Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 18:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

mwana wake wamkaziyo pamodzi ndi ana ake aamuna awiri. Mose anamupatsa mwana wachisamba dzina loti Geresomu popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko lachilendo.”

Onani mutuwo

Buku Lopatulika

dzina la winayo ndiye Geresomo, pakuti anati, Ndakhala mlendo m'dziko lachilendo;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

dzina la winayo ndiye Geresomo, pakuti anati, Ndakhala mlendo m'dziko lachilendo;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yetero adabweranso ndi ana aamuna aŵiri aja a Zipora. Mwana woyamba Mose adaamutcha Geresomo (chifukwa adati, “Ndakhala mlendo m'dziko lachilendo.”)

Onani mutuwo



Eksodo 18:3
8 Mawu Ofanana  

Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.


“Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.


Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”


Kotero Mose anatenga mkazi wake ndi ana ake aamuna, ndipo anawakweza pa bulu nayamba ulendo wobwerera ku Igupto. Ndipo anatenga ndodo ya Mulungu ija mʼdzanja lake.


Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.


Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.


Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu.


Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.