Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 7:49 - Buku Lopatulika

Koma khamu ili losadziwa chilamulo, likhala lotembereredwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma khamu ili losadziwa chilamulo, likhala lotembereredwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma anthu wambaŵa sadziŵa Malamulo a Mose; ngotembereredwa basi!”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”

Onani mutuwo



Yohane 7:49
11 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake imvani mau a Yehova, inu amuna amnyozo, olamulira anthu awa a mu Yerusalemu.


Tsoka kwa iwo amene adziyesera anzeru ndi ochenjera!


amene ati, Ima pa wekha, usadze chifupi ndi ine, pakuti ine ndili woyera kupambana iwe; amenewa ndiwo utsi m'mphuno mwanga, moto woyaka tsiku lonse.


Kodi wina wa akulu anakhulupirira Iye, kapena wa Afarisi?


Nikodemo ananena kwa iwo, amene uja adadza kwa Iye kale, ali mmodzi wa iwo,


Anayankha nati kwa iye, Wabadwa iwe konse m'zoipa, ndipo iwe utiphunzitse ife kodi? Ndipo anamtaya kunja.


Ndipo Afarisi ena akukhala ndi Iye anamva izi, nati kwa Iye, Kodi ifenso ndife osaona?