Numeri 4:1 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: Buku Lopatulika Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati, Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati, Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Chauta adauza Mose ndi Aroni kuti, |
Ndasankhanso Oholiabu mwana wa Ahisamaki wa fuko la Dani. Ndiponso ndapereka nzeru kwa anthu aluso motero adzagwira ntchito zonse zimene ndakulamulira kuti zichitike monga izi:
Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.
“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.