Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 9:2 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.

Onani mutuwo

Buku Lopatulika

Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Aisraele azichita Paska pa nthaŵi yake.

Onani mutuwo



Numeri 9:2
12 Mawu Ofanana  

Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”


Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.


Pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba, obwera ku ukapolo aja anachita chikondwerero cha Paska.


Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.


“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.


Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”


Pa tsiku loyamba la Phwando la Buledi wopanda yisiti, nthawi imene mwa mwambo inali ya kupha mwana wankhosa wa Paska, ophunzira a Yesu anafunsa Iye kuti, “Mufuna tipite kuti kumene tikakonzekere kuti mukadyere Paska?”


Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe.


Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.