Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


54 Mauthenga a Mulungu Okhudza Mabwenzi Oipa

54 Mauthenga a Mulungu Okhudza Mabwenzi Oipa

Munthu amene mumayenda naye amakukhudzani, kaya bwino kaya moyipa. Ndipo lemba la Miyambo 13:20 limati: “Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru, koma mnzawo wa zitsiru adzaphwanyidwa.”

Mabwenzi oipa amakubweretserani mavuto ambiri, nthawi zonse mumakhala ngati mukupereka zambiri kuposa zomwe mukupeza, ndipo mumakhala osasangalala. Zimakhala ngati mukuzungulira mu bwalo la mavuto basi.

M’Malemba Opatulika muli nkhani zambiri zokhudza mabwenzi oipa. Mwachitsanzo, Aisiraeli atayandikira Dziko Lolonjezedwa, Yehova anawachenjeza kuti asayanjane ndi anthu a m’dzikomo komanso kuti asamapembedze milungu yachilendo.

M’moyo wanu mumapeza machenjezo nthawi zonse okhudza zinthu zomwe simuyenera kuchita, zomwe sizingakupindulitseni. Ndikofunika kuti mumvere machenjezo amenewa, chifukwa mudzapulumutsa moyo wanu ku mavuto aakulu amene amabwera chifukwa cha kusamvera.

Pali anthu ena amene angadzitche kuti ndi mabwenzi anu, koma ngati akukutulutsani m’malamulo a Mulungu, akhoza kukutsogolerani ku imfa mosavuta. Yesu sakufunirani zimenezo. Choncho, mupemphe Mulungu kuti akuwongolereni ndiponso kuti chifuniro chake chichitike m’moyo wanu.

Mupemphere Mulungu kuti akupezeni mabwenzi abwino. Ndikukutsimikizirani kuti adzayankha pemphero lanu, ndipo adzakuthandizani kusiya mabwenzi oipa amene akukutsogolerani ku zoipa ndi chiwerewere.




Yakobo 4:4

Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 1:1

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Yohane 1:10-11

Wina aliyense akadza kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamlandire m'nyumba mwanu. Musampatse ndi moni womwe, pakuti wopatsa munthu wotere moni, akuvomereza zochita zake zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:7

Usayandikirepo pamene pali chitsiru, paja pamenepo supezapo mau anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:24-25

Usachite naye chibwenzi munthu wopsa mtima msanga, ndipo usamayenda naye munthu waukali, kuwopa kuti ungadzaphunzireko mayendedwe ake, ndi kukodwa mu msampha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:15

Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Woyenda ndi anthu anzeru nayenso amakhala ndi nzeru, koma woyenda ndi zitsiru adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:11

Koma ndidaakulemberani kuti musamayanjane ndi munthu amene amati ndi mkhristu, pamene chikhalirecho ndi munthu wadama, kapena waumbombo, wopembedza mafano, waugogodi, chidakwa, kapena wachifwamba. Munthu wotere musamadye naye nkomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:24

Pali abwenzi ena amene chibwenzi chao nchachiphamaso chabe, koma pali ena amene amakukangamira koposa mbale yemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:33

Musadzinyenge. “Paja kuyanjana ndi anthu ochimwa kumaononga khalidwe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:28

Munthu woipa mtima amafalitsa mkangano, kazitape amadanitsa anthu okhala pa chibwenzibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 1:2

Ukungolira usiku wonse, misozi ikungoti mbwembwembwe pamasaya pake. Mwa onse amene ankaukonda, palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala woti aziwusangalatsa. Abwenzi ake onse auchita zaupandu, onse asanduka adani ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:9

Wokhululukira cholakwa amafunafuna chikondi, koma wosunga nkhani kukhosi amapha chibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:6

Abale, tsopano tikukulamulani m'dzina la Ambuye Yesu Khristu kuti muziŵapewa abale onse a makhalidwe aulesi, osafuna kutsata mwambo umene tidaŵapatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:6

Amene amakukonda, ngakhale akupweteke, chikondi chake chimakhalapobe, mdani wako ngakhale akumpsompsone, nkunyenga chabe kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 3:10-11

Munthu woyambitsa mipatuko, utamdzudzula kaŵiri konse, usakhale nayenso nkanthu. Paja ukudziŵa kuti munthu wotere ngwosokonezeka ndipo ngwochimwa. Mwini wake yemwe amadziimba mlandu yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:32

Paja Chauta amanyansidwa ndi munthu woipa, koma olungama okha amayanjana nawo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:29

Munthu wandeu amakopa mnzake, ndipo amamuyendetsa m'njira yoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:4

Chuma chimachulukitsa abwenzi atsopano, koma wosauka abwenzi ake amamthaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:19

Wolima m'munda mwake adzakhala ndi chakudya chambiri, koma wonka nafuna zopanda pake adzasauka kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 19:2

Koma mneneri Yehu, mwana wa Hanani, adatuluka kuti akumane naye, ndipo adafunsa mfumu Yehosafati kuti, “Kodi ndi bwino kuŵathandiza anthu oipa amene amadana ndi Chauta? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Chauta ulikudza kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:115

Chokereni inu, anthu ochita zoipanu, kuti ine ndizitsata malamulo a Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:4-5

Sindikhala pamodzi ndi anthu onyenga, sindiyenda ndi anthu achiphamaso. Ndimadana ndi anthu ochita zoipa, sindikhala pamodzi ndi anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:14-15

Ngati wina aliyense akana kumvera mau amene talemba m'kalatayi, mumuwonetsetse ameneyo, ndipo musayanjane naye, kuti choncho achite manyazi. Koma musamuwone ngati mdani. Makamaka mumchenjeze ngati mbale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:1

Usamachitira nsanje anthu ochimwa, kapena kumalakalaka kuti uzimvana nawo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 9:18

Nzeru nzabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amatha kuwononga zabwino zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:26

Munthu wochita zabwino amatsogolera anzake pa njira yokhoza, koma njira ya munthu woipa imaŵasokeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 1:1-3

Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu, koma wokondwerera kumvera malamulo a Chauta, nkumasinkhasinkha za malamulowo usana ndi usiku. Munthuyo ali ngati mtengo wobzalidwa m'mbali mwa mtsinje wa madzi, ngati mtengo wobereka zipatso pa nthaŵi yake, umene masamba ake safota konse. Zochita zake zonse zimamuyendera bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:11

Musayanjane nawo anthu ochita zopanda pake za mdima, koma muŵatsutse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 6:14

Musamagwirizana ndi anthu akunja, monga ngati kuti iwo ndi inu mumafanana. Nanga kulungama kungagwirizane bwanji ndi kusalungama? Kapena kuŵala kungayanjane bwanji ndi mdima?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:19-22

Ndikadakonda kuti muwononge anthu oipa, Inu Mulungu, ndipo kuti anthu okhetsa magazi andichokere. Inu mumadziŵa pamene ndikhala pansi, pamenenso ndidzuka, mumazindikira maganizo anga muli kutali. Anthuwo amakunenani zinthu zoipa, namakuukirani ndi mtima woipa. Kodi sindidana nawo anthu odana nanu, Inu Chauta? Kodi sindinyansidwa nawo anthu okuukirani? Ndimadana nawo ndi chidani chenicheni. Ndimaŵayesa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:9

Chofufumitsira chapang'ono chabe chimafufumitsa buledi yense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:7-9

Munkathamanga bwino lomwe. Tsono adakuletsani ndani kuti musamverenso choona? Kukopeka kwanu kumeneku sikuchokera kwa Mulungu amene amakuitanani. Chofufumitsira chapang'ono chabe chimafufumitsa buledi yense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:17

Chitsulo amachinola nchitsulo chinzake, chonchonso munthu amasulidwa ndi munthu mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8

Khalani odziletsa, khalani maso. Mdani wanu Satana amakhala akuyenda uku ndi uku ngati mkango wobangula, kufunafuna woti amudye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:15-17

Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye. Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi. Ndipotu dziko lapansi likupita, pamodzi ndi zake zonse zimene anthu amazilakalaka. Koma munthu wochita zimene Mulungu afuna, amakhalapo mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:17-18

Ndikukupemphani abale, chenjera nawoni anthu amene amapatutsa anzao naŵachimwitsa. Iwo amaphunzitsa zosiyana ndi zimene inu mudaphunzira. Muziŵalewa, pakuti anthu otere satumikira Khristu Ambuye athu, koma amangotumikira zilakolako zao basi. Ndi mau okoma ndi oshashalika amanyenga anthu a mitima yoona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:11-12

Koma iwe, munthu wa Mulungu, uzipewe zonsezi. Uzikhala ndi mtima wofunafuna chilungamo, wolemekeza Mulungu, wokhulupirika, wachikondi, wolimbika ndi wofatsa. Uzimenya nkhondo yabwino ya kusunga chikhulupiriro, mpaka ukalandire moyo wosatha. Paja Mulungu adakuitanira zimenezi, ndipo udavomera bwino chikhulupiriro chako pamaso pa mboni zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 1:10-15

Mwana wanga, anthu oipa akafuna kukukopa, usamaŵamvera. Adzati, “Tiye kuno, tikabisale kuti tiphe anthu, tiye tikalalire anthu osalakwa. Tiyeni tiŵameze amoyo ngati manda, tiŵameze athunthu ngati anthu otsikira ku manda. Motero tidzapata zinthu zambiri zamtengowapatali, nyumba zathu tidzazidzaza ndi zofunkha. Tiye uloŵe m'gulu lathu, chuma chathu tidzagaŵana tonse.” Mwana wanga, usamayenda nawo anthu amenewo, usatsagane nawo pa njira yaoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:9

Munthu woyenda mwaungwiro, amayenda mosatekeseka. Koma woyenda njira zoipa, adzadziŵika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:20

Uzimvera malangizo ndi kuvomera mwambo, kuti ukhale ndi nzeru m'tsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:4

Anthu akunja amadabwa tsopano poona kuti mwaleka kuthamangira nao zoipitsitsa zimene iwo amachita mosadziletsa konse. Nchifukwa chake amalalata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:15

“Chenjera nawoni aneneri onyenga. Amadza kwa inu ali ndi maonekedwe ofatsa ngati nkhosa, koma m'kati mwao ndi mimbulu yolusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:12

Wonyada sakonda kumdzudzula, sapitako kwa anthu anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:19

Kukhulupirira munthu wosakhulupirika pa nthaŵi yamavuto kuli ngati kudya ndi dzino loŵaŵa, kapena kuyenda ndi mwendo wothyoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:27

Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mau opatsa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:1

Abale, wina akagwa m'tchimo lililonse, inu amene Mzimu Woyera amakutsogolerani, mumthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe ndi zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:22

Uthaŵe zilakolako zoipa zachinyamata. Pamodzi ndi anthu onse otama Ambuye mopemba ndi mtima woyera, uzifunafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:4

Ndidzakhala kutali ndi anthu a mtima woipa, sindidzalola choipa chilichonse kuloŵa mwa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:2

Muzifunafuna za Kumwamba, osati zapansipano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:29-32

Mitima yao idadzaza ndi zosalungama zamitundumitundu, monga kuipa, umbombo ndi dumbo. Amangolingalira za kaduka, za kupha anthu, za ndeu, za kunyenga, ndi za njiru. Amachita ugogodi, Umasimba za Mwana wake, Yesu Ambuye athu. Poyang'anira umunthu wake, kholo lake ndi Davide, amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao. Ndi opusa, osakhulupirika, okhakhala moyo, ndi opanda chifundo. Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:17

Bwenzi lako ndiye amakukonda nthaŵi zonse, ndipo mbale wako adabadwira kuti azikuthandiza pa mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:15-16

Musamalikonde dziko lapansi kapena zinthu zapansipano. Munthu akamakonda dziko lapansi, chikondi chokonda Atate sichikhalamo mwa iye. Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wakumwamba, ngati pali chilichonse mu mtima mwanga, ndi chikhumbo chachikulu chokukondweretsani. Ndikufuna kukulemekezani ndi moyo wanga wonse ndi zisankho zanga zonse. Ndikupemphani munditeteze ku mabwenzi oipa, omwe mitima yawo ili ndi nsanje, miseche, ndi mawu otukwana; mabwenzi osamanga koma ogumula, ofuna kungobweretsa mavuto ndi mawu ndi zochita zawo. Ambuye, ndipatseni nzeru zosankhira mabwenzi abwino ndipo musalole kuti chilichonse choipa chindiipitse. Inu munati mu Mawu anu: "Munthu woipa amabweretsa ndewu, ndipo wamisala amalekanitsa mabwenzi abwino." Mzimu Woyera, ndipatseni kuzindikira kuti ndisamalire mgwirizano wa omwe ali pafupi nane. Ambuye, gwetsani ntchito yonse yoipa ndi mphamvu ya mdani yomwe ikufuna kubweretsa magawano. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa