake zonyenga. Mtima wanu, umene uli gwero la maganizo anu, usanduke watsopano. Ndipo muvale moyo watsopano, umene Mulungu adaulenga, wofanafana naye. Apo mudzakhala olungama ndi oyera mtima kwenikweni. Tsono lekani kunama. Aliyense azilankhula zoona zokhazokha ndi mkhristu mnzake, pakuti tonse pamodzi mogwirizana ndife ziwalo za thupi la Khristu. Inde mwina nkupsa mtima, koma musachimwe, ndipo musalole kuti dzuŵa likuloŵereni muli chikwiyire. Musampatse mpata Satana woti akugwetseni. Amene ankaba, asabenso, koma makamaka azigwira ntchito kolimba ndi kumachita zolungama ndi manja ake, kuti akhale nkanthu kopatsa osoŵa. M'kamwa mwanu musatuluke mau aliwonse oipa, koma muzinena mau okhaokha abwino ndi olimbitsa mtima monga kungafunikire, kuti mupindulitse anzanu omva mau anuwo. ndipo muziyesetsa kusunga umodzi mwa Mzimu Woyera pa kulunzana mu mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 28:3

Musandichotsere kumodzi ndi anthu oipa, anthu amene amachita zonyenga, amene amalankhula zamtendere ndi anzao, koma mitima yao ndi yodzaza ndi chidani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:14-15

“Ndithu ngati mukhululukira anthu machimo ao, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani inunso. Koma ngati simukhululukira anthu machimo ao, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wakumwamba, ulemerero ndi ulemu zikhale zako! Ndikukuthokozani chifukwa cha miyoyo ya anzanga ndi abale anga m'chikhulupiriro. Mawu anu amati: “Wobisa cholakwa afunafuna chikondi; koma wowulula nkhani alekanitsa mabwenzi.” Ndithangateni ine monga mnzanga ndi m'bale, ndikhale wanzeru polankhula, kuti ndisadetsedwe ndi ena, ndipo potero ndivulaze ndi kuwapweteka ndi mawu ndi machitidwe anga. Ndithangateni kuti ndisunge umboni wanga monga mnzanga ndi m'bale, ndipo ndisakhale chokhumudwitsa kwa iwo. Mawu anu amati: “Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe abwino.” Ambuye sungani makutu anga, maganizo anga ndi mtima wanga, kuti ndisatengeke ndi chilichonse mwa izi, limbitsani ubale wa chiyanjano ndi ubale pakati pathu. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa