Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


105 Mau a Mulungu Pa Chilungamo Chake

105 Mau a Mulungu Pa Chilungamo Chake

Ndikufuna tikambirane za chilungamo cha Mulungu chomwe ndi chofunika kwambiri pa moyo wathu. Tangoganizani, Mulungu ndi wolungama kwambiri mwa Iye mwini. Chilungamo Chake chikutionetsa kuti Iye ndi woyera ndipo sakonda zoyipa.

M’buku la Aroma 2:6-10, Baibulo limatiuza kuti Mulungu adzatipatsa mphoto malinga ndi zochita zathu. Amene amachita zabwino adzalandira moyo wosatha, koma amene amachita zoyipa adzalandira mkwiyo wa Mulungu. Izi zikutanthauza kuti pali chilango kwa ochita zoyipa ndi madalitso kwa ochita zabwino, kaya ndi Myuda kapena Mkhristu.

Chilungamo cha Mulungu chikusonyeza kuti Iye ndi ndani. Ndikukhulupirira kuti kuganizira izi kungatithandize kukhala moyo woyera ndi wokondweretsa Mulungu.




Masalimo 50:6

Zamumlengalenga zikulalika chilungamo cha Mulungu, pakuti Iye mwini ndiye muweruzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:37

“Musamaweruza anthu ena kuti ngolakwa, ndipo Mulungu sadzakuweruzani. Musamaimba ena mlandu, ndipo Mulungu sadzakuimbani mlandu. Muzikhululukira ena, ndipo Mulungu adzakukhululukirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:17

Ndiye ine ndidayamba kulingalira kuti, “Mulungu adzaŵaweruza onse, abwino ndi oipa omwe, pakuti adaika nthaŵi yochitikira chinthu chilichonse ndiponso ntchito iliyonse.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:5

Iye amachita zolungama ndi kuweruza mosakondera. Amaonetsa chikondi chosasinthika pa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:8

“Ine Chauta ndimakonda chilungamo, ndimadana ndi zakuba ndi zoipa. Anthu anga ndidzaŵapatsa mphotho mokhulupirika, ndidzapangana nawo chipangano chosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 37:23

Mphambe sitingathe kumufika pafupi, ndi woopsa pa ulamuliro ndi pa mphamvu. Ndi wolungamadi kwambiri, sangazunze anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:28

Chauta amakonda chilungamo, sadzaŵasiya okha anthu ake okhulupirika. Iye adzawasunga mpaka muyaya, koma adzaononga ana a anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:12

Ndimadziŵa kuti Inu Chauta mumateteza ozunzika, mumaweruza mwachilungamo anthu osoŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 10:18

Amateteza ana amasiye ndi akazi amasiye. Amakonda anthu achilendo amene amakhala pakati panu, ndipo amaŵapatsa chakudya ndi zovala zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:28

Musamaŵaopa amene amapha thupi, koma mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m'Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:1

Munthu aliyense azimvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sudachokere kwa Mulungu. Ndipo olamulira amene alipo, adaŵaika ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 9:8

Pamenepo Chauta adalamula Mose ndi Aroni kuti, “Tapaniko phulusa lapamoto. Tsono Mose awaze phulusalo kumwamba pamaso pa Farao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:18

Komabe Chauta akufunitsitsa kuti akukomereni mtima. Ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo, chifukwa Chauta ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:4

Chauta ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama, ndi Mulungu wokhulupirika ndi wosaipa konse, wachilungamo ndi wosalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:14

Maziko a ufumu wanu ndiwo kulungama ndi kuweruza mosakondera. Mumaonetsa chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika pa zonse zimene mumachita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 6:8

Iyai, Chauta adakuwonetsa kale, munthu iwe, chimene chili chabwino. Zimene akufuna kuti uzichita ndi izi: uzichita zolungama, uzikhala wachifundo, ndipo uziyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:7-8

Koma Chauta amakhala pa mpando wake waufumu nthaŵi zonse, adakhazika mpando wake kuti aziweruza. Iye amaweruza dziko lapansi molungama, amagamula milandu ya anthu mosakondera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:6

Iye adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:3-4

Inu tetezani anthu ofooka ndi amasiye mwachilungamo. Weruzani molungama ozunzika ndi amphaŵi. “Landitsani ofooka ndi osoŵa. Apulumutseni kwa anthu oipa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:15

Chilungamo chikachitika, nzika zabwino zimakondwera, koma zimadederetsa atambwali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:7-9

Amachitira anthu opsinjidwa zolungama, amaŵapatsa chakudya anthu anjala. Chauta amamasula am'ndende. Chauta amatsekula maso a anthu osapenya, Chauta amakweza anthu otsitsidwa. Chauta amakonda anthu ochita chilungamo. Chauta amateteza alendo, amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye. Koma njira za anthu oipa amazipotoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:30

Paja tikumdziŵa kale amene adati, “Kulipsira nkwanga, ndidzakhaulitsa ndine.” Adatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:160

mau anu ndi oona okhaokha, malangizo anu onse olungama ngamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 1:6

Paja Mulungu mwa chilungamo chake, adzaŵalanga ndi masautso anthu amene amakusautsani inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:6

Chauta amaweruza mwachilungamo onse opsinjidwa amaŵachitira zolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:1-2

Inu Mulungu, patsaniko mfumu nzeru zoweruzira, patsaniko mwana wa mfumu mtima wokonda chilungamo. Mafumu a ku Tarisisi ndi akuzilumba adzaipatsa mitulo, mafumu a ku Sheba ndi a ku Seba adzabwera ndi mphatso. Mafumu onse adzaigwadira ndipo mitundu yonse ya anthu idzaitumikira. Ndithu iyo idzalanditsa anthu osoŵa amene amaiitana, idzapulumutsa anthu osauka ndiponso opanda woŵathandiza. Idzamvera chisoni anthu ofooka ndi osoŵa, ndipo idzapulumutsa moyo wa anthu aumphaŵi. Idzaombola moyo wao kwa anthu oŵapsinja ndi kwa oŵachita zankhanza, pakuti magazi ao ndi amtengowapatali pamaso pake. Ikhale ndi moyo wautali! Golide wa ku Sheba apatsidwe kwa mfumuyo. Anthu aipempherere nthaŵi zonse, aipemphere madalitso kosalekeza. M'dziko mukhale chakudya chambiri, pamwambanso pa mapiri pakhale dzinthu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni, anthu ake achuluke m'mizindamo ngati udzu wakuthengo. Dzina lake lisaiŵalike konse, mbiri yake ikhalepobe monga momwe limakhalira dzuŵa. Anthu alandire madalitso chifukwa cha iyo, a mitundu yonse aitche yodala. Atamandike Chauta, Mulungu wa Israele. Iye yekha ndiye amene amachita zinthu zodabwitsa. Dzina lake laulemerero litamandike mpaka muyaya. Ulemerero wake udzaze dziko lonse lapansi. Inde momwemo. Inde momwemo. Motero mfumuyo idzaweruza anthu anu molungama ndiponso anthu anu osauka mosakondera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:26

Ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira aŵakomere mtima, koma munthu amamuweruza molungama ndi Chauta yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:1

Chauta akuti, “Nayu mtumiki wanga amene ndimamchirikiza, amene ndamsankhula, amene ndimakondwera naye. Ndaika Mzimu wanga mwa iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:6

Adzaonetsa poyera kusalakwa kwako, ndipo kulungama kwako kudzaŵala ngati usana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:2

Mitambo ndi mdima waukulu zamzinga Chauta. Amalamulira molungama, mu ufumu wake mulibe tsankho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:6-7

“Ngati mmodzi mwa anthu ako osauka aimbidwa mlandu, umuweruze molungama ndithu. Ulewe zabodza, zosinjirira. Usaphe munthu wosalakwa ndi wosapalamula, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 10:1-2

Tsoka kwa amene amapanga malamulo opanda chilungamo, ndi kwa alembi amene amalemba zongovutitsa anzao. Ine ndidakantha mafumu a anthu opembedza mafano, amene mafano ao ndi aakulu kupambana a ku Yerusalemu ndi a ku Samariya. Ndiye ndingalephere kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake omwe, monga momwe ndidachitira Samariya ndi mafano ake?” Ambuye atamaliza ntchito yao yolanga onse pa phiri la Ziyoni ndiponso ku Yerusalemu, adzalanganso mfumu ya ku Asiriya, chifukwa cha kudzitama kwake ndi kunyada kwake. Pakuti mfumuyo ikuti, “Ndachita zimenezi ndi mphamvu zanga ndiponso ndi nzeru zanga, pakuti kumvetsa nkwanga. Ndachotsa malire a mitundu ya anthu, ndipo ndafunkha chuma chao. Ndaŵatsitsa amene anali pa mipando yaufumu. Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu, monga momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame. Monga momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, ndimo m'mene Ine ndidasonkhanitsira dziko lonse lapansi. Ndipo panalibe mbalame ndi imodzi yomwe yoti mapiko phephere-phephere, kapena yoti kukamwa yasa kapena yolira kuti psepsepse.” Koma Chauta akuti: “Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana munthu woigwiritsa ntchito? Kodi sowo ingathe kudzikuza kupambana munthu woigwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti mkwapulo ukuzunguza munthu, kapena ndodo yanyamula munthu!” Nchifukwa chake Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse, adzatumiza matenda oondetsa kwa ankhondo amphamvu a mfumu ya ku Asiriya. Ndipo mfumuyo kunyada kwake kudzapsa ndi moto wosazimika. Mulungu, Kuŵala kwa Israele, adzakhala ngati moto. Mulungu, Woyera Uja wa Israele, adzakhala ngati malaŵi a moto. Motowo udzaŵatentha ndi kuŵapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi. Adzaononga nkhalango yaikulu ndi nthaka yachonde. Zidzaonongeka m'kati ndi kunja kwake, ndipo zidzakhala ngati munthu wodwala amene akuwonda. Mitengo yotsalira yam'nkhalangomo idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe nkuiŵerenga. Pakutero amapotoza malamulo poweruza amphaŵi mosalungama. Amaŵalanda zoŵayenerera anthu anga osauka, amafunkha za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:2-3

Inu mukuti, “Pa nthaŵi imene ndiisankhule, ndidzaweruza mwachilungamo. Pamene dziko lapansi likugwedezeka pamodzi ndi zonse zokhalamo, ndine amene ndimachirikiza mizati yake.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 8:3

Kodi Mulungu amapotoza kuweruza kwake? Kodi Mphambe amalephera kuchita zachilungamo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:5

Chifukwa choti osauka alandidwa zao ndipo osoŵa akudandaula, Chauta akunena kuti, “Ndichitapo kanthu tsopano, ndiŵapulumutsa monga momwe akufuniramo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 16:5

Pamenepo mpando wachifumu udzakhazikitsidwa mwachikondi, mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata zachilungamo, ndipo adzalimbikira kuchita zaungwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Aisraele inu, aliyense mwa inu ndidzamuweruza molingana ndi ntchito zake. Lapani, tembenukani mtima, kuti machimo anu asakuwonongeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:15

Woweruza munthu woipa mtima kuti ndi wosalakwa, amanyansa Chauta, nayenso wopasa mlandu munthu wosalakwa amaipira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:17

Chauta ndi wolungama m'zochita zake zonse, ndi wachifundo pa zonse zimene achita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:9

Mtima wanga wonse umalakalaka Inu usiku, mzimu wanga m'kati mwa ine umakufunafunani. Pamene muweruza dziko lapansi, anthu onse okhalamo amaphunzira chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:6

Ngodala anthu amene akumva njala ndi ludzu lofuna chilungamo, pakuti Mulungu adzakwaniritsa zofuna zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 67:4

Mitundu ya anthu isangalale ndi kuimba ndi chimwemwe, chifukwa Inu mumaweruza anthu mwachilungamo, ndi kuŵatsogolera pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7

Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:26

Koma tsopano wapereka Yesu pofuna kutsimikiza chilungamo chake, kuti anthu adziŵe kuti Iye mwini ngwolungama, adziŵenso kuti aliyense wokhulupirira Yesu amapezeka kuti ngwolungama pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 11:7

Paja Chauta ndi wolungama, amakonda ntchito zolungama, ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:8-9

Ukamaona anthu osauka akuzunzika m'dziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzao ndi kuŵalanda ufulu wao mwankhanza, usadabwe nazo zimenezo. Paja woyang'anira wokulapo ali naye wina wamkulu kwambiri amene amamuyang'anira. Ndipo palinso akuluakulu enanso oyang'anira iwowo. Alimi onse amatengako dzinthu dzam'minda, koma ndi mfumu yokha imene imaona phindu lake la mindayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:15

Chilungamo chidzaŵabwereranso kwa anthu ake, ndipo onse oongoka mtima adzachitsata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:9

Chauta amateteza alendo, amachirikiza mkazi wamasiye ndiponso mwana wamasiye. Koma njira za anthu oipa amazipotoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:14-15

Kuweruza kolungama kwalekeka, ndipo kuchita zaungwiro kwaiŵalika. Zoona sizikupezekanso m'mabwalo a milandu, ndipo chilungamo sichikutha kupezeka kumeneko. Zoona zikusoŵa kumeneko, ndipo wina aliyense akapanda kuchita nawo zoipa, amapeza mavuto.” Chauta adaziwona zimenezi ndipo zidamunyansa kuti palibe chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:10-12

Tsono iwe, ukuweruziranji mbale wako? Kapena iwe winawe, ukunyozeranji mbale wako? Tonsefe tidzaima pamaso pa Mulungu kuti atiweruze. Paja Malembo akunena kuti, “Ambuye akuti, ‘Pali Ine ndemwe, anthu onse adzandigwadira ndi kuvomereza kuti ndine Mulungu.’ ” Motero aliyense mwa ife adzadzifotokozera yekha kwa Mulungu zimene adazichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:16

Chauta wadziwulula yekha, pakuweruza molungama, koma anthu oipa akodwa mu msampha wotcha iwo omwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:3

Maso a Chauta ali ponseponse, amayang'ana oipa ndi abwino omwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:17

Phunzirani kuchita zabwino. Funafunani chilungamo, opsinjidwa muŵathandize. Tetezani ana amasiye, muŵaimirire pa milandu yao akazi amasiye.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:123

Maso anga atopa chifukwa cha kuyembekeza chipulumutso chanu, chifukwa cha kudikira kuti malonjezo anu olungama aja achitikedi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 5:24

Koma kuweruza kwanu kwangwiro kuziyenda kosalekeza ngati madzi, kulungama kwanu kukhale ngati mtsinje wosaphwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:1

Tsono woweruza enawe, kaya ndiwe yani, ulibe pozembera. Pakutitu pamene ukuweruza mnzako, ukudzitsutsa wekha, popeza kuti iweyo woweruzawe umachita zokhazokhazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 15:1-2

Inu Chauta, kodi ndani angathe kukhala m'Nyumba mwanu? Ndani angathe kukhala pa phiri lanu loyera? Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 8:12

Ngakhale kuti wochimwa amati akachita zoipa kambirimbiri, amakhalabe moyo nthaŵi yaitali, komabe ndikudziŵa kuti omvera Mulungu ndiwo amene zinthu zidzaŵayendere bwino, poti ndi amene amamlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:3

Wandituma kuti ndiŵakonzere zofunika olira a ku Ziyoni, ndiye kuti ndiŵapatse maluŵa achisangalalo m'malo mwa phulusa lachisoni, ndiŵapatse mafuta osonyeza kukondwa m'malo mwa kulira, ndiŵapatse chovala cha chikondwerero m'malo mwa kutaya mtima. Tsono adzatchedwa mitengo yamphamvu yachilungamo, yoibzala Chauta, kuti Iye mwini apezepo ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:23

“Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi a Malamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumapereka chachikhumi cha timbeu tonunkhira, ndi cha timbeu tokometsera chakudya, koma simusamala zazikulu zenizeni pa Malamulo a Mulungu, monga kuweruza molungama, kuchita zachifundo, ndi kukhala okhulupirika. Mukadayenera kuchitadi zimenezi, komabe osasiya zinazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:3

Ngodala anthu otsata malamulo a Chauta, anthu ochita zolungama nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:5

Si kwabwino pa mlandu kukondera munthu woipa, kapena kupondereza munthu wosalakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:1

Zoonadi, Mulungu ndi wabwino kwa olungama, kwa anthu oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:20

Mukonde osati china ai, koma chilungamo chokha basi, kuti mudzalandiredi dziko limene Chauta, Mulungu wanu, akukupatsani ngati choloŵa chanu, ndi kukhazikikamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:5-6

Koma ngati kuipa mtima kwathu kuwonetsa kuti Mulungu ngwolungama, tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ngwosalungama pamene atilanga? (Ndikulankhulatu monga momwe anthu ena amalankhulira). Mpang'ono pomwe. Mulungu akadakhala wosalungama, akadatha bwanji kukhala woweruza anthu onse?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 32:16-17

Pamenepo m'dziko lonse mudzakhala chilungamo, kuyambira ku chipululu mpaka ku minda yachonde. Chifukwa anthu onse akamachita zachilungamo, m'dziko mudzakhala mtendere ndi bata mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:1-2

Usamavutika ndi anthu oipa. Usamakhumbira kukhala ngati ochita zoipa, Kanthaŵi pang'ono ndipo munthu woipa sadzakhalaponso, ngakhale muyang'ane bwino pamalo pamene analiri, simudzampezapo. Koma anthu ofatsa adzalandira dziko kuti likhale lao, ndipo adzakhala pa mtendere wosaneneka. Munthu woipa amachitira upo mnzake wabwino, namamtuzulira maso mwachidani. Koma Chauta amamseka munthu woipayo, poti amaona kuti tsiku lake la kuwonongeka likubwera. Anthu oipa amasolola lupanga, ndipo amakoka mauta, kuti aphe anthu ovutika ndi osoŵa, amene amayenda molungama. Koma lupanga lao lidzalasa mitima ya eniake omwewo, ndipo mauta ao adzaŵathyokera m'manja. Nkwabwino kukhala m'chilungamo ndi kusauka, kupambana kukhala nazo zokoma zambiri zimene munthu woipa ali nazo. Pakuti Chauta adzathetsa mphamvu za anthu oipa, koma adzalimbikitsa anthu onse abwino. Chauta amasamalira moyo wa anthu angwiro, ndipo choloŵa chao chidzakhalapo mpaka muyaya. Pa nthaŵi ya mavuto sadzazunzika, pa nthaŵi yanjala, adzakhala nazo zakudya zochuluka. pakuti mosachedwa amanyala ngati udzu, ndipo amafota ngati masamba aaŵisi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:5

Anthu oipa samvetsa kuti chilungamo nchiyani, koma amene amatsata kufuna kwa Chauta amachimvetsa kwathunthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:23

Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sadabwezere chipongwe. Pamene ankazunzika, Iye sadaopseze, koma adapereka zonse kwa Mulungu amene amaweruza molungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:6

Chauta adalenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili m'menemo. Amasunga malonjezo ake nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:10

Munthu woipa mukamchitira zabwino, saphunzira zachilungamo. Amachita zoipa m'dziko lachilungamoli, ndipo amalephera kuzindikira ukulu wa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:38-39

“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Diso kulipa diso, dzino kulipa dzino.’ Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti munthu woipa osalimbana naye. Ngati munthu akumenya pa tsaya la ku dzanja lamanja, upereke linalonso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 85:10

Chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika zidzakumana. Chilungamo ndi mtendere zidzagwirizana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:16

China chimene ndidachiwona pansi pano ndi ichi: Koyenera kukhala chiweruzo chabwino, komwekonso kumapezeka kuipa mtima. Koyenera kukhala chilungamo, komwekonso kumapezeka zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:4

Ndachimwira Inu, Inu nokha, ndachita choipa pamaso panu. Motero mwakhoza ponditchula wolakwa, simudalakwe pogamula mlandu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:23

Malipiro amene uchimo umalipira ndi imfa. Koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:5

Motero musaweruziretu munthu aliyense, Ambuye asanabwere. Iwo ndiwo adzaunika pa zonse zobisika mu mdima, ndipo adzaulula maganizo a m'mitima mwa anthu. Pamenepo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko chomuyenerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:24-25

Amene amauza munthu woipa kuti, “Ndiwe wosalakwa,” anthu adzamtemberera, ndipo mitundu ya anthu idzaipidwa naye. Koma aweruzi amene amalanga anthu oipa adzapeza bwino, ndipo adzakhala ndi madalitso ambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:8

Dzambatukani, Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, popeza kuti mitundu yonse ya anthu ndi yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:5

Koma adambaya chifukwa cha machimo athu, ndipo adamtswanya chifukwa cha zoipa zathu. Chilango chimene chidamgwera iye chatipatsa ife mtendere, ndipo mabala ake atichiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 7:18

Kodi ndani ali Mulungu ngati Inu, amene amakhululukira machimo ndi kuiŵala zolakwa za anthu anu otsala? Simusunga mkwiyo mpaka muyaya, chifukwa muli ndi chikondi chosasinthika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:39-40

Chipulumutso cha anthu abwino chimachokera kwa Chauta. Chauta ndiye kothaŵirako anthuwo pa nthaŵi yamavuto. Kondwa mwa Chauta, ndipo adzakupatsa zimene mtima wako ukukhumba. Chauta amaŵathandiza ndi kuŵalanditsa. Amaŵachotsa m'manja mwa anthu oipa nkuŵapulumutsa, popeza kuti anthuwo amadalira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:9

Koma tikamavomera kuti ndife ochimwa, Mulungu amene ali wokhulupirika ndi wolungama, adzatikhululukira machimo athuwo. Adzatiyeretsa ndi kutichotsera kusalungama kwathu konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:9

Kuwopa Chauta ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Chiweruzo cha Chauta nchoona, ncholungama nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:27

Anthu osoŵa chilungamo amanyansa anthu ochita chilungamo, monga momwe anthu abwino amanyansira anthu oipa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:15

Pa moyo wanga wopandapakewu, ndaona zinthu ziŵiri izi: mwina anthu abwino amaonongeka, zabwino chichitirecho, mwinanso anthu oipa amakhala ndi moyo nthaŵi yaitali, zoipa chichitirecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:1-2

Chauta ndiye Mfumu, anthu a pa dziko lapansi akondwere, anthu onse a m'mbali mwa nyanja asangalale. Chauta amakonda anthu odana ndi zoipa. Iye amasunga moyo wa anthu ake oyera mtima. Amaŵapulumutsa kwa anthu oipa. Amaŵalira anthu amene amamumvera, ndipo anthuwo amakhaladi ndi chimwemwe. Inu ndi anthu a Chauta, kondwerani mwa iye, ndipo mumthokoze potchula dzina lake loyera. Mitambo ndi mdima waukulu zamzinga Chauta. Amalamulira molungama, mu ufumu wake mulibe tsankho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:16-17

Sambani, dziyeretseni, chotsani pamaso panga ntchito zanu zoipa. Inde, lekani kuchita zoipa. Phunzirani kuchita zabwino. Funafunani chilungamo, opsinjidwa muŵathandize. Tetezani ana amasiye, muŵaimirire pa milandu yao akazi amasiye.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 17:15

Koma ine m'kulungama kwanga ndidzaona nkhope yanu. Tsono ine nditadzuka, ndidzakondwa kotheratu poonana ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:32

Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 5:15

Muzidana ndi zoipa, muzikonda zabwino. Mukhazikitse chilungamo m'mabwalo a milandu. Mwina mwake Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse, adzakukomerani mtima inu anthu otsala a m'banja la Yosefe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 43:1

Inu Mulungu, onetsani kuti ine ndine wosalakwa, munditchinjirize pa mlandu wanga kwa anthu osasamala za Mulungu. Mundipulumutse kwa anthu onyenga ndi opanda chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:1

Muyeso wonyenga umanyansa Chauta, koma muyeso wachilungamo umamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 56:1

Chauta akuuza anthu ake kuti, “Muzichita zabwino ndi zolungama, chifukwa ndikuwombolani posachedwa, chipulumutso changa chiwoneka.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:15

Mverani nyimbo m'mahema mwa anthu a Mulungu, nyimbo zokondwerera kupambana, zakuti, “Dzanja lamanja la Chauta limagonjetsa mwamphamvu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:23

Kondani Chauta, inu nonse anthu oyera mtima. Chauta amasunga anthu okhulupirika, koma amalanga koopsa anthu odzikuza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:6-7

“Kusala koona kumene ndimafuna ndi uku: masulani maunyolo ozunzira anzanu, masulani nsinga za goli la kuweruza mokondera. Opsinjidwa muŵapatse ufulu, muthetse ukapolo uliwonse. Anthu anjala muziŵagaŵirako chakudya chanu, osoŵa pokhala muziŵapatsako malo. Mukaona wausiŵa, mpatseni chovala, musalephere kuthandiza amene ali abale anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:33

Koma inu, yambani mwafunafuna ufumu wa Mulungu ndi kumachita zimene Iye akufuna, ndipo zina zonsezi adzakupatsaninso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:16-17

Ndani amalimba mtima kuti andimenyere nkhondo ndi anthu oipa? Ndani amaimira mbali yanga, kuti alimbane ndi anthu ochita zoipa? Chauta akadapanda kundithandiza, bwenzi posachedwa nditapita ku dziko lazii.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:12

Ukanena kuti, “Ife sitidazidziŵe zimenezi,” kodi iye amene amayesa mtima, zimenezi saziwona? Kodi amene amayang'anira moyo wako sazidziŵa? Kodi sadzambwezera munthu potsata ntchito zake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:27

Tsono leka zoipa, ndipo chita zabwino, motero udzakhala pa mtendere mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:17

Chauta, Mpulumutsi wako, Woyera uja wa Israele, akunena kuti, “Ine ndine Chauta, Mulungu wako, amene ndimakuphunzitsa, kuti zinthu zikuyendere bwino. Ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuitsata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Wanga, Mpulumutsi! Lero ndikukuitanani ndi kufuna nkhope yanu kuti ndikupatseni ulemerero ndi ulemu. Atate Woyera, ndikukweza pemphero langa kwa Inu, podziwa kuti ndinu Mulungu amene amasangalala ndi chilungamo komanso kulungama. Ndikupemphani kuti mundiphunzitse kupumula ndi kuyembekezera chilungamo chanu chauzimu, mundipatse mphamvu ndi kulimba mtima kuti mtima wanga usachite zoyipa kapena kusangalala ndi mavuto a ena, chifukwadi. Mawu anu amati: "Mulungu adzaweruza wolungama ndi woipa; pakuti pali nthawi yake yochitira chilichonse." Mulungu ndinu Wolungama, mundithandize kukhulupirira ziweruzo zanu zolungama ndikuyenda molungama mogwirizana ndi mawu anu. Ndikupemphani kuti munditeteze ku adani anga, mundipulumutse ku anthu oyipa amene amandizunza, Ambuye, mundibisire mumthunzi wa mapiko anu, mundiphunzitse kuona ndi maso achifundo ndi chikhululukiro. Inu munati m'mawu anu: "Musamaweruze, ndipo simudzaweruzidwa; musamagwetse mlandu, ndipo simudzagwetsedwa mlandu; khululukirani, ndipo mudzakhululukidwa." Ambuye mundithandize kumvetsa kuti si ntchito yanga kuweruza ndi kupereka chiweruzo, koma kuti Inu ndinu Woweruza yekha. Ndikupemphaninso kuti muteteze banja langa, mpingo wanu, ndi anansi anga ndi kutichitira chilungamo nthawi zonse. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa