Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 21:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.

Onani mutuwo

Buku Lopatulika

Akalowa ali yekha azituluka ali yekha; akakhala ndi mkazi, mkazi wake azituluka naye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Akalowa ali yekha azituluka ali yekha; akakhala ndi mkazi, mkazi wake azituluka naye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Akakhala kuti anali yekha, adzachokanso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pobwerapo, mkazi wakeyo adzapita naye limodzi.

Onani mutuwo



Eksodo 21:3
5 Mawu Ofanana  

“Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.


Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.


“Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.


Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.