Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -

Masalimo 128 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero


Salimo 128
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1 Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.

2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.

4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.

5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,

6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

The Word of God in Contemporary Chichewa

Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.®

Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.®

Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.

Biblica, Inc.
Titsatireni:



Zotsatsa