Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Zekariya 2:2 - Buku Lopatulika

Ndipo ndinati, Upita kuti? Ndipo anati kwa ine, Kukayesa Yerusalemu, kuona ngati chitando chake nchotani, ndi m'litali mwake motani.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndinati, Upita kuti? Ndipo anati kwa ine, Kukayesa Yerusalemu, kuona ngati chitando chake nchotani, ndi m'litali mwake motani.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndidamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti?” Iye adandiyankha kuti, “Ndikukayesa mzinda wa Yerusalemu kuti ndidziŵe kutalika kwa muufupi mwake ndi m'litali mwake.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”

Onani mutuwo



Zekariya 2:2
10 Mawu Ofanana  

Ndipo chingwe choyesera chidzatulukanso kulunjika ku chitunda cha Garebu, ndipo chidzazungulira kunka ku Gowa.


Ndipo anamuka nane komweko, ndipo taona, panali munthu, maonekedwe ake ngati amkuwa, ndi chingwe chathonje m'dzanja lake, ndi bango loyesa nalo, naima kuchipata iye.


Ndipo dziko lake la mzindawo mulipereke la mikono zikwi zisanu kupingasa kwake, ndi mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m'litali mwake, pa mbali ya chipereko chopatulika, ndilo la nyumba yonse ya Israele.


Chifukwa chake atero Yehova: Ndabwera kudza ku Yerusalemu ndi zachifundo; nyumba yanga idzamangidwamo, atero Yehova wa makamu, ndipo adzayesa Yerusalemu ndi chingwe.


Ndipo ndinati kwa mthenga wakulankhula ndi ine, Amenewa amuka naye kuti efayo?


Koma tsopano ndimuka kwa Iye wondituma Ine; ndipo palibe wina mwa inu andifunsa Ine, Munka kuti?


Ndipo anandipatsa ine bango ngati ndodo, ndi kuti, Tanyamuka, nuyese Kachisi wa Mulungu, ndi guwa la nsembe, ndi iwo akulambiramo.