Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.
Eksodo 2:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo. Buku Lopatulika Ndipo mlongo wake anaima patali, adziwe chomwe adzamchitira. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo mlongo wake anaima patali, adziwe chomwe adzamchitira. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Ndipo mlongo wake wa mwanayo adaimirira pafupi namangopenyetsetsa, kuti aone zimene zimchitikire mwanayo. |
Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.