Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


115 Mauthenga a Mulungu Okhudza Satana

115 Mauthenga a Mulungu Okhudza Satana

Ndikufuna ndikuuzeni za mdani wathu, mdierekezi. M’malemba oyera, timamudziwa ngati wabodza, wodzikuza, komanso wotsutsana ndi Mulungu. Iye ndi mdani wanu ndi wanga.

Baibulo limatiuza momveka bwino za mdierekezi. Ndi mzimu wa mdima, wonyengerera, komanso woneneza. Mukumbukira nkhani ya Yesu m’chipululu? Mdierekezi anayesa kumunyengerera Yesu. Cholinga chake ndi chimodzi: kutisokoneza kuti tisatsate Mulungu, kuti miyoyo yathu itaike pangozi.

Malemba amatiuza kuti mdierekezi amabwera kudzaba, kupha, ndi kuwononga. Safuna china chilichonse koma kutiwononga ndi kutisokoneza ndi mabodza ake. Amadzibisa m’njira zosiyanasiyana, monga zilakolako zathu, mtima wadyera, ndi makhalidwe oipa. Amayesa kutipangitsa kukhulupirira kuti zoipa ndi zabwino.

Ndikukulangizani kuti muzipemphera nthawi zonse ndi kukhala maso. Mdierekezi ali ngati mkango wobangula, akufunafuna munthu woti ameze. Koma musaope! Mungathe kumutsutsa mwa mphamvu ya Mzimu Woyera. Mzimu Woyera ndiye mphamvu yanu yolimbana ndi mayesero.

Ndikudziwa kuti mdierekezi ndi wamphamvu, koma Mulungu ndi wamphamvu kwambiri. Mulungu alibe malire, ali paliponse, ndipo nthawi zonse adzakutetezani. Musalole kuti choipa chilamulire moyo wanu. Tsutsani mdierekezi, ndipo Mulungu adzakhala nanu.




1 Petro 5:8

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:11

Tavalani zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoze kuchilimika pokana machenjerero a mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:1

Ndipo njoka inali yakuchenjera yoposa zamoyo zonse za m'thengo zimene anazipanga Yehova Mulungu. Ndipo inati kwa mkaziyo, Eya! Kodi anatitu Mulungu, Usadye mitengo yonse ya m'mundamu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 1:6-7

Ndipo panali tsiku lakuti ana a Mulungu anadza kudzionetsa kwa Yehova, nadzanso Satana pakati pao. Nati Yehova kwa Satana, Ufuma kuti? Nayankha Satana kwa Yehova, nati, Kupitapita m'dziko ndi kuyendayenda m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 3:3

Koma Ambuye ali wokhulupirika amene adzakukhazikitsani inu, nadzakudikirirani kuletsa woipayo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:7

Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:1-11

Pamenepo Yesu anatengedwa ndi Mzimu kunka kuchipululu kukayesedwa ndi mdierekezi. Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Choka Satana, pakuti kwalembedwa, Ambuye Mulungu wako udzamgwadira, ndipo Iye yekhayekha udzamlambira. Pomwepo mdierekezi anamsiya Iye, ndipo onani, angelo anadza, namtumikira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:18

Ndipo anati kwa iwo, Ndinaona Satana alinkugwa ngati mphezi wochokera kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:8

iye wochita tchimo ali wochokera mwa mdierekezi, chifukwa mdierekezi amachimwa kuyambira pachiyambi. Kukachita ichi Mwana wa Mulungu adaonekera, ndiko kuti akaononge ntchito za mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:26-27

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire, ndiponso musampatse malo mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:44

Inu muli ochokera mwa atate wanu mdierekezi, ndipo zolakalaka zake za atate wanu mufuna kuchita. Iyeyu anali wambanda kuyambira pachiyambi, ndipo sanaime m'choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wake; pakuti ali wabodza, ndi atate wake wa bodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:10

Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga. Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8-9

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire: ameneyo mumkanize okhazikika m'chikhulupiriro, podziwa kuti zowawa zomwezo zilimkukwaniridwa pa abale anu ali m'dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:20

Ndipo Mulungu wa mtendere adzaphwanya Satana pansi pa mapazi anu tsopano lino. Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:13

Mwa ichi mudzitengere zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoza kuima chitsutsire pofika tsiku loipa, ndipo, mutachita zonse, mudzachilimika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:13

Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:3-4

Koma Petro anati, Ananiya, Satana anadzaza mtima wako chifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wake wa mundawo? Mulungu wa makolo athu anaukitsa Yesu, amene munamupha inu, ndi kumpachika pamtengo. Ameneyo Mulungu anamkweza ndi dzanja lake lamanja, akhale Mtsogoleri ndi Mpulumutsi, kuti apatse kwa Israele kulapa, ndi chikhululukiro cha machimo. Ndipo ife ndife mboni za zinthu izi; Mzimu Woyeranso, amene Mulungu anapatsa kwa iwo akumvera Iye. Koma m'mene anamva iwo analaswa mtima, nafuna kuwapha. Koma ananyamukapo wina pa bwalo la akulu, ndiye Mfarisi, dzina lake Gamaliele, mphunzitsi wa chilamulo, wochitidwa ulemu ndi anthu onse, nalamula kuti atumwiwo akhale kunja pang'ono. Ndipo anati kwa iwo, Amuna inu a Israele, kadzichenjerani nokha za anthu awa, chimene muti muwachitire. Pakuti asanafike masiku ano anauka Teudasi, nanena kuti ali kanthu iye mwini; amene anthu anaphatikana naye, chiwerengero chao ngati mazana anai; ndiye anaphedwa; ndi onse amene anamvera iye anamwazika, napita pachabe. Atapita ameneyo, anauka Yudasi wa ku Galileya, masiku a kulembedwa, nakopa anthu amtsate. Iyeyunso anaonongeka, ndi onse amene anamvera iye anabalalitsidwa. Ndipo tsopano ndinena ndi inu, Lekani anthu amenewa, nimuwalole akhale; pakuti ngati uphungu umene kapena ntchito iyi ichokera kwa anthu, idzapasuka; koma ngati ichokera kwa Mulungu simungathe kuwapasula; kuti kapena mungapezeke otsutsana ndi Mulungu. Pamene unali nao, sunali wako kodi? Ndipo pamene unagulitsa sunali m'manja mwako kodi? Bwanji chinalowa ichi mumtima mwako? Sunanyenga anthu, komatu Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:1-2

Ndipo Yesu, wodzala ndi Mzimu Woyera, anabwera kuchokera ku Yordani, natsogozedwa ndi Mzimu kunka kuchipululu pakuti kwalembedwa kuti, Adzalamula angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize. Ndipo, Pa manja ao adzakunyamula iwe, kuti ungagunde konse phazi lako pamwala. Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iye, Kwanenedwa, Usamuyese Ambuye Mulungu wako. Ndipo mdierekezi, m'mene adamaliza mayesero onse, analekana naye kufikira nthawi ina. Ndipo Yesu anabwera ndi mphamvu ya Mzimu ku Galileya; ndipo mbiri yake ya Iye inabuka ku dziko lonse loyandikira. Ndipo Iye anaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalemekezedwa ndi anthu onse. Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo tsiku la Sabata analowa m'sunagoge, monga anazolowera, naimiriramo kuwerenga m'kalata. Ndipo anapereka kwa Iye buku la Yesaya mneneri. Ndipo m'mene Iye adafunyulula bukulo, anapeza pomwe panalembedwa, Mzimu wa Ambuye uli pa Ine, chifukwa chake Iye anandidzoza Ine ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino: anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe, ndi akhungu kuti apenyanso, kutulutsa ndi ufulu ophwanyika, kulalikira chaka chosankhika cha Ambuye. kukayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anai. Ndipo Iye sanadye kanthu masiku awo; ndipo pamene anatha anamva njala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:15

Sindipempha kuti muwachotse iwo m'dziko lapansi, koma kuti muwasunge iwo kuletsa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:5

Musakanizana, koma ndi kuvomerezana kwanu ndiko, kwa nthawi, kuti mukadzipereke kwa kupemphera, nimukakhalenso pamodzi, kuti Satana angakuyeseni, chifukwa cha kusadziletsa kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:11-12

Tavalani zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoze kuchilimika pokana machenjerero a mdierekezi. Chifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akuchita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi auzimu a choipa m'zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 26:18

kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kuchokera kumdima, kulinga kukuunika, ndi kuchokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti alandire iwo chikhululukiro cha machimo, ndi cholowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi chikhulupiriro cha mwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 11:14

Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 12:9

Ndipo chinaponyedwa pansi chinjoka chachikulu, njoka yokalambayo, iye wotchedwa mdierekezi ndi Satana, wonyenga wa dziko lonse; chinaponyedwa pansi kudziko, ndi angelo ake anaponyedwa naye pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:2

zimene munayendamo kale, monga mwa mayendedwe a dziko lapansi lino, monga mwa mkulu wa ulamuliro wa mlengalenga, wa mzimu wakuchita tsopano mwa ana a kusamvera;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:13

amene anatilanditsa ife kuulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa m'ufumu wa Mwana wa chikondi chake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:15-16

Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye. Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:8-9

Pomwepo mdierekezi anamuka naye kuphiri lalitali, namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi, ndi ulemerero wao; nati kwa Iye, Zonse ndikupatsani Inu, ngati mudzagwa pansi ndi kundigwadira ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 13:39

ndipo mdani amene anamfesa uwu, ndiye mdierekezi: ndi kututa ndicho chimaliziro cha nthawi ya pansi pano; ndi otutawo ndiwo angelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:6

Ndipo mdierekezi anati kwa Iye, Ine ndidzapatsa Inu ulamuliro wonse umenewu ndi ulemerero wao: chifukwa unaperekedwa kwa ine; ndipo ndiupatsa kwa iye amene ndifuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 12:31

Tsopano pali kuweruza kwa dziko ili lapansi; mkulu wa dziko ili lapansi adzatayidwa kunja tsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:30

Sindidzalankhulanso zambiri ndi inu, pakuti mkulu wa dziko lapansi adza; ndipo alibe kanthu mwa Ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:14

Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:38

za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza Iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nachita zabwino, nachiritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:15

atavula maukulu ndi maulamuliro, anawaonetsera poyera, nawagonjetsera nako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:31-32

Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu; koma ndinakupempherera kuti chikhulupiriro chako chingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 2:13

Ndidziwa kumene ukhalako kuja kuli mpando wachifumu wa Satana; ndipo ugwira dzina langa, osakaniza chikhulupiriro changa, angakhale m'masiku a Antipa, mboni yanga, wokhulupirika wanga, amene anaphedwa pali inu, kuja akhalako Satana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:23

Koma Iye anapotoloka, nati kwa Petro, Pita kumbuyo kwanga, Satana iwe; ndiwe chondikhumudwitsa Ine; chifukwa sumasamalira za Mulungu, koma za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 12:12

Chifukwa chake, kondwerani, miyamba inu, ndi inu akukhala momwemo. Tsoka mtunda ndi nyanja, chifukwa mdierekezi watsikira kwa inu, wokhala nao udani waukulu, podziwa kuti kamtsalira kanthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:13

Ndipo anakhala m'chipululu masiku makumi anai woyesedwa ndi Satana; nakhala ndi zilombo, ndipo angelo anamtumikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 20:10

Ndipo mdierekezi wakuwasokeretsa anaponyedwa m'nyanja ya moto ndi sulufure, kumeneko kulinso chilombocho ndi mneneri wonyengayo; ndipo adzazunzidwa usana ndi usiku kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:17

Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazichite.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 3:6

Asakhale wophunza, kuti podzitukumula ungamgwere mlandu wa mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:19

Tidziwa kuti tili ife ochokera mwa Mulungu, ndipo dziko lonse lapansi ligona mwa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 2:10

Usaope zimene uti udzamve kuwawa; taona, mdierekezi adzaponya ena a inu m'nyumba yandende, kuti mukayesedwe; ndipo mudzakhala nacho chisautso masiku khumi. Khala wokhulupirika kufikira imfa, ndipo ndidzakupatsa iwe korona wa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 1:12

Nati Yehova kwa Satana, Taona, zonse ali nazo zikhale m'dzanja mwako; pa iye pokha usatambasula dzanja lako. Natuluka Satana pamaso pa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 3:1-2

Pamenepo anandionetsa Yoswa mkulu wa ansembe alikuima pamaso pa mthenga wa Yehova, ndi Satana alikuima pa dzanja lake lamanja, atsutsana naye. Tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, mudzaitanizana yense mnansi wake patsinde pa mpesa ndi patsinde pa mkuyu. Ndipo Yehova anati kwa Satana, Yehova akudzudzula, Satana iwe; inde Yehova amene anasankha Yerusalemu akudzudzula; uyu sindiye muuni wofumulidwa kumoto?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 14:12-15

Wagwadi kuchokera kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mbandakucha! Wagwetsedwa pansi, iwe wolefula amitundu! Ndipo iwe unati mumtima mwako, Ndidzakwera kumwamba, ndidzakweza mpando wanga wachifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pamwamba pa phiri la khamu, m'malekezero a kumpoto; ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanana ndi Wam'mwambamwamba. Koma udzatsitsidwa kunsi kumanda, ku malekezero a dzenje.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 28:12-17

Wobadwa ndi munthu iwe, kweza nyimbo ya maliro yolirira mfumu ya Tiro, nuziti kwa iye, Atero Ambuye Yehova, Wakomera muyeso ndi chizindikiro, wodzala ndi nzeru wokongola wangwiro. Unali m'Edeni, munda wa Mulungu, mwala uliwonse wa mtengo wake unali chofunda chako, sardiyo, topazi, diamondi, berulo, sohamu, ndi yaspi, safiro, nofeki, bareketi, ndi golide; malingaka ako ndi akazi ako anakutumikira tsiku lolengedwa iwe zinakonzekeratu. Unali kerubi wodzozedwa wakuphimba, ndipo ndinakuika unali pa phiri lopatulika la Mulungu, anayendayenda pakati pa miyala yamoto. Unali wangwiro m'njira zako chilengedwere iwe, mpaka chinapezeka mwa iwe chosalungama. Mwa kuchuluka kwa malonda ako anakudzaza m'kati mwako ndi chiwawa, ndipo unachimwa; chifukwa chake ndinakukankha kukuchotsa pa phiri la Mulungu; ndipo ndinakuononga, kerubi wakuphimba iwe, kukuchotsa pakati pa miyala yamoto. Unadzikuza mtima chifukwa cha kukongola kwako, waipsa nzeru zako; chifukwa cha kuwala kwako ndakugwetsa pansi, ndakuika pamaso pa mafumu, kuti akupenye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:23

koma ndiona lamulo lina m'ziwalo zanga, lilikulimbana ndi lamulo la mtima wanga, ndi kundigonjetsa kapolo wa lamulo la uchimo m'ziwalo zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 13:4

ndipo analambira chinjoka, chifukwa chinachipatsa ulamuliro chilombocho; ndipo analambira chilombo ndi kunena, Afanana ndi chilombo ndani? Ndipo akhoza ndani kugwira nkhondo nacho?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 25:41

Pomwepo Iye adzanena kwa iwo a kudzanja lamanzere, Chokani kwa Ine otembereredwa inu, kumoto wa nthawi zonse wokolezedwera mdierekezi ndi angelo ake:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:12

Ndipo za m'mbali mwa njira ndiwo anthu amene adamva; pamenepo akudza mdierekezi, nachotsa mau m'mitima yao, kuti angakhulupirire ndi kupulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:24-26

Koma Afarisi pakumva, anati, Uyu samatulutsa ziwanda koma ndi mphamvu yake ya Belezebulu, mkulu wa ziwanda. Ndipo Yesu anadziwa maganizo ao, nati kwa iwo, Ufumu uliwonse wogawanika pa wokha sukhalira kupasuka, ndi mudzi uliwonse kapena banja logawanika pa lokha silidzakhala; ndipo ngati Satana amatulutsa Satana, iye agawanika pa yekha; ndipo udzakhala bwanji ufumu wake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 4:15

Ndipo iwo ndiwo a m'mbali mwa njira mofesedwamo mau; ndipo pamene anamva, pomwepo akudza Satana nachotsa mau ofesedwa mwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:26

ndipo akadzipulumutse kumsampha wa mdierekezi, m'mene anagwidwa naye, kuchifuniro chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:27

ndiponso musampatse malo mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 4:7

Ukachita zabwino, sudzalandiridwa kodi? Ukaleka kuchita zabwino, uchimo ubwatama pakhomo: kwa iwe kudzakhala kulakalaka kwake, ndipo iwe udzamlamulira iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:20-21

Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda osati kwa Mulungu; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda. Simungathe kumwera chikho cha Ambuye, ndi chikho cha ziwanda; simungathe kulandirako kugome la Ambuye, ndi kugome la ziwanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:13-15

Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sakhoza kuyesedwa ndi zoipa, ndipo Iye mwini sayesa munthu: koma munthu aliyense ayesedwa pamene chilakolako chake cha iye mwini chimkokera, nichimnyenga. Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:27

koma kulindira kwina koopsa kwa chiweruziro, ndi kutentha kwake kwa moto wakuononga otsutsana nao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:10

Ndipo Mulungu wa chisomo chonse, amene adakuitanani kulowa ulemerero wake wosatha mwa Khristu, mutamva zowawa kanthawi, adzafikitsa inu opanda chilema mwini wake, adzakhazikitsa, adzalimbikitsa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 11:18

Ndiponso ngati Satana agawanika kudzitsutsa mwini, udzaimika bwanji ufumu wake? Popeza munena kuti nditulutsa ziwanda ndi Belezebulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 3:9

Taona, ndikupatsa ena otuluka m'sunagoge wa Satana akudzinenera okha ali Ayuda, osakhala Ayuda, komatu anama; taona, ndidzawadzetsa alambire pa mapazi ako, nazindikire kuti Ine ndakukonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:24

Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:13

Udzaponda mkango ndi mphiri; udzapondereza msona wa mkango ndi chinjoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:1-5

Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; Makala amoto awagwere; aponyedwe kumoto; m'maenje ozama, kuti asaukenso. Munthu wamlomo sadzakhazikika pa dziko lapansi; choipa chidzamsaka munthu wachiwawa kuti chimgwetse. Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu, ndi kuweruzira aumphawi. Indedi, olungama adzayamika dzina lanu; oongoka mtima adzakhala pamaso panu. amene adzipanga zoipa mumtima mwao; masiku onse amemeza nkhondo. Anola lilime lao ngati njoka; pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri. Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; kwa iwo akuti akankhe mapazi anga. Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe; anatcha ukonde m'mphepete mwa njira; ananditchera makwekwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 141:4

Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa, kuchita ntchito zoipa ndi anthu akuchita zopanda pake; ndipo ndisadye zankhuli zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:29

Kapena akhoza bwanji munthu kulowa m'banja la munthu wolimba, ndi kufunkha akatundu ake, ngati iye sayamba kumanga munthu wolimbayo? Ndipo pamenepo adzafunkha za m'banja lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:21

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:19

Masautso a wolungama mtima achuluka, koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:5

kumpereka iye wochita chotere kwa Satana, kuti lionongeke thupi, kuti mzimu upulumutsidwe m'tsiku la Ambuye Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:19

chitsiriziro chao ndicho kuonongeka, mulungu wao ndiyo mimba yao, ulemerero wao uli m'manyazi ao, amene alingirira za padziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:16

koposa zonse mutadzitengeranso chikopa cha chikhulupiriro, chimene mudzakhoza kuzima nacho mivi yonse yoyaka moto ya woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 18:18

Indetu ndinena kwa inu, Zilizonse mukazimanga pa dziko lapansi zidzakhala zomangidwa Kumwamba: ndipo zilizonse mukazimasula pa dziko lapansi, zidzakhala zomasulidwa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 2:1-3

Aphokoseranji amitundu, nalingiriranji anthu zopanda pake? Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru; langikani, oweruza inu a dziko lapansi. Tumikirani Yehova ndi mantha, ndipo kondwerani ndi chinthenthe. Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wake. Odala onse akumkhulupirira Iye. Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti, Tidule zomangira zao, titaye nsinga zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:19

Chomwecho iwo adzaopa dzina la Yehova kuchokera kumadzulo, ndi ulemerero wake kumene kutulukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati chigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 83:1-3

Mulungu musakhale chete; musakhale duu, osanena kanthu, Mulungu. amene anaonongeka ku Endori; anakhala ngati ndowe ya kumunda. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu; mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna, amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu; ngati ziputu zomka ndi mphepo. Monga moto upsereza nkhalango, ndi monga lawi liyatsa mapiri. Momwemo muwatsate ndi namondwe, nimuwaopse ndi kamvulumvulu wanu. Achititseni manyazi pankhope pao; kuti afune dzina lanu, Yehova. Achite manyazi, naopsedwe kosatha; ndipo asokonezeke, naonongeke. Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova, ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi. Pakuti taonani, adani anu aphokosera, ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu. Apangana mochenjerera pa anthu anu, nakhalira upo pa obisika anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:24

chifukwa Akhristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikulu ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 4:1

Koma Mzimu anena monenetsa, kuti m'masiku otsiriza ena adzataya chikhulupiriro, ndi kusamala mizimu yosocheretsa ndi maphunziro a ziwanda,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 2:4

Pakuti ngati Mulungu sanalekerera angelo adachimwawo, koma anawaponya kundende nawaika kumaenje a mdima, asungike akaweruzidwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yuda 1:6

Angelonso amene sanasunga chikhalidwe chao choyamba, komatu anasiya pokhala paopao, adawasunga m'ndende zosatha pansi pa mdima, kufikira chiweruziro cha tsiku lalikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31-39

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani? Iye amene sanatimana Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye? Ndani adzaneneza osankhidwa a Mulungu? Mulungu ndiye amene awayesa olungama; ndani adzawatsutsa? Khristu Yesu ndiye amene adafera, inde makamaka, ndiye amene adauka kwa akufa, amene akhalanso pa dzanja lamanja la Mulungu, amenenso atipempherera ife. Adzatisiyanitsa ndani ndi chikondi cha Khristu? Nsautso kodi, kapena kupsinjika mtima, kapena kuzunza, kapena njala, kapena usiwa, kapena zoopsa kapena lupanga kodi? Monganso kwalembedwa, Chifukwa cha Inu tilikuphedwa dzuwa lonse; tinayesedwa monga nkhosa zakupha. Koma m'zonsezi, ife tilakatu, mwa Iye amene anatikonda. Pakuti ndakopeka mtima kuti ngakhale imfa, ngakhale moyo, ngakhale angelo, ngakhale maufumu, ngakhale zinthu zilipo, ngakhale zinthu zilinkudza, ngakhale zimphamvu, ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:1

Okondedwa, musamakhulupirira mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ichokera mwa Mulungu: popeza aneneri onyenga ambiri anatuluka kulowa m'dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 2:19

Ukhulupirira iwe kuti Mulungu ali mmodzi; uchita bwino; ziwanda zikhulupiriranso, ndipo zinthunthumira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:11

ndipo musayanjane nazo ntchito za mdima zosabala kanthu, koma makamakanso muzitsutse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:18

Pakuti otere satumikira Ambuye wathu Khristu, koma mimba yao; ndipo ndi mau osalaza ndi osyasyalika asocheretsa mitima ya osalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:8

Penyani kuti pasakhale wina wakulanda inu ngati chuma, mwa kukonda nzeru kwake, ndi chinyengo chopanda pake, potsata mwambo wa anthu, potsata zoyamba za dziko lapansi, osati potsata Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:24-25

Ndi chikhulupiriro Mose, atakula msinkhu, anakana kutchedwa mwana wake wa mwana wamkazi wa Farao; nasankhula kuchitidwa zoipa pamodzi ndi anthu a Mulungu, kosati kukhala nazo zokondweretsa za zoipa nthawi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:1-2

Ndipulumutseni Mulungu; pakuti madzi afikira moyo wanga. Ndipo ndinalira pa kusala kwa moyo wanga, koma uku kunandikhalira chotonza. Ndipo chovala changa ndinayesa chiguduli, koma amandiphera mwambi. Okhala pachipata akamba za ine; ndipo oledzera andiimba. Koma ine, pemphero langa lili kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika; Mulungu, mwa chifundo chanu chachikulu, mundivomereze ndi choonadi cha chipulumutso chanu. Mundilanditse kuthope, ndisamiremo, ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama. Chigumula chisandifotsere, ndipo chakuya chisandimize; ndipo asanditsekere pakamwa pake pa dzenje. Mundiyankhe Yehova; pakuti chifundo chanu nchokoma; munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu. Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu; pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga. Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola; ndipulumutseni chifukwa cha adani anga. Mudziwa chotonza changa, ndi manyazi anga, ndi chimpepulo changa. Akundisautsa ali pamaso panu. Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo; ndalowa m'madzi ozama, ndipo chigumula chandimiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 20:2-3

Ndipo anagwira chinjoka, njoka yakaleyo, ndiye mdierekezi ndi Satana, nammanga iye zaka chikwi, namponya ku chiphompho chakuya, natsekapo, nasindikizapo chizindikiro pamwamba pake, kuti asanyengenso amitundu kufikira kudzatha zaka chikwi; patsogolo pake ayenera kumasulidwa iye kanthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 2:11

kuti asatichenjerere Satana; pakuti sitikhala osadziwa machenjerero ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:24-25

Munthu wosauka ine; adzandilanditsa ndani m'thupi la imfa iyi? Ndiyamika Mulungu, mwa Yesu Khristu Ambuye wathu. Ndipo chotero ine ndekha ndi mtimatu nditumikira chilamulo cha Mulungu; koma ndi thupi nditumikira lamulo la uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:1

Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani, inu amene Yesu Khristu anaonetsedwa pa maso panu, wopachikidwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:13

Koma anthu oipa ndi onyenga, adzaipa chiipire, kusokeretsa ndi kusokeretsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:26-27

Chifukwa chake musaopa iwo; pakuti palibe kanthu kanavundikiridwa, kamene sikadzaululidwa; kapena kanthu kobisika, kamene sikadzadziwika. Chimene ndikuuzani inu mumdima, tachinenani poyera; ndi chimene muchimva m'khutu, muchilalikire pa machindwi a nyumba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 12:11

Ndipo iwo anamlaka iye chifukwa cha mwazi wa Mwanawankhosa, ndi chifukwa cha mau a umboni wao; ndipo sanakonda moyo wao kungakhale kufikira imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:37

Koma m'zonsezi, ife tilakatu, mwa Iye amene anatikonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:1

Ndipo inu, anakupatsani moyo, pokhala munali akufa ndi zolakwa, ndi zochimwa zanu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:57

koma ayamikike Mulungu, amene atipatsa ife chigonjetso mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:30

Iye wosakhala pamodzi ndi Ine akana Ine, ndi iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwazamwaza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:16

Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse chilakolako cha thupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:13-14

Ndikulemberani, atate, popeza mwamzindikira Iye amene ali kuyambira pachiyambi. Ndikulemberani, anyamata, popeza mwamlaka woipayo. Ndakulemberani, ana, popeza mwazindikira Atate. Ndakulemberani, atate, popeza mwamzindikira Iye amene ali kuyambira pachiyambi. Ndakulemberani, anyamata, popeza muli amphamvu, ndi mau a Mulungu akhala mwa inu, ndipo mwamlaka woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:14-15

Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi; nakamasule iwo onse amene, chifukwa cha kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:115

Mundichokere ochita zoipa inu; kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:2

kukayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anai. Ndipo Iye sanadye kanthu masiku awo; ndipo pamene anatha anamva njala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:3

Ndipo woyesayo anafika nanena kwa Iye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, tauzani kuti miyala iyi isanduke mikate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuno cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:32-34

Ndipo ndinene chiyaninso? Pakuti idzandiperewera nthawi ndifotokozere za Gideoni, Baraki, Samisoni, Yefita; za Davide, ndi Samuele ndi aneneri; mene mwa chikhulupiriro anagonjetsa maufumu, anachita chilungamo, analandira malonjezano, anatseka pakamwa mikango, nazima mphamvu ya moto, napulumuka lupanga lakuthwa, analimbikitsidwa pokhala ofooka, anakula mphamvu kunkhondo, anapirikitsa magulu a nkhondo yachilendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:13

Adani a moyo wanga achite manyazi, nathawe; chotonza ndi chimpepulo zikute ondifunira choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:18

Tidziwa kuti yense wobadwa kuchokera mwa Mulungu sachimwa, koma iye wobadwa kuchokera mwa Mulungu adzisunga yekha, ndipo woipayo samkhudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:19

Taonani, ndakupatsani ulamuliro wakuponda pa njoka ndi zinkhanira, ndi pa mphamvu iliyonse ya mdaniyo; ndipo kulibe kanthu kadzakuipsani konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:12

Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wavomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wathu wodala ndi wamphamvu zonse, dzina lanu likwezekedwe nthawi zonse, muyi inu ndinu Mfumu yopambana, wodzala ndi ulemerero ndi chiyero, palibe wina aliyense wofanana nanu kapena kukulimbanani nanu, dzina lanu lili pamwamba pa zonse, inu ndinu Mkango wa fuko la Yuda, mbendera yathu ndi msilikali wathu wankhondo, mwa inu tili otetezeka, chifukwa chake sitidzachita mantha ndi chilichonse chimene choipa chingatichitire, tikudziwa kuti mutilandira ndi kutiteteza mu mtendere wonse omwe mitima yathu imapeza mwa inu, Ambuye lero tikukupemphani kuti mutithandize kukaniza mdierekezi mpaka iye athawe, mutipatse zida zanu ndipo musatisiye tigwere m'mayesero ake ndi zitonzo zake, mutithandize kuima olimba pamaso pa ziwembu zake ndi kumukumbutsa nthawi zonse kuti iye ndi mdani woagonjetsedwa chifukwa Khristu adamgonjetsa pa Mtanda wa pa Gologota, chifukwa chake, tikulengeza kuti ndife opambana kwambiri kudzera mwa iye amene anatikonda ndipo mdierekezi alibe kanthu mwa ife, nthawi ino tikudzudzula chiwembu chilichonse cha mdima m'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa