Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -



57 Mau a Mulungu Okhudza Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu

57 Mau a Mulungu Okhudza Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu

Mukayandikira Atate, mukuyandikiranso Mwana, chifukwa onse ndi mmodzi. Kale, chifukwa cha zolakwa zathu, tinali kutali ndi Atate; mkhalowu unatilenga kutali ndi iye.

Koma chikondi chake ndi chachikulu, ndipo chifundo chake n’chosatha, moti sanafune kukhala kutali nanu, cholengedwa chake chamtengo wapatali. Chifukwa cha chikondi chake chopanda malire, anatuma Mwana wake yekha kuti adzafere inu; mwana wopanda chilema, wopanda tchimo, wangwiro.

Iye anachita izi kuti pasakhale cholepheretsa inu kukapembedza dzina lake. Kuti mukafike kwa Atate, muyenera kudzera mwa Yesu, kumuzindikira ngati Mpulumutsi wokha komanso wokwanira. Ndipo magazi ake adzakutsukani ku zoipa zanu, ndipo mudzakhala mwana wa Mulungu.

Palibe chifukwa choti musayandikire kwa iye; chophimba chachotsedwa, ndipo tsopano muli ndi ufulu wokhala osangalala ndikukonda Mlengi wanu. Musaiwale Yesu pa moyo wanu wa tsiku ndi tsiku, yamikirani nsembe yake ndipo muzimufunafuna ndi mtima wanu wonse.

Musakhale popanda chisomo chake, musachoke pafupi naye, musatembenukire chisomo chabwino chomuchitira ichi chomwe chabwera pa moyo wanu kuti mukakhale ndi moyo. Koposa zonse, kondani Mulungu ndi mtima wanu wonse, ndipo yendani naye nthawi zonse. Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi mkhalapakati mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Khristu Yesu (1 Timoteo 2:5).




Yohane 15:1

“Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndi mlimi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:15

monga momwe Atate amadziŵira Ine, nanenso nkuŵadziŵa Atatewo. Ndimatayirapo moyo wanga pa nkhosazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:31

koma anthu onse ayenera kudziŵa kuti ndimakonda Atate, nchifukwa chake ndikuchita monga Atate adandilamulira. Tiyeni, tizipita.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:38

Pajatu ndidatsika kuchokera Kumwamba kudzachita zofuna za Iye amene adandituma, osati kuti ndidzachite zofuna Ine ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:28

Ndidachokeradi kwa Atate kudza pansi pano. Tsopano ndikuchokanso pansi pano kupita kwa Atate.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 20:21

Yesu adatinso, “Mtendere ukhale nanu. Monga Atate adandituma, Inenso ndikukutumani.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:37

Onse amene Atate andipatsa, adzabwera kwa Ine. Ndipo munthu aliyense wodza kwa Ine, sindidzamkana konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:43

Ine ndidadza m'dzina la Atate anga, ndipo inu simukundilandira. Koma wina atabwera m'dzina la iye yekha, iyeyo ndiye mungamlandire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:30

Ine ndi Atate ndife amodzi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:58

Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti Abrahamu asanabadwe, Ine ndilipo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:19

Tsono Yesu adati, “Kunena zoona Ine Mwanane sindingathe kuchita kanthu pandekha. Ndimangochita zimene ndikuwona Atate anga akuchita. Zimene Atate amachita, Mwana amachitanso zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 3:22

ndipo Mzimu Woyera adatsikira pa Iye, akuwoneka ndi thupi ngati la nkhunda. Tsono kudamveka mau ochokera Kumwamba akuti, “Iwe ndiwe Mwana wanga wapamtima. Ndimakondwera nawe kwambiri.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:16

Mulungutu adaŵakonda kwambiri anthu a pa dziko lonse lapansi. Anali naye Mwana mmodzi yekha, komabe adampereka kuti aliyense wokhulupirira Iyeyo asatayike, koma akhale ndi moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:23

Atate amafuna kuti anthu onse azilemekeza Mwana, monga momwe amalemekezera Atate. Munthu amene salemekeza Mwana, salemekezanso Atate amene adamtuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:1

Pachiyambi pa zonse Iye amene amatchedwa dzina loti Mau, anali alipo kale. Anali kwa Mulungu, ndipo anali Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 1:23

“Namwali wina wosadziŵa mwamuna adzatenga pathupi nkubala mwana wamwamuna. Mwanayo adzatchedwa dzina loti Imanuele,” ndiye kuti “Mulungu ali nafe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:20

Tsiku limenelo mudzadziŵa kuti Ine ndimakhala mwa Atate, ndipo inu mumakhala mwa Ine, monga Ine ndimakhala mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:16

Simoni Petro adayankha kuti, “Inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja, Mwana wa Mulungu wamoyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 3:17

Tsono kuthamboko kudamveka mau akuti, “Uyu ndiye Mwana wanga wapamtima. Ndimakondwera naye kwambiri.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:3

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu. Ndiwo Atate a chifundo ndi otilimbitsa mtima kwathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:3

Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu akukomereni mtima ndi kukupatsani mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:10

Ngati mutsata malamulo anga, mudzakhala m'chikondi changa, monga momwe Ine ndatsatira malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala m'chikondi chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:8

“Ine ndine Woyamba ndiponso Wotsiriza,” akutero Ambuye Mulungu, Mphambe, amene alipo, amene analipo kale, amene alikudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:20

Pakuti Atate amakonda Mwana, namuwonetsa zonse zimene Iwo akuchita. Atate adzamuwonetsanso ntchito zoposa zimenezi, kuti inu muzizwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:15-16

Apo Yesu adaŵafunsa kuti, “Nanga inuyo, mumati ndine yani?” Simoni Petro adayankha kuti, “Inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja, Mwana wa Mulungu wamoyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:17

Koma Yesu adaŵauza kuti, “Atate anga akugwira ntchito mpaka tsopano, nanenso ndikugwira ntchito.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:13

Pajatu tikudikira tsiku lodala, pamene zidzachitike zimene tikuyembekeza, pamene Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu adzaonetsa ulemerero wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 24:49

Ine ndidzakutumizirani mphatso imene Atate anga adalonjeza. Koma inu bakhalani mumzinda muno mpaka mutalandira mphamvu zochokera Kumwamba.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 23:34

Yesu adati, “Atate, muŵakhululukire anthuŵa, chifukwa sakudziŵa zimene akuchita.” Iwo aja adagaŵana zovala zake pakuchita maere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:14

Wotchedwa Mau uja adasanduka munthu, nadzakhala pakati pathu. Anali wokoma mtima ndi wokhulupirika kwabasi. Ndipotu tidaona ulemerero wake, ndiye kuti ulemerero womwe Iye amalandira kwa Atate pokhala Mwana wao mmodzi yekha uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:35

Mulungu Atate amakonda Mwana wake, ndipo adaika zonse m'manja mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:49

Koma Yesu adati, “Mumandifunafuna chifukwa chiyani? Kani simumadziŵa kuti ndiyenera kupezeka m'nyumba ya Atate anga?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:2-3

Koma masiku otsiriza ano walankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Ndi mwa Iyeyu Mulungu adalenga zolengedwa zonse, namuika kuti alandire zinthu zonse ngati choloŵa chake. Iye ndiye kuŵala koonetsa ulemerero wa Mulungu, ndipo ndiye chithunzi chenicheni chosonyeza khalidwe la Mulungu. Iyeyu amachirikiza zonse ndi mau ake amphamvu. Atayeretsa mtundu wa anthu pakuŵachotsa machimo, adakakhala Kumwamba, ku dzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:44

Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene adandituma samkoka. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15-17

Khristuyo ndiye chithunzi chenicheni cha Mulungu wosaoneka. Iye ndiye Mwana wake woyamba, wolamulira zolengedwa zonse. Kudzera mwa Iye Mulungu adalenga zonse zakumwamba ndi zapansipano, zooneka ndi zosaoneka, mafumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu ena onse. Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, zonsezo adalengera Iyeyo. Iyeyo analipo zinthu zonse pakadalibe, mwa Iye zinthu zonse zimalunzana pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:15

Khristuyo ndiye chithunzi chenicheni cha Mulungu wosaoneka. Iye ndiye Mwana wake woyamba, wolamulira zolengedwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:28

Mwandimva ndikukuuzani kuti, ‘Ndikupita, koma ndidzabweranso kwa inu.’ Mukadandikonda, bwenzi mutakondwera kuti ndikupita kwa Atate, chifukwa Atate ngoposa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:4

koma poyang'anira kuyera kwake kwaumulungu, kuuka kwake kwa akufa kukutsimikiza kuti Yesuyo ndi Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:3-4

Umasimba za Mwana wake, Yesu Ambuye athu. Poyang'anira umunthu wake, kholo lake ndi Davide, amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao. Ndi opusa, osakhulupirika, okhakhala moyo, ndi opanda chifundo. Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita. koma poyang'anira kuyera kwake kwaumulungu, kuuka kwake kwa akufa kukutsimikiza kuti Yesuyo ndi Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:39

Adapita patsogolo pang'ono, nadzigwetsa choŵeramitsa nkhope pansi nkuyamba kupemphera. Adati, “Atate, ngati nkotheka, chindichokere chikho chamasautsochi. Komabe chitani zimene mukufuna Inu, osati zimene ndikufuna Ine ai.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:6

Yesu adamuyankha kuti, “Ineyo ndine njira, ndine choona ndiponso moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate ngati sadzera mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:20

Tikudziŵa kuti Mwana wa Mulungu adafika, ndipo adatipatsa nzeru kuti timdziŵe Mulungu woona. Ndipo tili mwa Mulungu woonayo, chifukwa tili mwa Mwana wake Yesu Khristu. Iyeyo ndiye Mulungu woona ndiponso moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:11-12

Umboniwo tsono ndi wakuti Mulungu adatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowo umapezeka mwa Mwana wake. Amene ali ndi Mwanayo, ali nawo moyo. Amene sali ndi Mwana wa Mulungu, alibe moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndidapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano m'thupi lino, ndi moyo wokhulupirira Mwana wa Mulungu, amene adandikonda napereka moyo wake chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:35

Mngeloyo adayankha kuti, “Mzimu Woyera adzakutsikirani, ndipo mphamvu za Mulungu Wopambanazonse zidzakuphimbani. Nchifukwa chake Mwana wodzabadwayo adzakhala Woyera, ndipo adzatchedwa Mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:18

Pamenepo ndiye Ayuda adankirankira kufuna kumupha. Ankati Yesu akuphwanya lamulo lokhudza Sabata, ndiponso ponena kuti Mulungu ndi Atate ake, ankadzilinganiza ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:6-7

Iyeyu anali ndi umulungu chikhalire, komabe sadayese kuti kulingana ndi Mulungu ndi chinthu choti achigwiritsitse. Koma adadzitsitsa kotheratu pakudzitengera umphaŵi wa kapolo, ndi kukhala munthu wonga anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife. Ulamuliro udzakhala m'manja mwake, ndipo adzamtchula dzina lake lakuti “Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, Mfumu ya Mtendere.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:25-26

Yesu adamuuza kuti, “Woukitsa anthu kwa akufa ndiponso woŵapatsa moyo ndine. Munthu wokhulupirira Ine, ngakhale afe adzakhala ndi moyo. Ndipo aliyense amene ali ndi moyo nakhulupirira Ine, sadzafa konse. Kodi ukukhulupirira zimenezi?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:15

Sitili ndi Mkulu wa ansembe woti sangathe kutimvera chifundo chifukwa cha zofooka zathu. Wathu Mkulu wa ansembe onse adayesedwa pa zonse, monga momwe ife timayesedwera, koma Iye sadachimwe konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:32

Iye sadaumire ngakhale Mwana wakewake, koma adampereka chifukwa cha ife tonse. Atatipatsa Mwana wakeyo, nanga Iye nkulephera kutipatsanso zonse mwaulere?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:12

Ndipo palibe wina aliyense amene angathe kupulumutsa anthu, pakuti pa dziko lonse lapansi palibe dzina lina limene Mulungu adapatsa anthu kuti tipulumuke nalo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:18-19

Mukudziŵa bwino chimene adakuwombola nachoni ku khalidwe lanu lachabe limene mudalandira kwa makolo anu. Sadakuwomboleni ndi ndalama zotha kuwonongeka zija, siliva kapena golide ai, adakuwombolani ndi magazi amtengowapatali a Khristu amene adakhala ngati mwanawankhosa wopanda banga kapena chilema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:3

Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu. Iye mwa chifundo chake chachikulu adatibadwitsanso pakuukitsa Yesu Khristu kwa akufa. Motero timakhulupirira molimba mtima

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:12

Pambuyo pake Yesu adalankhulanso ndi Afarisi aja, adati, “Ine ndine kuŵala kounikira anthu onse. Munthu wotsata Ine, sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuŵala kotsogolera anthu ku moyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:13

Alefa ndi Omega ndine. Ndiye kuti Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimalizo ndine.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wakumwamba, zikomo kwambiri chifukwa cha chikondi chanu chosatha ndipo mwanditulutsa mu mdima. Mwachita zinthu zazikulu pa ine, ndinu wodabwitsa ndipo nthawi zonse mumandikwana ndi ubwino wanu. Mtima wanga ukukuthokozani chifukwa cha zonse. Ndikudziwa kuti ndinu nokha njira, choonadi, ndi moyo, ndipo palibe afika kwa Atate koma kudzera mwa inu. Chonde, ndiphunzitseni kukhala nanu paubwenzi wolimba wachikondi ndi kudzipereka ngati mmene mulili ndi Atate. Zikomo Ambuye Yesu, chifukwa cha mawu anu, chifukwa mwalonjeza kuti tidzachita zinthu zazikulu m'dzina lanu. Mawu anu amati: “Tsiku limenelo mudzadziwa kuti Ine ndili mwa Atate, ndi inu muli mwa Ine, ndi Ine mwa inu.” Ambuye Yesu, zikomo pondibweretsa kwa Atate, ndithandizeni tsiku lililonse kuti ndikhale nanu paubwenzi wolimba ndi kukhala womvera ngati mmene munali kwa Atate, kuti nditsatire mawu anu ndi kukhala mmodzi ndi inu, monga inu ndi Atate muli mmodzi. Ulemerero ndi ulemu zonse zikhale kwa inu. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa