Yuda INTRO1 - Buku LopatulikaMau Oyamba Kalata yolembedwa ndi mtumwi Yuda analembedwa pofuna kuwachenjeza za aphunzitsi onyenga amene amadzitcha okhulupirira. M'kalata iyi yachidule imene nkhani zake zikufanana ndi za mu Kalata yachiwiri yolembedwa ndi mtumwi Petro, ndipo wolembayo akuwalimbikitsa awerengi ake kuti “mulimbanetu chifukwa cha chikhulupiriro chapatsidwa kamodzi kwa oyera mtima”. Za mkatimu Mau oyamba 1.1-2 Khalidwe labwino, chiphunzitso, ndi mathero a aphunzitsi onyenga 1.3-16 Awalimbikitsa asunge chikhulupiriro 1.17-23 Mdalitso 1.24-25 |
Bible Society of Malawi
Bible Society of Malawi